< 1 Akorinto 10 >

1 Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja.
Kangithandi-ke ukuthi lingazi, bazalwane, ukuthi bonke obaba bethu babengaphansi kweyezi, njalo bonke badabula ulwandle,
2 Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja.
futhi bonke babhabhathizwa kuMozisi eyezini lasolwandle,
3 Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu
labo bonke badla ukudla kunye komoya,
4 ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu.
futhi bonke banatha okunathwayo kunye komoya; ngoba banatha edwaleni lomoya elabalandelayo; lalelodwala lalinguKristu.
5 Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.
Kodwa ubunengi babo uNkulunkulu wayengathokozi ngabo; ngoba bachithwa enkangala.
6 Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo.
Lalezizinto zaba yizibonelo kithi, ukuze singaloyisi okubi, njengalokhu labo baloyisa.
7 Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.”
Njalo lingabi ngabakhonza izithombe, njengabanye babo; njengokulotshiweyo ukuthi: Abantu bahlala phansi ukudla lokunatha, basebesukuma ukudlala.
8 Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000.
Njalo kasingaphingi, njengabanye babo abaphingayo, basebesiwa ngasuku lunye inkulungwane ezingamatshumi amabili lantathu.
9 Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka.
Njalo asingamlingi uKristu, njengabanye babo futhi bamlinga, basebebhujiswa zinyoka.
10 Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.
Lingasoli-ke, njengabanye babo labo basola, babhujiswa ngumbhubhisi.
11 Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn g165)
Lalezizinto zonke zabehlela labo kube yizibonelo, njalo zabhalelwa ukuba yisixwayiso sethu, osekufike ukucina kwezikhathi. (aiōn g165)
12 Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe!
Ngakho lowo ocabanga ukuthi umi, kabone ukuthi kawi.
13 Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.
Kakulakulingwa okulibambileyo ngaphandle kokusebantwini; kodwa uNkulunkulu uthembekile, ongayikuvuma ukuthi lilingwe ngokungaphezu kwamandla enu, kanti kanye lesilingo uzakwenza lendlela yokuphepha, ukuze libe lamandla okusithwala.
14 Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano.
Ngakho-ke, bathandiweyo bami, balekelani ukukhonza izithombe.
15 Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi.
Ngikhuluma njengakwabahlakaniphileyo; lina yehlukanisani engikutshoyo.
16 Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu?
Inkezo yesibusiso esiyibusisayo, kayisiyo yini eyokuhlanganyela kwegazi likaKristu? Isinkwa esisihlephunayo, kayisiso yini esokuhlanganyela komzimba kaKristu?
17 Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.
Ngoba thina abanengi siyisinkwa sinye, simzimba munye; ngoba thina sonke sihlanganyela lesosinkwa sinye.
18 Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo?
Khangelani uIsrayeli ngokwenyama; abadlayo imihlatshelo kabasibo yini abahlanganyela lelathi?
19 Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse?
Ngithini pho? Ukuthi isithombe siyilutho yini? Kumbe ukuthi okuhlatshelwe izithombe kuyilutho?
20 Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo.
Kodwa ukuthi izinto abezizwe abazihlabayo, bazihlabela amadimoni, njalo kungeyisikho kuNkulunkulu; kodwa kangithandi ukuthi libe lenhlanganyelo lamadimoni.
21 Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda.
Lingenathe inkezo yeNkosi lenkezo yamadimoni; lingehlanganyele itafula leNkosi letafula lamadimoni.
22 Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?
Kumbe sizayivusela ubukhwele iNkosi? Kambe silamandla kulayo?
23 Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza.
Zonke izinto zivunyelwe kimi, kodwa kayisizo zonke izinto ezisizayo. Zonke izinto zivunyelwe kimi, kodwa kayisizo zonke izinto ezakhayo.
24 Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.
Kakungabi khona ozidingela okwakhe, kodwa ngulowo lalowo okomunye.
25 Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
Konke okuthengiswa esilaheni kudleni, lingabuzi lutho ngenxa yesazela;
26 Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”
ngoba umhlaba ungoweNkosi lokugcwala kwawo.
27 Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
Njalo uba omunye kwabangakholwayo elinxusa, njalo lithanda ukuya, dlanini konke okubekwa phambi kwenu, lingabuzi lutho ngenxa yesazela.
28 Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima.
Kodwa uba umuntu esithi kini: Lokhu kuhlatshelwe isithombe; lingadli ngenxa yalowo olitshelileyo, langenxa yesazela; ngoba umhlaba ungoweNkosi lokugcwala kwawo.
29 Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina?
Kodwa isazela ngithi, esingeyisiso esakho, kodwa esomunye; ngoba kungani inkululeko yami yahlulelwe yisazela somunye?
30 Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?
Njalo uba mina ngomusa ngihlanganyela, ngikhulunyelwani kubi ngalokho mina engikubongayo?
31 Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.
Ngakho uba lisidla, loba linatha, loba lisenzani, konke kwenzeleni udumo lukaNkulunkulu.
32 Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu.
Lingabi ngabakhubekisi lakumaJuda lakumaGriki lebandleni likaNkulunkulu;
33 Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.
njengami futhi ezintweni zonke ngithokozisa bonke, ngingadingi olwami usizo, kodwa olwabanengi, ukuze basindiswe.

< 1 Akorinto 10 >