< 1 Akorinto 1 >

1 Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.
Eu, Paulo, chamado por Deus para ser apóstolo de Jesus Cristo, junto com o nosso irmão Sóstenes, escrevemos esta carta
2 Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.
para a igreja de Deus em Corinto, para aqueles que se tornam justos em Cristo Jesus, chamados para serem santos e para todos os que louvam o Senhor Jesus Cristo, Senhor tanto deles quanto nosso, em todo o mundo.
3 Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Que a graça e a paz de Deus, nosso Pai, e do Senhor Jesus Cristo estejam com vocês.
4 Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu.
Eu sempre agradeço a Deus por vocês, por causa da graça que ele lhes deu, em Cristo Jesus.
5 Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse,
Por meio dele, vocês se tornaram ricos em tudo, em tudo o que vocês dizem e em tudo o que sabem.
6 chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu.
De fato, a mensagem sobre Cristo se provou tão válida nas suas vidas
7 Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe.
que vocês continuam a receber todos os dons espirituais, enquanto esperam pela vinda do nosso Senhor Jesus Cristo.
8 Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu.
Ele também os manterá fortes até o fim, para que vocês se mantenham justos até o dia da chegada do Senhor Jesus Cristo.
9 Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
Deus é fiel e chamou vocês para que se unam ao seu Filho, Jesus Cristo, o nosso Senhor.
10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo.
Irmãos e irmãs, eu suplico a vocês, em nome do nosso Senhor Jesus Cristo, que todos vivam em acordo e que não haja divisões entre vocês. E que, pelo contrário, sejam unidos e tenham o mesmo propósito.
11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu.
Pois ouvi coisas sobre vocês, meus irmãos e minhas irmãs, ditas por algumas pessoas da família de Cloé, de que está havendo discussões entre vocês.
12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
Deixem que eu explique o que quero dizer: Vocês andam dizendo: “Eu sigo Paulo”, ou “Eu sigo Apolo” e outro “Eu sigo Pedro”, ou “Eu sigo Cristo.”
13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo?
Será que Cristo está dividido? Por acaso, Paulo morreu preso a uma cruz por vocês? Foi em nome de Paulo que vocês foram batizados?
14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo,
Estou agradecido a Deus pelo fato de não ter batizado vocês, a não ser Crispo e Gaio.
15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa.
Pois assim, ninguém pode afirmar que foi batizado em meu nome.
16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense).
Ah, eu também batizei a família de Estéfanas; mas não consigo me lembrar de mais ninguém além desses.
17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
Pois Cristo não me enviou para batizar e, sim, para anunciar a boas novas, sem usar para isso a linguagem da sabedoria humana, para que, assim, a morte de Cristo na cruz não perdesse o seu poder.
18 Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu.
Pois a mensagem da cruz não faz sentido para aqueles que estão perdidos, mas é o poder de Deus para aqueles entre nós que estão salvos.
19 Pakuti kwalembedwa kuti, “Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru; luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
Como está escrito nas Sagradas Escrituras: “Destruirei a sabedoria dos sábios e acabarei com a inteligência dos inteligentes.”
20 Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn g165)
Onde estão os sábios, os escritores e os filósofos desta época? Porventura, Deus não transformou a sabedoria deste mundo em loucura? (aiōn g165)
21 Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira.
Pois Deus, em toda a sua sabedoria, não permitiu que as pessoas do mundo, com a sabedoria que possuem, o conhecessem. Mas, é por meio da, assim chamada, loucura do anúncio das boas novas que Deus salva aqueles que têm fé nele.
22 Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru,
Os judeus pedem por sinais milagrosos, e os gregos buscam sabedoria,
23 koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina.
mas a nossa mensagem é a de Cristo morto em uma cruz, que se mostra como uma ofensa para os judeus e como loucura para os não-judeus.
24 Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu.
No entanto, para as pessoas que são chamadas por Deus, sejam elas judias ou pagãs, Cristo é o poder e a sabedoria de Deus.
25 Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.
Pois a loucura de Deus é mais sábia do que a nossa sabedoria, e a fraqueza de Deus é mais forte do que a força humana.
26 Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero.
Irmãos e irmãs, lembrem-se de quando foram chamados. Lembrem-se de que este chamado não incluiu muitos dos que são considerados pela humanidade como sábios, poderosos ou importantes.
27 Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu.
Pelo contrário, Deus escolheu as coisas que o mundo considera loucas para humilhar as pessoas que se acham sábias. Ele escolheu o que é considerado pelo mundo como fraco para humilhar aqueles que se acham fortes.
28 Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo,
Ele escolheu coisas que o mundo não considera importantes e as quais despreza, mesmo coisas que não são importantes, para reduzir a nada as coisas que são.
29 kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu.
Assim, ninguém poderá se vangloriar diante de Deus.
30 Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso.
É por causa de Deus que vocês vivem em Cristo Jesus, dado por Deus a nós, para ser a nossa sabedoria. Ele nos torna justos e nos liberta.
31 Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
Então, como as Sagradas Escrituras dizem: “Quem quiser se orgulhar, que se orgulhe das ações do Senhor.”

< 1 Akorinto 1 >