< 1 Mbiri 9 >

1 Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
And, all Israel, registered themselves, and lo! they are written, in the Book of the Kings of Israel, and, Judah, was carried away captive to Babylon, for their faithlessness.
2 Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
Now, the first inhabitants, who were in their possessions, in their cities, were Israel, the priests, the Levites, and the Nethinim.
3 Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
And, in Jerusalem, there dwelt, of the sons of Judah, and of the sons of Benjamin, —and of the sons of Ephraim, and Manasseh:
4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
Uthai son of Ammihud, son of Omri, son of Imri, son of Bani, of the sons of Perez, son of Judah.
5 A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
And, of the Shilonites, Asaiah the firstborn, and his sons.
6 A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
And, of the sons of Zerah, Jeuel, —and their brethren, six hundred and ninety.
7 A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
And, of the sons of Benjamin, Sallu, son of Meshullam, son of Hodaviah, son of Hassenuah;
8 Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
and Ibneiah, son of Jeroham, and Elah, son of Uzzi, son of Michri, —and Meshullam, son of Shephatiah, son of Reuel, son of Ibnijah;
9 Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
and their brethren, by their generations, nine hundred and fifty-six, —all these men, were ancestral chiefs, to their ancestral house.
10 Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
And, of the priests, Jedaiah, and Jehoiarib, and Jachin, —
11 Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
and Azariah son of Hilkiah, son of Meshullam, son of Zadok, son of Meraioth, son of Ahitub, chief ruler of the house of God;
12 Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
and Adaiah, son of Jeroham, son of Pashhur, son of Malchijah, —and Maasai son of Adiel, son of Jahzerah, son of Meshullam, son of Meshillemith, son of Immer;
13 Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
and their brethren, chief men of their ancestral house, a thousand and seven hundred and sixty, —able men, for the business of the service of the house of God.
14 Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
And, of the Levites, Shemaiah, son of Hasshub, son of Azrikam, son of Hashabiah, of the sons of Merari;
15 Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
and Bakbakkar, Heresh, and Galal, —and Mattaniah, son of Mica, son of Zichri, son of Asaph;
16 Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
and Obadiah, son of Shemaiah, son of Galal, son of Jeduthun, —and Berechiah son of Asa, son of Elkanah, who dwelt in the villages of the Netophathites.
17 Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
And, the keepers of the gates, were Shallum, and Akkub, and Talmon, and Ahiman, —and their brethren—Shallum the chief;
18 Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
and, hitherto, they were in the gate of the king, eastward, —the same, were the keepers of the gate, for the camps of the sons of Levi.
19 Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
And, Shallum, son of Kore, son of Ebiasaph, son of Korah and his brethren of his ancestral house—the Korahites, were over the business of the service, watchers at the vestibule of the tent, —and, their fathers, had been over the camp of Yahweh, watchers at the entrance.
20 Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
And, Phinehas son of Eleazar, was, chief ruler, over them aforetime, Yahweh, being with him.
21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Zechariah son of Meshelemiah, was door-keeper at the entrance of the tent of meeting.
22 Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
All those who were chosen for door-keepers in the vestibule, were two hundred and twelve, —the same, in their villages, had registered themselves, the same, did David and Samuel the seer establish in their trust.
23 Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
So, they and their sons, were over the gates of the house of Yahweh, of the house of the tent, by watches.
24 Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
Towards the four winds, were the keepers of the gates, —eastward, westward, northward, and southward.
25 Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
And, their brethren in their villages, had to come in, every seven days, from time to time, along with these.
26 Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
For, in trust, were four mighty men of the keepers of the gates, the same, were Levites, —and they were over the chambers, and over the treasuries of the house of God.
27 Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
And, round about the house of God, used they to lodge, —for, upon them, was the charge, and they were over the setting open, morning by morning.
28 Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
And, some from among them, were over the utensils of the service, —for, by number, used they to bring them in, and, by number, used they to take them forth.
29 Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
And, some from among them, were appointed over the utensils, yea over all the vessels of the holy place, —and over the fine meal, and the wine, and the oil, and the frankincense, and the spices.
30 Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
And, some from among the sons of the priests, were compounders of perfumes, with the spices.
31 Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
And, Mattithiah, from among the Levites, —the same, was the firstborn of Shallum the Korahite—was in trust over the making of the flat cakes.
32 Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
And, some from among the Kohathites, of their brethren, were over the Bread that was set in Array, —to place it sabbath by sabbath.
33 Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
These, also were the singers, ancestral chiefs of the Levites, in the chambers, free, —for, by day and by night, was there [a charge] upon them, in the business.
34 Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
These, were the ancestral chiefs, of the Levites, by their generations, chief men, —these, dwelt in Jerusalem.
35 Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
And, in Gibeon, dwelt the father of Gibeon, Jeiel, —the name of whose wife, was Maacah:
36 ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
and, his firstborn son, Abdon, —and Zur, and Kish, and Baal and Ner, and Nadab;
37 Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
and Gedor, and Ahio, and Zechariah, and Mikloh.
38 Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
And, Mikloth, begat Shimeam—and, they also, over against their brethren, did dwell in Jerusalem, along with their brethren.
39 Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
And, Ner, begat Kith, and, Kish, begat Saul, —and, Saul, begat Jonathan, and Malchishua, and Abinadab, and Eshbaal;
40 Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
and, the son of Jonathan, was Merib-baal, —and, Merib-baal, begat Micah;
41 Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
and, the sons of Micah, were Pithon, and Melech, and Tahrea [and Ahaz];
42 Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
and, Ahaz, begat Jarah, and, Jarah begat Alemeth, and Azmaveth, and Zimri, —and Zimri, begat Moza;
43 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
and, Moza, begat Binea, —and Raphaiah his son, Eleasah his son, Azel his son;
44 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.
and, Azel, had six sons, and these are their names—Azrikam, [his firstborn], and Ishmael, and Sheariah and Obadiah, and Hanan, [and Asah]. These, were the sons of Azel.

< 1 Mbiri 9 >