< 1 Mbiri 9 >

1 Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
A tak všickni Izraelští sečteni byli, a aj, zapsáni jsou v knize králů Izraelských a Judských, a přeneseni jsou do Babylona pro přestoupení své.
2 Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
Ti pak, kteříž bydlili prvé v vládařství svém v městech svých, totiž Izraelští, kněží, Levítové a Netinejští,
3 Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
Bydlili v Jeruzalémě, z synů Judových, z synů Beniaminových, ano i z synů Efraimových a Manassesových:
4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
Uttai syn Amiuda, syna Amri, syna Imri, syna Bani, z synů Fáresových, syna Judova.
5 A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
A z čeledi Silonovy: Azaiáš prvorozený a synové jeho.
6 A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
A z synů Zerachových: Jehuel, a příbuzných jejich šest set a devadesát.
7 A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
Z synů pak Beniaminových: Sallu syn Mesullama, syna Hodavia, syna Hasenuova,
8 Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
A Ibneiáš syn Jerochamův, Ela syn Uzi, syna Michri, a Mesullam syn Sefatiáše, syna Rehuelova, syna Ibniášova.
9 Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
Bratří také jejich po pokoleních jejich, devět set padesáte a šest; všickni ti muži knížata čeledí po domích otců svých.
10 Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
Z kněží také Jedaiáš, Jehoiarib a Jachin,
11 Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
Azariáš syn Helkiáše, syna Mesullamova, syna Sádochova, syna Meraiotova, syna Achitobova, kníže v domě Božím.
12 Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
A Adaiáš syn Jerochama, syna Paschurova, syna Malchiášova, a Masai syn Adiele, syna Jachzery, syna Mesullamova, syna Mesillemitova, syna Immerova.
13 Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
A bratří jejich knížata po domích otců svých, tisíc sedm set a šedesát mužů udatných v práci přisluhování domu Božího.
14 Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
A z Levítů: Semaiáš syn Chasuba, syna Azrikamova, syna Chasabiášova, z synů Merari.
15 Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
A Bakbakar Cheres, a Galal, a Mataniáš syn Míchy, syna Zichri, syna Azafova.
16 Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
A Abdiáš syn Semaiáše, syna Galalova, syna Jedutunova, a Berechiáš syn Asy, syna Elkánova, kterýž přebýval ve vsech Netofatských.
17 Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
Též vrátní: Sallum a Akkub, a Talmon, Achiman, i bratří jejich, z nichž byl Sallum kníže.
18 Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
Kterýž až po dnes v bráně královské stával k východu, onino pak vrátnými byli po houfích synů Léví.
19 Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
Ale Sallum syn Chóre, syna Abiazafova, syna Chóre, a bratří jeho z domu otce jeho, Chorejští, nad pracemi přisluhování, ostříhali prahů při stánku, tak jako otcové jejich nad vojskem Hospodinovým, kteříž ostříhali vcházení.
20 Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
Nad kterýmiž Fínes syn Eleazarův byl někdy knížetem, a Hospodin byl s ním.
21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Zachariáš pak syn Meselemiášův vrátným byl u dveří stánku úmluvy.
22 Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
Všickni ti voleni za vrátné k veřejím, osob dvě stě a dvanáct. Ti ve vsech svých vyčteni jsou, kteréž nařídil David a Samuel vidoucí, pro jejich věrnost,
23 Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
Aby oni i synové jejich byli při branách domu Hospodinova, v domě stánku po strážích.
24 Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
Po čtyřech stranách byli vrátní, k východu, k západu, k půlnoci a ku poledni.
25 Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
A bratří jejich, po vsech svých bydlící, aby každého sedmého dne časy svými přicházeli s nimi.
26 Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
Nebo Levítové byli pod spravou těch čtyř předních vrátných, a byli nad komorami a nad poklady domu Božího,
27 Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
A aby vůkol domu Božího ponocovali; nebo jim poručena stráž, a otvírati každý den ráno.
28 Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
Z těch také ustaveni nad nádobami přisluhování; nebo v počtu vnášeli je, a v jistém počtu též vynášeli.
29 Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
Z nichž opět někteří postaveni byli nad nádobami jinými a nade všemi nádobami posvátnými, a nad bělí, vínem, olejem, kadidlem a vonnými věcmi.
30 Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
Někteří také synové kněžští strojili masti z těch vonných věcí.
31 Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
Matatiáš pak z Levítů, prvorozený Salluma Choritského, správcí byl těch věcí, kteréž se na pánvi smažily.
32 Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
A z synů Kahat, z bratří jejich, byli ustanoveni nad chlebem předložení, aby jej připravovali na každou sobotu.
33 Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
Z těch také byli zpěváci, přednější z čeledí otcovských mezi Levíty bydlíce, nejsouce zaměstknaní něčím jiným; nebo ve dne i v noci k své povinnosti státi musili.
34 Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
Ti jsou přední z čeledí otcovských mezi Levíty v čeledech svých, a ti přední jsouce, bydlili v Jeruzalémě.
35 Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
V Gabaon pak bydlili, otec Gabaonitských Jehiel, a jméno manželky jeho Maacha.
36 ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
Syn pak jeho prvorozený Abdon, Zur, Cis, Bál, Ner a Nádab.
37 Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
Ale Gedor, Achio, Zachariáš a Miklot,
38 Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
(Miklot pak zplodil Simam), ti také naproti bratřím svým bydlili v Jeruzalémě s bratřími svými.
39 Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
Ner pak zplodil Cisa, a Cis zplodil Saule, Saul pak zplodil Jonatu, Melchisua, Abinadaba a Ezbále.
40 Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
Syn pak Jonatův Meribbál, a Meribbál zplodil Mícha.
41 Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
Synové pak Míchovi: Piton, Melech, Tarea.
42 Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
Achaz pak zplodil Járu, Jára pak zplodil Alemeta, Azmaveta a Zimri. Zimri pak zplodil Mozu.
43 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
Moza pak zplodil Bina. Refaiáš syn jeho, Elasa syn jeho, Azel syn jeho.
44 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.
Azel pak měl šest synů, jichžto tato jsou jména: Azrikam, Bochru, Izmael, Seariáš, Abdiáš a Chanan. Ti jsou synové Azelovi.

< 1 Mbiri 9 >