< 1 Mbiri 7 >
1 Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
Des fils d'Issachar: Tola, Puah, Jashub et Shimron, quatre.
2 Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
Fils de Tola: Uzzi, Rephaja, Jeriel, Jahmaï, Ibsam et Shemuel, chefs des maisons de leurs pères, de Tola; hommes vaillants dans leurs générations. Leur nombre, du temps de David, était de vingt-deux mille six cents.
3 Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
Fils d'Uzzi: Jizrachia. Fils de Jizrachiah: Micaël, Abdias, Joël et Jischja, au nombre de cinq; tous étaient des chefs.
4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
Avec eux, selon leurs générations, selon les maisons de leurs pères, il y avait des troupes pour la guerre, au nombre de trente-six mille; car ils avaient beaucoup de femmes et de fils.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
Leurs frères, parmi toutes les familles d'Issacar, hommes vaillants, tous enregistrés selon leur généalogie, étaient quatre-vingt-sept mille.
6 Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
Fils de Benjamin: Bela, Becher et Jediael, trois.
7 Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
Fils de Béla: Ezbon, Uzzi, Uzziel, Jerimoth et Iri, cinq; chefs de maisons paternelles, vaillants hommes; ils étaient au nombre de vingt-deux mille trente-quatre par généalogie.
8 Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
Fils de Becher: Zemirah, Joas, Eliezer, Eliœnai, Omri, Jeremoth, Abijah, Anathoth et Alemeth. Tous ceux-là étaient les fils de Bécher.
9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
Ils furent classés par généalogie, selon leurs générations, chefs des maisons de leurs pères, vaillants hommes, au nombre de vingt mille deux cents.
10 Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
Fils de Jediaël: Bilhan. Fils de Bilhan: Jeush, Benjamin, Ehud, Chenaana, Zethan, Tarsis et Ahishahar.
11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
Tous ceux-là étaient fils de Jediaël, selon les chefs de famille de leurs pères, hommes vaillants, au nombre de dix-sept mille deux cents, aptes à aller à l'armée pour la guerre.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
Il en était de même de Shuppim, de Huppim, des fils de Ir, de Hushim et des fils de Aher.
13 Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
Fils de Nephtali: Jahziel, Guni, Jezer, Shallum, et les fils de Bilha.
14 Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
Fils de Manassé: Asriel, qu'a porté sa concubine l'Aramitesse. Elle enfanta Makir, père de Galaad.
15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
Machir prit une femme de Huppim et de Shuppim, dont la sœur s'appelait Maaca. Le nom de la seconde était Zelophehad; et Zelophehad eut des filles.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
Maaca, femme de Makir, enfanta un fils, qu'elle appela Peresh. Le nom de son frère était Sheresh; ses fils étaient Ulam et Rakem.
17 Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
Fils d'Ulam: Bedan. Ce sont là les fils de Galaad, fils de Makir, fils de Manassé.
18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
Sa sœur Hammolecheth enfanta Ishhod, Abiezer et Mahla.
19 Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
Les fils de Shemida furent: Ahian, Sichem, Likhi et Aniam.
20 Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
Fils d'Ephraïm: Shuthelah, Bered, son fils, Tahath, son fils, Eleada, son fils, Tahath, son fils,
21 Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
Zabad, son fils, Shuthelah, son fils, Ezer et Elead, que les hommes de Gath, nés dans le pays, tuèrent, parce qu'ils étaient descendus pour prendre leurs troupeaux.
22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
Ephraïm, leur père, fut longtemps dans le deuil, et ses frères vinrent le consoler.
23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
Il alla vers sa femme; elle conçut et enfanta un fils, qu'il appela Beriah, parce qu'il y avait du trouble dans sa maison.
24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
Sa fille était Schéérah, qui bâtit Beth Horon le bas et le haut, et Uzzen Schéérah.
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
Il eut pour fils Repha, pour fils Resheph, pour fils Telah, pour fils Tahan, pour fils
26 Ladani, Amihudi, Elisama,
Ladan, pour fils Ammihud, pour fils Elishama, pour fils
Nun, pour fils et Josué, pour fils.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
Leurs possessions et leurs établissements étaient Béthel et ses villes, à l'orient Naaran, à l'occident Guézer et ses villes, Sichem et ses villes, jusqu'à Azza et ses villes,
29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
et, sur le territoire des fils de Manassé, Beth-Shean et ses villes, Taanac et ses villes, Meguiddo et ses villes, Dor et ses villes. Les enfants de Joseph, fils d'Israël, habitèrent dans ces localités.
30 Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
Fils d'Asher: Imnah, Ishvah, Ishvi et Beriah. Sérah était leur sœur.
31 Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
Fils de Beria: Héber et Malkiel, qui fut le père de Birzaith.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
Héber engendra Japhlet, Shomer, Hotham et Shua, leur sœur.
33 Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
Fils de Japhlet: Pasach, Bimhal et Ashvath. Ce sont les fils de Japhlet.
34 Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
Fils de Shemer: Ahi, Rohga, Jehubba et Aram.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
Fils de Helem, son frère: Zopha, Imna, Shelesh et Amal.
36 Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
Fils de Zopha: Sua, Harnépher, Schual, Beri, Imrah,
37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
Bezer, Hod, Shamma, Schilsha, Ithran et Beera.
38 Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
Fils de Jéther: Jephunné, Pispa et Ara.
39 Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
Fils d'Ulla: Arach, Hanniel et Rizia.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
Tous ceux-là étaient les fils d'Aser, chefs des maisons paternelles, hommes de choix et vaillants, chefs des princes. Le nombre de ceux qui étaient inscrits sur les listes généalogiques pour servir à la guerre était de vingt-six mille hommes.