< 1 Mbiri 7 >

1 Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
Forsothe the sones of Isachar weren foure; Thola, and Phua, Jasub, and Sameron.
2 Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
The sones of Thola weren Ozi, and Raphaia, and Jerihel, and Jemay, and Jepsen, and Samuel, princis bi the housis of her kynredis. Of the generacioun of Thola, weren noumbrid strongeste men in the daies of Dauid, two and twenti thousynde and sixe hundrid.
3 Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
The sones of Ozi weren Jezraie; of whom weren borun Mychael, and Obadia, and Johel, and Jezray, fyue, alle princes.
4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
And with hem weren bi her meynees and puplis, sixe and thretti thousynde strongeste men gird to batel; for thei hadden many wyues and sones.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
And her britheren by alle the kynredis of Isachar `moost stronge to fiyte weren noumbrid foure scoore and seuene thousynde.
6 Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
The sones of Beniamyn weren Bale, and Bothor, and Adiel, thre.
7 Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
The sones of Bale weren Esbon, and Ozi, and Oziel, and Jerymoth, and Vray, fyue, princes of meynees, mooste stronge to fiyte; for the noumbre of hem was two and twenti thousynde and foure and thretti.
8 Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
Forsothe the sones of Bochor weren Samara, and Joas, and Eliezer, and Elioenai, and Zamri, and Jerimoth, and Abia, and Anathoth, and Almachan; alle these weren the sones of Bochor.
9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
Sotheli the princes of kynredis weren noumbrid bi her meynees twenti thousynde and two hundrid moost stronge men to batels.
10 Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
Forsothe the sones of Ledihel weren Balan; sotheli the sones of Balan weren Jheus, and Beniamyn, and Aoth, and Camana, and Jothan, and Tharsis, and Thasaar.
11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
Alle these the sones of Ledihel weren princes of her meynees, seuentene thousynde and two hundrid, strongeste men goynge forth to batel.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
Also Saphan and Apham weren the sones of Hir; and Basym was the sone of Aser.
13 Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
Forsothe the sones of Neptalym weren Jasiel, and Guny, and Aser, and Sellum; the sones of Bale.
14 Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
Sotheli the sone of Manasses was Esriel; and Sira his secundarie wijf childide Machir, the fadir of Galaad.
15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
And Machir took wyues to hise sones Huphyn and Suphyn; and he hadde a sister Maacha bi name; and the name of the secounde sone was Salphaath, and douytris weren borun to Salphaath.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
And Maacha, the wijf of Machir, childide a sone, and clepide his name Phares; forsothe the name of his brothir was Sares; and hise sones weren Vlam and Recem.
17 Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
Sotheli the sone of Vlam was Baldan. These weren the sones of Galaad, sone of Machir, sone of Manasses;
18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
forsothe Regma his sistir childide a feir man, Abiezer, and Mola.
19 Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
Forsothe the sones of Semyda weren Abym, and Sichem, and Liey, and Amany.
20 Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
Sotheli the sones of Effraym weren Suchaba; Bareth, his sone; Caath, his sone; Elda, his sone; and Thaath, his sone; and Zadaba, his sone;
21 Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
and Suthala, his sone; and Ezer, and Elad, his sones. Forsothe men of Geth borun in the lond killiden hem, for thei yeden doun to assaile her possessiouns.
22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
Therfor Effraym, the fadir of hem, weilide bi many daies; and hise britheren camen to coumforte hym.
23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
And he entride to his wijf, which conseyuede, and childide a sone; and he clepide his name Beria, for he was borun in the yuelis of his hows.
24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
Sotheli his douytir was Sara; that bildide Betheron, the lowere and the hiyere, and Ozen, and Sara.
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
Forsothe his sone was Rapha, and Reseph, and Thale;
26 Ladani, Amihudi, Elisama,
of whom was borun Thaan, that gendride Laodon; and Amyud, the sone of hym, gendride Elysama;
27 Nuni ndi Yoswa.
of whom was borun Nun; that hadde a sone Josue.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
Sotheli the possessioun and `dwellyng place of hem was Bethil with hise villagis, and ayens the eest, Noram; at the west coost, Gazer, and hise villagis, also Sichem with hise villagis, and Aza with hise villagis.
29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
Also bisidis the sones of Manasses, Bethsan, and hise townes, Thanach and hise townes, Maggeddo, and hise townes, Dor, and hise townes; the sones of Joseph sone of Israel dwelliden in these townes.
30 Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
The sones of Aser weren Sona, and Jesua, and Isuy, and Baria; and Sara was the sister of hem.
31 Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
Sotheli the sones of Baria weren Heber, and Melchiel; he is the fadir of Barsath.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
Sotheli Heber gendride Ephiath, and Soomer, and Otham, and Sua, the sister of hem.
33 Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
Forsothe the sones of Jephiath weren Phosech, and Camaal, and Jasoph; these weren the sones of Jephiath.
34 Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
Sotheli the sones of Soomer weren Achi, and Roaga, and Jaba, and Aram.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
Sotheli the sones of Helem, his brother, weren Supha, and Jema, and Selles, and Amal.
36 Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
The sones of Supha weren Sue, Arnapheth, and Sual, and Bery,
37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
and Jamra, and Bosor, and Ador, and Sama, and Salusa, and Jethram, and Beram.
38 Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
The sones of Ether weren Jephone, and Phaspha, and Ara.
39 Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
Sotheli the sones of Ollaa weren Areth, and Aniel, and Resia.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
Alle these weren the sones of Aser, princes of kynredis, chosun men and strongeste duykis of duykis; forsothe the noumbre, of the age of hem that weren abel to batel, was sixe and twenti thousynde.

< 1 Mbiri 7 >