< 1 Mbiri 7 >

1 Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
And the sons of Issachar were Tola and Puah, Jashub and Shimron, four.
2 Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
And the sons of Tola: Uzzi, and Rephaiah, and Jeriel, and Jahmai, and Jibsam, and Samuel, heads of their fathers' houses, of Tola, valiant men of might in their generations; their number in the days of David was twenty-two thousand six hundred.
3 Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
And the sons of Uzzi: Jizrahiah; and the sons of Jizrahiah: Michael, and Obadiah, and Joel, [and] Jishijah, five; all of them chief men.
4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
And with them by their generations, according to their fathers' houses, were military bands for war, thirty-six thousand; for they had many wives and sons.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
And their brethren among all the families of Issachar valiant men of might, registered by genealogy, in all eighty-seven thousand.
6 Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
[The sons of] Benjamin: Bela, and Becher, and Jediael, three.
7 Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
And the sons of Bela: Ezbon, and Uzzi, and Uzziel, and Jerimoth, and Iri, five; heads of fathers' houses, mighty men of valour; and they were registered by their genealogy twenty-two thousand and thirty-four.
8 Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
And the sons of Becher: Zemirah, and Joash, and Eliezer, and Elioenai, and Omri, and Jeremoth, and Abijah, and Anathoth, and Alemeth; all these were the sons of Becher.
9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
And they were registered by their genealogy by their generations, heads of their fathers' houses, mighty men of valour, twenty thousand two hundred.
10 Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
And the sons of Jediael: Bilhan; and the sons of Bilhan: Jeush, and Benjamin, and Ehud, and Chenaanah, and Zethan, and Tarshish, and Ahishahar.
11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
All these were the sons of Jediael, by the heads of their fathers, mighty men of valour, seventeen thousand two hundred, fit for service for war.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
And Shuppim, and Huppim, the children of Ir. — Hushim: the sons of Aher.
13 Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
The sons of Naphtali: Jahziel, and Guni, and Jezer, and Shallum, the sons of Bilhah.
14 Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
The sons of Manasseh: Asriel, ...whom she bore; his Syrian concubine bore Machir the father of Gilead.
15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
And Machir took a wife [the sister] of Huppim and Shuppim, and the name of their sister was Maachah. And the name of the second [son] was Zelophehad; and Zelophehad had daughters.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
And Maachah the wife of Machir bore a son, and she called his name Peresh; and the name of his brother was Sheresh; and his sons were Ulam and Rakem.
17 Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
And the sons of Ulam: Bedan. These were the sons of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh.
18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
And his sister Moleketh bore Ishhod, and Abiezer, and Mahlah.
19 Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
And the sons of Shemidah were Ahian, and Shechem, and Likhi, and Aniam.
20 Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
And the sons of Ephraim: Shuthelah, and Bered his son, and Tahath his son, and Eladah his son, and Tahath his son,
21 Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
and Zabad his son, and Shuthelah his son, and Ezer, and Elad. And the men of Gath born in the land slew them, because they came down to take their cattle.
22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
And Ephraim their father mourned many days, and his brethren came to comfort him.
23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
And he went in to his wife; and she conceived, and bore a son; and he called his name Beriah, for [he was born] when calamity was in his house.
24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
And his daughter was Sheerah; and she built Beth-horon the nether, and the upper, and Uzzen-sheerah.
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
And his son was Rephah, and Resheph, and Telah his son, and Tahan his son,
26 Ladani, Amihudi, Elisama,
Laadan his son, Ammihud his son, Elishama his son,
27 Nuni ndi Yoswa.
Nun his son, Joshua his son.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
And their possession and dwelling-places were Bethel and its dependent villages, and eastward Naaran, and westward Gezer and its dependent villages, and Shechem and its dependent villages as far as to Gazah and its dependent villages.
29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
And in the hands of the children of Manasseh, Beth-shean and its dependent villages, Taanach and its dependent villages, Megiddo and its dependent villages, Dor and its dependent villages. In these dwelt the children of Joseph the son of Israel.
30 Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
The sons of Asher: Jimnah, and Jishvah, and Jishvi, and Beriah; Serah their sister.
31 Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
And the sons of Beriah: Heber, and Malchiel, who is the father of Birzavith.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
And Heber begot Japhlet, and Shomer, and Hotham, and Shua their sister.
33 Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
And the sons of Japhlet: Pasach, and Bimhal, and Ashvath; these are the sons of Japhlet.
34 Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
And the sons of Shemer: Ahi, and Rohgah, and Hubbah, and Aram.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
And the sons of his brother Helem: Zophah, and Jimna, and Shelesh, and Amal.
36 Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
The sons of Zophah: Suah, and Harnepher, and Shual, and Beri, and Jimrah,
37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
Bezer, and Hod, and Shamma, and Shilshah, and Jithran, and Beera.
38 Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
And the sons of Jether: Jephunneh, and Pispah, and Ara.
39 Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
And the sons of Ulla: Arah, and Hanniel, and Rizia.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
All these were the sons of Asher, heads of fathers' houses, choice men, mighty of valour, chiefs of the princes. And their number according to their genealogy, registered as fit for service for war, was twenty-six thousand men.

< 1 Mbiri 7 >