< 1 Mbiri 5 >

1 Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa,
А синови Рувима, првенца Израиљевог, јер он беше првенац, али кад оскрвни постељу оца свог, дано би његово првенаштво синовима Јосифа сина Израиљевог, али не тако да се броји првенац,
2 ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe)
Јер Јуда би најсилнији међу браћом својом и од њега је вођ, али првенаштво доби Јосиф;
3 ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa: Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.
Синови Рувима, првенца Израиљевог беху: Анох и Фалуј, Есрон и Хармија,
4 Ana a Yoweli anali awa: Semaya, Gogi, Simei,
Синови Јоилови: Семаја син му, а његов син Гог, а његов син Симеј,
5 Mika, Reaya, Baala,
А његов син Миха, а његов син Реаја, а његов син Вал,
6 ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.
А његов син Веира, ког одведе Теглат-Феласар цар асирски; он беше кнез племена Рувимовог.
7 Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa: Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya,
А браћи његовој по породицама њиховим кад се избројаше по коленима својим, беше кнез Јеило и Захарија,
8 ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni.
А Вела син Азаза сина Семе сина Јоиловог; он живљаше у Ароиру и до Невона и Валмеона.
9 Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.
Потом живљаше к истоку дори до пустиње од реке Ефрата, јер им се стока умножи у земљи галадској.
10 Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.
И за времена Сауловог војеваше на Агарене, који изгибоше од руке њихове; и тако се населише у шаторима њиховим по свему источном крају земље галадске.
11 Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:
А синови Гадови живљаху према њима у земљи васанској до Салхе.
12 Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.
Јоило им беше поглавар, а Сафан други, па Јанај и Сафат у Васану.
13 Abale awo mwa mabanja awo anali awa: Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.
А браћа њихова по домовима отачким беху: Михаило и Месулам и Сева и Јорај и Јахан и Зије и Евер, седморица.
14 Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.
Ти беху синови Авихаила сина Урија сина Јароје сина Галада сина Михаила сина Јесисаја сина Јадона сина Вузовог.
15 Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.
Ахије син Авдила сина Гунијевог беше поглавар у дому отаца њихових.
16 Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.
И живљаху у Галаду, у Васану и селима његовим и у свим подграђима саронским до међа његових.
17 Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.
Сви ови бише избројани за времена Јотама, цара Јудиног и за време Јеровоама, цара Израиљевог.
18 Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo.
Синова Рувимових и Гадових и половине племена Манасијиног, храбрих људи, што ношаху штит и мач, и затезаху лук, и вештих боју, беше четрдесет и четири хиљаде и седам стотина и шездесет, који иђаху на војску;
19 Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu.
И војеваше на Агарене, на Јетуреје и Нафисеје и Нодавеје,
20 Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira.
И дође им помоћ супрот њих, и Агарени им бише дани у руке и све што имаху; јер завапише Богу у боју, и услиши их, јер се поуздаше у Њ.
21 Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000,
И запленише стоку њихову, педесет хиљада камила и двеста и педесет хиљада оваца и две хиљаде магараца и сто хиљада душа људских.
22 enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.
А рањених много паде; јер тај бој би од Бога; и наставаше на месту њиховом до сеобе своје.
23 Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.
А синови половине племена Манасијиног живљаху у тој земљи од Васана до Вал-Ермона и Сенира, до горе Ермона; беху се умножили.
24 Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo.
А ово беху поглавари у дому отаца њихових: Ефер и Јесеј и Елило и Азрило и Јеремија и Одавија и Јадило, људи храбри и на гласу поглавари у дому отаца својих.
25 Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika.
Али кад згрешише Богу отаца својих и чинише прељубу за боговима народа оне земље, које Бог истреби испред њих,
26 Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.
Подиже Бог Израиљев дух Фула, цара асирског и дух Теглат-Феласара, цара асирског, и преселише племе Рувимово и племе Гадово и половину племена Манасијиног, и одведоше их у Алу и у Авор и у Ару, и на реку Гозан, где осташе до данас.

< 1 Mbiri 5 >