< 1 Mbiri 5 >

1 Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa,
Isarel e camin teh Reuben e capanaw katang doeh. Hateiteh, a na pa e ikhun a khin sak dawkvah, camin lah a onae hah Isarel e capa Joseph e capanaw koe poe e lah ao. Hatdawkvah, setouknae dawk camin lah a onae hah pakhum e lah awm hoeh.
2 ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe)
Judah teh a hmaunawnghanaw hlak a tha a sai teh, ahni dawk hoi kaukkung a tâco. Camin lah a onae teh Joseph ni a coe.
3 ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa: Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.
Isarel camin Reuben e casaknaw teh Hanok, Pallu, Hezron hoi Karmi.
4 Ana a Yoweli anali awa: Semaya, Gogi, Simei,
Joel casak teh, a capa Shemaiah, Shemaiah capa Gog, Gog capa Shimei.
5 Mika, Reaya, Baala,
Shimei capa Maikah, Mikah capa Reaiah, Reaiah capa Baal.
6 ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.
Baal capa Beerah. Ahni teh Reuben e khobawi lah ao eiteh, Assyria siangpahrang Tiglathpileser ni san lah a hrawi.
7 Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa: Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya,
Amae a nawngha Jeiel hoi Zekhariah, ahnimouh roi teh ca catoun separuinae pakhumnae dawkvah, imthungnaw kahrawikung lah ao.
8 ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni.
Azaz capa Bela, Shema capa Azaz, Joel capa Shema ni Aroer hoi Nebo Baalmeon totouh kho a sak.
9 Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.
Kanîtholah Euphrates palang hoi kahrawng thung kâennae totouh, a coe awh. Bangkongtetpawiteh, Gilead ram dawk saringnaw hah a pungdaw toe.
10 Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.
Sawl se navah Hagri miphunnaw hoi a kâtuk awh teh, Gilead kanîtholah totouh, rimnaw dawk kho a sak awh.
11 Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:
Gad e casaknaw teh avangvanglah Bashan ram dawk Salkah totouh ao awh.
12 Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.
Bashan vah a lû lah Joel, apâhni lah Shapham, Janai hoi Shaphat tinaw doeh.
13 Abale awo mwa mabanja awo anali awa: Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.
A na pa imthung hoi a hmaunawnghanaw Michael, Meshullam, Sheba, Jorai, Jakhan, Zia, Eber hoi sari touh a pha awh.
14 Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.
Hetnaw teh Huri capa Abihail e capanaw doeh. Ahni teh Jaorah capa doeh. Gilead capa, Michael capa, Jeshishai capa, Jahdo capa, Buz capa lah ao.
15 Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.
Guni capa, Abdiel capa, Ahni teh imthung kahrawikung lah ao.
16 Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.
Hatdawkvah, Gilead hoi Bashan khotenaw tengpam e ram pueng khori totouh kho a sak awh.
17 Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.
Hote hnonaw pueng teh, Judah siangpahrang Jotham e se hoi Isarel siangpahrang Jeroboam e se teh setouknae dawk thut lah ao toe.
18 Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo.
Reuben casak, Gad casak, hoi Manasseh miphun tangawn dawk hoi tarankahawinaw, bahling, tahloi ka patuem thai e naw, likathoumnaw, taran ka tuk thai e naw 44, 760 touh a pha awh.
19 Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu.
Hatnavah, Hagri, Jetur, Naphish hoi Nodabnaw hoi a kâtuk awh.
20 Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira.
Kâtuk nahaiyah Cathut koe a hram awh teh, ama a kâuep awh dawkvah, ahnimouh teh a kabawp awh. Hatdawkvah, Hagrinaw hoi ahnimouh koe kaawm e abuemlah a kut dawk hoi a rungngang awh.
21 Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000,
Saringnaw a man pouh awh teh, kalauk 50000, tu 250000, hoi la 2000 hoi tami 100000 a la awh.
22 enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.
Tarantuknae teh Cathut e lah ao dawkvah, tami moikapap a due awh. San toung totouh a onae hmuen koe ao awh.
23 Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.
Manasseh miphun tangawn teh, haw e ram dawk kho a sak awh. Bashan hoi Baalhermon hoi Senir hoi Hermon mon totouh tami teh a pungdaw awh.
24 Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo.
Hetnaw heh a imthungnaw kahrawikung lah a o: Epher, Ishi, Eliel, Azriel, Jeremiah, Hodaviah, Jahdiel. Ahnimanaw teh tami a thakaawme, min kamthang e, imthung kahrawikung lah ao awh.
25 Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika.
Mintoenaw e Cathut koe yuemkamcu awh hoeh dawkvah, ahnimae hmaitung Cathut ni a raphoe teh, hote ram dawk e cathutnaw koe a kâyo awh.
26 Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.
Hottelah Isarel Cathut ni Assiria siangpahrang Pul, Assiria siangpahrang Tiglathpileser e lungthin a tho sak teh, Reuben hoi Gad, Manasseh miphun tangawn hah san lah a man awh teh, Halah, Habor, Hara tinaw hah Gozan palang a ceikhai awh teh atu totouh ao awh.

< 1 Mbiri 5 >