< 1 Mbiri 29 >
1 Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
Ensuite David, le roi, dit à toute l’assemblée; Dieu a choisi uniquement Salomon, mon fils, encore jeune et délicat, quoique l’œuvre soit grande; car ce n’est pas pour un homme que se prépare cette habitation, mais pour Dieu.
2 Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
Pour moi, j’ai préparé de toutes mes forces les dépenses de la maison de mon Dieu; l’or pour les vases d’or, l’argent pour les vases d’argent, l’airain pour ceux d’airain, le fer pour ceux de fer, le bois pour ceux de bois, des pierres d’onyx, d’autres semblables à l’antimoine, d’autres de diverses couleurs, enfin toute sorte de pierres précieuses, et du marbre de Paros en très grande quantité.
3 Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
Et, par-dessus ces choses que j’ai offertes pour la maison de mon Dieu, je donne de mon propre bien de l’or et de l’argent pour le temple de mon Dieu, outre ce que j’ai préparé pour son sanctuaire:
4 Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
Trois mille talents d’or, de l’or d’Ophir, et sept mille talents d’argent très pur, pour en revêtir les murailles du temple.
5 zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
Et partout où il est besoin d’or et partout où il est besoin d’argent, que les ouvrages soient faits d’or et d’argent par les mains des ouvriers; et si quelqu’un fait spontanément une offrande, qu’il remplisse sa main aujourd’hui, et qu’il offre ce qu’il voudra au Seigneur.
6 Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
C’est pourquoi les princes des familles et les grands des tribus d’Israël le promirent, ainsi que les tribuns, les centurions et les intendants des possessions du roi.
7 Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
Et ils donnèrent pour les ouvrages de la maison de Dieu cinq mille talents d’or et dix mille solides, dix mille talents d’argent, dix-huit mille talents d’airain, ainsi que cent mille talents de fer.
8 Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
De même tous ceux chez qui on trouva des pierres précieuses les donnèrent pour le trésor de la maison du Seigneur, par l’entremise de Jahiel, le Gersonite.
9 Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
Et le peuple se livra à l’allégresse en promettant spontanément ses offrandes, parce qu’il les offrait de tout cœur au Seigneur; et aussi, David, le roi, se réjouit d’une grande joie.
10 Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
Et il bénit le Seigneur devant toute la multitude, et il dit: Seigneur, Dieu d’Israël, notre père, vous êtes béni de siècle en siècle.
11 Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
À vous, Seigneur, est la magnificence, la puissance, la gloire et la victoire; à vous la louange; car tout ce qui est dans le ciel et sur la terre est à vous; à vous. Seigneur, est le règne, et c’est vous qui êtes au-dessus de tous les princes.
12 Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
À vous les richesses et à vous la gloire; c’est vous qui dominez sur toutes les créatures: en votre maison sont la force et la puissance; en votre main la grandeur et l’empire sur toutes choses
13 Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
Maintenant donc, ô notre Dieu, nous vous glorifions et nous louons votre nom illustre.
14 “Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
Qui suis-je, et qui est mon peuple pour que nous puissions vous offrir toutes ces choses? Tout est à vous, et c’est de votre main que nous avons reçu ce que nous vous avons donné;
15 Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
Car nous sommes des voyageurs et des étrangers devant vous comme tous nos pères. Nos jours passent comme l’ombre sur la terre, et rien ne les retient.
16 Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
Seigneur notre Dieu, toutes ces richesses que nous avons préparées pour bâtir une maison à votre saint nom sont de votre main, et à vous sont toutes choses.
17 Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
Je sais, mon Dieu, que vous sondez les cœurs et que vous aimez la simplicité; c’est pourquoi, moi aussi, je vous ai offert toutes ces choses dans la simplicité de mon cœur, et plein d’allégresse; et votre peuple qui se trouve ici, je l’ai vu avec une grande joie vous offrir ses présents.
18 Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
Seigneur Dieu d’Abraham, d’Isaac et d’Israël, nos pères, conservez éternellement cette volonté de leur cœur, et que toujours ce sentiment de vénération pour vous persévère.
19 Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
Donnez aussi à Salomon, mon fils, un cœur parfait, afin qu’il garde vos commandements, vos témoignages et vos cérémonies, et qu’il les accomplisse tous; et qu’il bâtisse la maison dont j’ai préparé les dépenses.
20 Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
Or David ordonna à toute l’assemblée: Bénissez le Seigneur notre Dieu. Et toute l’assemblée bénit le Seigneur Dieu de leurs pères; ils s’inclinèrent, et ils adorèrent Dieu et ensuite le roi.
21 Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
Et ils immolèrent des victimes au Seigneur; et ils lui offrirent des holocaustes le jour suivant: mille taureaux, mille béliers et mille agneaux, avec leurs libations, et en accomplissant tout le rite: il y en eut très abondamment pour tout Israël.
22 Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
Et ils mangèrent et burent devant le Seigneur en ce jour-là avec une grande allégresse. Et ils oignirent une seconde fois Salomon, fils de David. Or, ils l’oignirent pour le Seigneur comme prince, et Sadoc, comme pontife.
23 Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
Ainsi Salomon s’assit sur le trône du Seigneur, comme roi, à la place de David, son père, et il plut à tous; et tout Israël lui obéit.
24 Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
Et tous les princes mêmes, les puissants, et tous les fils du roi David donnèrent la main et se soumirent à Salomon, le roi.
25 Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
Le Seigneur éleva donc Salomon sur tout Israël, et il donna à son règne une gloire telle que n’en eut avant lui aucun roi d’Israël.
26 Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
Ainsi David, fils d’Isaï, régna sur tout Israël;
27 Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
Et les jours pendant lesquels il régna sur Israël furent quarante années: il régna sept ans à Hébron, et à Jérusalem, trente-trois ans.
28 Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et il mourut dans une heureuse vieillesse, plein de jours, et dans les richesses et dans la gloire; et Salomon son fils régna en sa place.
29 Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
Or les actions de David, le roi, les premières et les dernières, sont écrites dans le Livre de Samuel, le Voyant, et dans le Livre de Nathan, le prophète, et dans le volume de Gad, le Voyant,
30 pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.
Et l’histoire de tout son règne, de sa force, et des temps qui ont passé de son vivant, soit en Israël, soit dans tous les royaumes de la terre.