< 1 Mbiri 29 >

1 Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
And kyng Dauid spak to al the chirche, God hath chose Salomon, my sone, yit a child and tendre; forsothe the werk is greet, and a dwellyng is not maad redi to man but to God.
2 Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
Sotheli Y in alle my myytis haue maad redi the costis of the hows of my God; gold to goldun vessels, siluer in to siluerne vessels, bras in to brasun vessels, irun in to irun vessels, tre in to trenun vessels, onychyn stonys, and stonys as of the colour of wymmens oynement, and ech precious stoon of dyuerse colouris, and marbil of dyuerse colouris, most plenteuously.
3 Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
And ouer these thingis Y yyue gold and siluer in to the temple of my God, whiche Y offride of my propir catel in to the hows of my God, outakun these thingis whiche Y made redi in to the hooli hows,
4 Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
thre thousynde talentis of gold, of the gold of Ophir, and seuene thousynde of talentis of siluer most preuyd, to ouergilde the wallis of the temple;
5 zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
and werkis be maad bi the hondis of crafti men, where euere gold is nedeful, of gold, and where euere siluer is nedeful, of siluer; and if ony man offrith bi his fre wille, fille he his hond to dai, and offre he that that he wole to the Lord.
6 Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
Therfor the princes of meynees, and the duykis of the lynagis of Israel, and the tribunes, and the centuriouns, and the princes of the possessiouns of the kyng, bihiyten;
7 Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
and thei yauen in to the werkis of the hows of the Lord, fyue thousynde talentis of gold, and ten thousynde schyllyngis; ten thousynde talentis of siluer, and eiytene thousynde talentis of bras, and an hundrid thousynde of talentis of irun.
8 Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
And at whom euere stoonys were foundun, thei yauen in to the tresour of the hows of the Lord, bi the hond of Jehiel Gersonyte.
9 Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
And the puple was glad, whanne thei bihiyten avowis bi her fre wille, for with al the herte thei offriden tho to the Lord. But also kyng Dauid was glad with greet ioye, and blesside the Lord bifor al the multitude,
10 Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
and seide, Lord God of Israel, oure fadir, thou art blessid fro with outen bigynnyng in to with outen ende;
11 Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
Lord, worthi doyng is thin, and power, and glorie, and victorie, and heriyng is to thee; for alle thingis that ben in heuene and in erthe ben thine; Lord, the rewme is thin, and thou art ouer alle princes; ritchessis ben thin, and glorie is thin;
12 Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
thou art Lord of alle; in thin hond is vertu, and power, and in thin hond is greetnesse, and lordschipe of alle.
13 Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
Now therfor, oure God, we knoulechen to thee, and we herien thi noble name.
14 “Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
Who am Y, and who is my puple, that we moun bihete alle these thingis to thee? Alle thingis ben thine, and we han youe to thee tho thingis, whiche we token of thin hond.
15 Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
For we ben pilgrimes and comelyngis bifor thee, as alle oure fadris; oure daies ben as schadewe on the erthe, and `no dwellyng is.
16 Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
Oure Lord God, al this plentee which we han maad redi, that an hows schulde be byldid to thin hooli name, is of thin hond; and alle thingis ben thin.
17 Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
My God, Y woot, that thou preuest hertis, and louest symplenesse of herte; wherfor and Y, in the symplenesse of myn herte, haue offrid gladli alle these thingis; and Y siy with greet ioye thi puple, which is foundun here, offre yiftis to thee.
18 Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
Lord God of Abraham, and of Ysaac, and of Israel, oure fadris, kepe thou with outen ende this wille of her hertis; and this mynde dwelle euere in to the worschipyng of thee.
19 Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
Also yyue thou to Salomon, my sone, a perfit herte, that he kepe thin heestis, and witnessyngis, and thi ceremonyes; and do alle thingis, and that he bilde the hows, whose costis Y haue maad redi.
20 Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
Forsothe Dauid comaundide to al the chirche, Blesse ye `oure Lord God. And al the chirche blesside the Lord God of her fadris, and thei bowiden hem silf, and worschipiden God, aftirward the kyng.
21 Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
And thei offriden slayn sacrifices to the Lord, and thei offriden brent sacrifices in the dai suynge; a thousynde boolis, and a thousynde rammes, and a thousynde lambren, with her fletynge sacrifices, and al the custom, most plenteuously, in to al Israel.
22 Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
And thei eten and drunken bifor the Lord in that dai, with greet gladnesse. And thei anoyntiden the secounde tyme Salomon, the sone of Dauid; and thei anoyntiden hym in to prince to the Lord, and Sadoch in to bischop.
23 Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
And Salomon sat on the trone of the Lord in to kyng, for Dauid, his fadir; and it pleside alle men, and al Israel obeiede to hym.
24 Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
But also alle princes, and myyti men, and alle the sones of kyng Dauid, yauen hond, and weren suget to `Salomon the kyng.
25 Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
Therfor the Lord magnefiede Salomon on al Israel, and yaue to hym glorie of the rewme, what maner glorie no kyng of Israel hadde bifor hym.
26 Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
Therfor Dauid, the sone of Ysai, regnede on al Israel;
27 Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
and the daies in whiche he regnede on Israel weren fourti yeer; in Ebron he regnede seuene yeer, and in Jerusalem thre and thretti yeer.
28 Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And he diede in good eelde, and was ful of daies, and richessis, and glorie; and Salomon, his sone, regnede for hym.
29 Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
Forsothe the formere and the laste dedis of Dauid ben writun in the book of Samuel, the prophete, and in the book of Nathan, prophete, and in the book of Gad, the prophete;
30 pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.
and of al his rewme, and strengthe, and tymes, that passiden vndur hym, ethir in Israel, ethir in alle rewmes of londis.

< 1 Mbiri 29 >