< 1 Mbiri 29 >

1 Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
And he said David the king to all the assembly Solomon son my [whom] one he has chosen him God [is] a youth and weak and the work [is] great for not [is] for a human person the temple for for Yahweh God.
2 Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
And according to all power my I have prepared for [the] house of God my the gold - for the gold and the silver for the silver and the bronze for the bronze the iron for the iron and the wood for the wood stones of onyx and settings stones of antimony and variegated color and every stone precious and stones of alabaster to abundance.
3 Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
And again because delight I in [the] house of God my there [belongs] to me treasure gold and silver I give for [the] house of God my upwards more than all [that] I have prepared for [the] house of the holiness.
4 Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
Three thousand talents of gold from [the] gold of Ophir and seven thousand talent[s] of silver purified to overlay [the] walls of the houses.
5 zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
the Gold for the gold and the silver for the silver and for every work by [the] hand of craftsmen and who? [is] making a contribution to fill own hand his this day to Yahweh.
6 Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
And they made a contribution [the] leaders of the fathers and [the] leaders of - [the] tribes of Israel and [the] commanders of the thousands and the hundreds and [the] leaders of [the] work of the king.
7 Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
And they gave for [the] service of [the] house of God gold talents five thousand and darics ten thousand and silver talents ten thousand and bronze ten thousand and eight thousand talents and iron one hundred thousand talents.
8 Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
And the [one who] was found with him stones they gave [them] to [the] treasury of [the] house of Yahweh on [the] hand of Jehiel the Gershonite.
9 Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
And they rejoiced the people because had made a contribution they for with a heart complete they had made a contribution to Yahweh and also David the king he rejoiced joy great.
10 Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
And he blessed David Yahweh to [the] eyes of all the assembly and he said David [be] blessed you O Yahweh [the] God of Israel ancestor our from antiquity and until perpetuity.
11 Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
[belong] to You O Yahweh the greatness and the strength and the splendor and the eminence and the majesty for everything in the heavens and on the earth [belongs] to you O Yahweh the kingdom and the [one who] raises himself to all - to head.
12 Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
And wealth and honor [are] from before you and you [are] ruling over everything and [are] in hand your power and strength and [are] in hand your to make great and to make strong everyone.
13 Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
And therefore O God our [are] giving thanks we to you and [are] praising [the] name of splendor your.
14 “Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
And that who? [am] I and who? [is] people my that we will retain strength to make a contribution like this for [is] from you everything and from hand your we have given to you.
15 Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
For [are] sojourners we before you and resident aliens like all ancestors our [are] like shadow - days our on the earth and there not [is] hope.
16 Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
O Yahweh God our all the abundance this which we have prepared to build for you a house for [the] name of holiness your [is] from hand your (it *Q(K)*) and [belongs] to you everything.
17 Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
And I know O God my that you [are] testing [the] heart and uprightness you are pleased with I in [the] uprightness of heart my I have made a contribution all these [things] and now people your who are found here I have seen with joy to make a contribution to you.
18 Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
O Yahweh [the] God of Abraham Isaac and Israel ancestors our keep! this for ever [the] inclination of [the] thoughts of [the] heart of people your and direct heart their to yourself.
19 Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
And to Solomon son my give a heart complete to keep commandments your testimonies your and decrees your and to do everything and to build the temple which I have prepared.
20 Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
And he said David to all the assembly bless please Yahweh God your and they blessed all the assembly Yahweh [the] God of ancestors their and they bowed low and they bowed down to Yahweh and to the king.
21 Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
And they sacrificed to Yahweh - sacrifices and they offered up burnt offerings to Yahweh to [the] next day of the day that young bulls one thousand rams one thousand lambs one thousand and drink offerings their and sacrifices to abundance for all Israel.
22 Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
And they ate and they drank before Yahweh on the day that with joy great and they made king a second [time] Solomon [the] son of David and they anointed [him] to Yahweh to ruler and Zadok to priest.
23 Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
And he sat Solomon on [the] throne of Yahweh - to king in place of David father his and he was successful and they listened to him all Israel.
24 Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
And all the officials and the mighty [men] and also all [the] sons of the king David they gave a hand under Solomon the king.
25 Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
And he made great Yahweh Solomon upwards to [the] eyes of all Israel and he put on him majesty of royalty which not it had been on any king before him over Israel.
26 Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
And David [the] son of Jesse he reigned over all Israel.
27 Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
And the days which he reigned over Israel [were] forty year[s] in Hebron he reigned seven years and in Jerusalem he reigned thirty and three [years].
28 Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And he died in old age good satisfied of days wealth and honor and he reigned Solomon son his (in place of him. *LA(bh)*)
29 Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
And [the] matters of David the king former and latter there they [are] written on [the] words of Samuel the seer and on [the] words of Nathan the prophet and on [the] words of Gad the seer.
30 pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.
With all kingdom his and might his and the times which they passed over him and over Israel and over all [the] kingdoms of the lands.

< 1 Mbiri 29 >