< 1 Mbiri 28 >

1 Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
UDavida wasebuthanisa zonke iziphathamandla zakoIsrayeli, iziphathamandla zezizwe, leziphathamandla zezigaba ezazisebenzela inkosi, labaphathi bezinkulungwane, labaphathi bamakhulu, labaphathi bempahla yonke labezifuyo zenkosi labezamadodana ayo, lezinduna, lamaqhawe, lawo wonke amaqhawe alamandla, eJerusalema.
2 Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
UDavida inkosi wasesima ngenyawo zakhe wathi: Ngilalelani, bafowethu labantu bami. Mina, kwakusenhliziyweni yami ukwakhela umtshokotsho wesivumelwano seNkosi indlu yokuphumula, leyisigcabha senyawo zikaNkulunkulu wethu, ngenza amalungiselelo okwakha.
3 Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
Kodwa uNkulunkulu wathi kimi: Kawuyikulakhela ibizo lami indlu, ngoba wena ungumuntu wempi, uchithe igazi elinengi.
4 “Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
Kanti iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli yangikhetha kuyo yonke indlu kababa ukuthi ngibe yinkosi phezu kukaIsrayeli kuze kube nininini; ngoba yakhetha uJuda ukuba ngumbusi, lendlini yakoJuda indlu kababa; laphakathi kwamadodana kababa yangithanda ukungenza ngibe yinkosi phezu kukaIsrayeli wonke.
5 Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
Lakuwo wonke amadodana ami (ngoba iNkosi yanginika amadodana amanengi) yakhetha uSolomoni indodana yami ukuthi ahlale esihlalweni sobukhosi sombuso weNkosi phezu kukaIsrayeli.
6 Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
Yasisithi kimi: USolomoni indodana yakho nguye ozakwakha indlu yami lamaguma ami, ngoba ngimkhethile ukuba yindodana yami, lami ngizakuba nguyise.
7 Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
Njalo ngizawuqinisa umbuso wakhe kuze kube nininini uba eqina ukwenza imilayo yami lezahlulelo zami njengalamuhla.
8 “Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
Ngakho-ke phambi kwamehlo kaIsrayeli wonke, ibandla leNkosi, lendlebeni zikaNkulunkulu wethu, gcinani lidinge yonke imilayo yeNkosi uNkulunkulu wenu, ukuze lidle ilifa lalelilizwe elihle, lenze abantwana benu badle ilifa lalo emva kwenu kuze kube nininini.
9 “Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
Wena-ke, Solomoni ndodana yami, mazi uNkulunkulu kayihlo, umkhonze ngenhliziyo epheleleyo langengqondo evumayo; ngoba iNkosi iyazihlola zonke inhliziyo, iqedisise konke ukuzindla kwemicabango. Uba uyidinga, izatholwa nguwe; kodwa uba uyitshiya, izakulahla kokuphela.
10 Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
Bona-ke, ngoba iNkosi ikukhethile ukuthi wakhe indlu ibe yindlu engcwele; qina, ukwenze.
11 Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
UDavida wasenika uSolomoni indodana yakhe umdwebo wekhulusi, lowezindlu zalo, loweziphala zezinto eziligugu, lowamakamelo aphezulu, lowamakamelo aphakathi, lowendlu yesihlalo somusa.
12 Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
Lomdwebo wakho konke ayelakho ngoMoya, lowamaguma endlu yeNkosi, lowamakamelo wonke azingelezeleyo, loweziphala zezinto eziligugu zendlu kaNkulunkulu, loweziphala zokuligugu zezinto ezingcwele,
13 Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
lowezigaba zabapristi lezamaLevi, lowomsebenzi wonke wenkonzo yendlu yeNkosi, lowezitsha zonke zenkonzo yendlu yeNkosi.
14 Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
Wapha igolide ngesisindo ngezinto zegolide, ngempahla yonke yenkonzo ngenkonzo, ngempahla yonke yesiliva ngesisindo, ngempahla yonke yenkonzo ngenkonzo,
15 kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
lesisindo sezinti zesibane zegolide, lezibane zazo zegolide, ngesisindo soluthi lwesibane ngalunye lezibane zalo, langezinti zesibane zesiliva, ngesisindo soluthi lwesibane lezibane zalo, njengomsebenzi woluthi lwesibane ngalunye.
16 kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
Wasenika igolide ngesisindo lamatafula ezinkwa zokubukiswa, ngalelo lalelotafula, lesiliva samatafula esiliva.
17 muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
Lamafologwe lemiganu yokufafaza lezinkezo zegolide elicwengekileyo, langezitsha zegolide ngesisindo saleso lalesositsha, langezitsha zesiliva ngesisindo saleso lalesositsha.
18 ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
Langelathi lempepha igolide elicwengekileyo ngesisindo, langomdwebo wenqola yamakherubhi egolide elule impiko agubuzela umtshokotsho wesivumelwano seNkosi.
19 Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
UDavida wathi: Konke lokhu iNkosi yenza ngikuqedisise ngombhalo ngesandla sayo phezu kwami, yonke imisebenzi yomdwebo.
20 Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
UDavida wasesithi kuSolomoni indodana yakhe: Qina, ube lesibindi, usebenze; ungesabi, ungatshaywa luvalo; ngoba iNkosi uNkulunkulu, uNkulunkulu wami, ilawe. Kayisoze yakulahla, kayisoze yakutshiya, uze uqede umsebenzi wonke wenkonzo yendlu yeNkosi.
21 Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”
Khangela-ke, izigaba zabapristi lezamaLevi, zenkonzo yonke yendlu kaNkulunkulu; njalo kuzakuba lawe kuwo wonke umsebenzi, wonke oyingcitshi ovumayo kuyo yonke inkonzo, labaphathi labo bonke abantu bazakuba njengokulaya kwakho konke.

< 1 Mbiri 28 >