< 1 Mbiri 28 >

1 Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
And David assembled all the princes of Israel, the princes of the tribes, and the captains of the divisions that ministered to the king, and the captains of the thousands, and the captains of the hundreds, and the rulers of all the property and the cattle of the king and of his sons, with the court-servants, and the mighty men, and with all the valiant men of the army, unto Jerusalem.
2 Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
Then arose king David upon his feet, and said, Hear me, my brethren, and my people! I had in my heart to build a house of rest for the ark of the covenant of the Lord, and for the footstool of our God, and I had made preparations to build;
3 Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
But God said unto me, Thou shalt not build a house unto my name; because thou art a man of war, and blood hast thou shed.
4 “Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
Yet the Lord the God of Israel made choice of me out of all the house of my father to be king over Israel for ever; for of Judah had he made choice as ruler, and among the house of Judah, of the house of my father; and among the sons of my father had he pleasure in me to make [me] king over all Israel:
5 Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
And of all my sons, —for the Lord hath given me many sons, — hath he made choice of Solomon my son, to sit upon the throne of the kingdom of the Lord over Israel.
6 Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
And he hath said unto me, Solomon thy son it is that shall build my house and my courts; for I have made choice of him to be as a son unto me, and I will be indeed to him as a father.
7 Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
Moreover, I will firmly establish his kingdom for everlasting, if he be strong to execute my commandments and my ordinances as it is this day.
8 “Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
And now before the eyes of all Israel, the congregation of the Lord, and in the hearing of our God, [I admonish you] observe and seek for all the commandments of the Lord your God: in order that ye may keep possession of this good land, and leave it for an inheritance unto your children after you forever.
9 “Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
And thou, Solomon my son, know thou the God of thy father, and serve him with an entire heart and with a willing soul; for all hearts doth the Lord search, and every imagination of the thoughts doth he understand; if thou seek him, he will let himself be found by thee; but if thou forsake him, he will cast thee off for ever.
10 Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
See now that the Lord hath made choice of thee to build a house for the sanctuary: be strong and do it.
11 Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
Then gave David to Solomon his son the pattern of the porch, and of its apartments, and of its treasuries, and of upper chambers, and of its inner chambers, and of the place of the cover of the ark.
12 Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
And the pattern of all that he had in his spirit, concerning the courts of the house of the Lord, and concerning all the chambers round about, concerning the treasuries of the house of God, and concerning the treasuries of the holy things:
13 Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
Also concerning the divisions of the priests and the Levites, and concerning all the work of the service of the house of the Lord, and concerning all the vessels of service of the house of the Lord;
14 Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
Concerning the golden vessels, after the weight of the gold, for all the vessels of all manner of service; concerning all the vessels of silver after the weight, for all the vessels of every kind of service;
15 kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
Also the weight for the candlesticks of gold, and for their lamps of gold, after the weight for every candlestick, and for its lamps; and concerning the candlesticks of silver after the weight, for the candlestick, and for its lamps, according to the use of every candlestick;
16 kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
And the gold after the weight for the tables of the rows of shewbread, for every table; and the silver for the tables of silver;
17 muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
Also [concerning] the forks, and the bowls, and the supporters of pure gold; and concerning the golden cups after the weight for every cup; and concerning the silver cups after the weight for every cup;
18 ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
And concerning the altar of incense the refined gold after the weight; and concerning the pattern of the chariot of the golden cherubim, which spread out [their wings], and over the ark of the covenant of the Lord.
19 Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
All [this, said David, ] was put in writing from the hand of the Lord, who gave me instruction [respecting] all the works of the pattern.
20 Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
And David said to Solomon his son, Be strong, and of good courage, and do [the work]; fear not, and be not dismayed; for the Lord God, [yea, ] my God is with thee: he will not fail thee, nor forsake thee, until thou have finished all the work for the service of the house of the Lord.
21 Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”
And, behold, the divisions of the priests and the Levites are there for all the service of the house of God; and with thee are in all manner of workmanship all kinds of men distinguished in wisdom, for every manner of service; and the princes and all the people are ready [to obey] all thy words.

< 1 Mbiri 28 >