< 1 Mbiri 28 >

1 Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
David in alenggam sung’a sepai jalamkai, vaipo le vaibol jouse, phung lamkai hihen gou ching hihen, hetthei a panmun la jouse chuleh gaalhang jouse Jerusalem a akou sohkei un.
2 Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
Akipatdoh in hity hin aseitai, “Ka sopi le Ka miteho, keiman Pathen kitepna thingkong a itih a aum jing nading, Pathen houin theng sahdoh ding ka ngaiton, kigotnan thil le lo angaicha tampi jong kakoitai.
3 Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
Ahinlah, Pakai Pathenin keima gaal-hat tah chuleh mi tampi that kahi jeh in eiphal pon ahi.
4 “Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
Hijeng jongle, Israel Pathenin Judahte lah a konna, ka insung uva pat keimatah, a itih hijongle Israel leng dia ei thaonu ahitai.
5 Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
Chutahle, chapa tamtah phatthei eiboh ho lah a konna ka chapa Solomon in ka lengtou namun ei khel ding ahi” ati.
6 Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
Pathenin kajah a aseiye, “Nachapa Solomon in Ka houin theng le akimvel asahdoh dia kalhendoh ahitan, keiman angaichat ijakai kapeh jing ding ahi” ati.
7 Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
Chutahle, “Ka thupeh chengse anit jing’a ahile, Keiman a lenggam a itih a ka umpi jing ding ahi” ati.
8 “Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
“Hijeh chun, Pakai le houbung pumpi angsung chuleh, Israel mite mitmun chingtheiyun lang na pakai na Pathen thupeh chengse nit jing un, chutileh lungmong a gampha lai na lo uva, nachateu le na tuteu khang geiya Pakai phatthei na nachan jing diu ahi,” ati.
9 “Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
“Chujongle, Solomon kachapa, na Pu le na Pa phattheiboh jing na Pathen chu haimil lou jen’in. Nalungthim pumpin choi’an jing inlang athun umjingin, ajehchu thil ijakai amun, ahe sohkeiyin, bel jing lechun, na lhaso lou ding ahi,” ati.
10 Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
“Hijeh chun, nalung gil in ngaiton. Pakai Pathen in a houin theng sa dia nalhendoh ahitan. Hat jing in lang natohdoh tei ding ahi,” ati.
11 Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
Chuin, David in athilgon ejakai, thil kholna indan ho chule chonset kingaidam na munho umdol jouse Solomon apetan ahi.
12 Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
David in alunggil a agontohsa, Houin lim asung apo, indan dang dang chule Maicham kibolna Muntheng dia agon ho jouse achapa Solomon aseipeh tai.
13 Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
Chujongle, Houin sunga Themgao hole Levi mite panmun hihen, Pathen hou nadia thil le lo kimang ding jouse jong ahiltan ahi.
14 Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
David in Pathen Hou na a Sana le Sum eng man dia lom jat jong ahiltoh in,
15 kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
Solomon jah a Sana thaomei semna ding le sum eng thaomei semna ding chuleh sana le sum eng alut ding jat jong ahilthem in ahi.
16 kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
Changlhah hung kitohdoh ho koina ding Sana theng a kisem Dokhang chule, sum eng a kisem dokhang ho jong akisem na a sana angaicha ding jat jong ahilthem e.
17 muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
Thih-khe sana thengsel ijat a sem a, khon, Kong, Sil kong ho jouse sana ijat cheh a sem ding aboncha a atetoh peh soh e.
18 ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
Chujongle, gim namtwi hal nading maicham phung semna dia sana thengsel man ding jat, chule Kangtalai sung a Cherubium vantil in a lhaving teni a akhu khum, Pakai kitepna thingkong sem ding dan jong ahiltan ahi.
19 Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
“Thilgon hichengse hi”, tin David in Solomon jah a, “Pathenin akhut tah a asut eimudohsah akon kahet ahi” ati.
20 Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
David in abanjom in, “hat in lang hang jingin, natohdoh ding ahi. Kichat le lunglhah daina neihih hel in. Pakai Pathenin na umpi jing’e. Nanganse nabang’a nachai theng tokah a Pakai Pathen in na lhonpi jing ding ahi”.
21 Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”
“Themgao ho le Levi mite akinganse na banga pakai kin abol diu, adangse injong akipeh nathei chan uva pan alah uva, gamsung vaipo ho jouse le thuneina aboncha a nangma thunoi a umding ahi” ati.

< 1 Mbiri 28 >