< 1 Mbiri 27 >
1 Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
Or les enfants d’Israël, suivant leur nombre, les princes de familles, les tribuns, les centurions, et les préposés qui, selon leurs bandes, servaient le roi, entrant et sortant à chaque mois dans l’année, étaient chacun à la tête de vingt-quatre mille hommes.
2 Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Au premier mois, Jesboa, fils de Zabdiel, était à la tête de la première bande, et sous lui étaient vingt-quatre mille hommes.
3 Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
Il était d’entre les fils de Pharès, et le prince de tous les princes dans l’armée, au premier mois.
4 Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Dudia, l’Ahohite, avait la bande du second mois, et après lui était un second du nom de Macelloth, qui dirigeait une partie de l’armée de vingt-quatre mille hommes.
5 Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
De plus, le chef de la troisième bande, au troisième mois, était Banaïas, le prêtre, fils de Joïada, et dans sa division étaient vingt-quatre mille hommes.
6 Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
C’est ce même Banaïas, le plus vaillant parmi les trente, et au-dessus des trente. Amizabad, son fils, était aussi à la tête de sa bande.
7 Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le quatrième chef, au quatrième mois, était Asahel, frère de Joab, et Zabadias, son fils, après lui; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
8 Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le cinquième, au cinquième mois, Samaoth, le Jézerite; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
9 Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le sixième, au sixième mois, Hira, fils d’Accès, le Thécuite; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
10 Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le septième, au septième mois, Hellès, le Phallonite, d’entre les fils d’Ephraïm; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
11 Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
Le huitième, au huitième mois, Sobochaï, le Husathite, de la race de Zarahi; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
12 Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le neuvième, au neuvième mois, Abiézer, l’Anathothite, d’entre les fils de Jémini; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
13 Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le dixième, au dixième mois, Maraï, le Nétophathite, de la race de Zaraï; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
14 Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le onzième, au onzième mois, Banaïas, le Pharatonite, d’entre les fils d’Ephraïm; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
15 Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Le douzième, au douzième mois, Holdaï, le Nétophathite, de la race de Gothoniel; et dans sa bande étaient vingt-quatre mille hommes.
16 Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
Quant aux tribus d’Israël, à la tête des Rubénites, était le chef, Eliézer, fils de Zechri; à la tête des Siméonites, le chef Saphatias, fils de Maacha;
17 mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
À la tête des Lévites, Hasabias, fils de Camuel; à la tête des Aaronites, Sadoc;
18 mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
À la tête de Juda, Eliu, frère de David; à la tête d’Issachar, Amri, fils de Michaël;
19 mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
À la tête des Zabulonites, Jesmaïas, fils d’Abdias; à la tête des Nephthalites, Jérimoth, fils d’Ozriel;
20 mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
À la tête des fils d’Ephraïm, Osée, fils d’Ozaziu; à la tête de la demi-tribu de Manassé, Joël, fils de Phadaïa;
21 mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
Et à la tête de la demi-tribu de Manassé en Galaad, Jaddo, fils de Zacharie; mais à la tête de Benjamin, Jasiel, fils d’Abner;
22 mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
Et à la tête de Dan, Ezrihel, fils de Jéroham. Voilà les princes des enfants d’Israël.
23 Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
Mais David ne voulut pas les dénombrer au-dessous de vingt ans, parce que le Seigneur avait dit qu’il multiplierait les enfants d’Israël comme les étoiles du ciel.
24 Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
Joab, fils de Sarvia, avait commencé à dénombrer; mais il n’acheva pas, parce que pour cela était tombée la colère du Seigneur sur Israël; et c’est pourquoi le nombre de ceux qui avaient été recensés n’a pas été relaté dans les fastes du roi David.
25 Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
Le surintendant des trésors du roi était Azmoth, fils d’Adiel; quant aux trésors des villes, des bourgs et des tours, Jonathan, fils d’Osias, en avait la garde;
26 Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
Mais aux travaux de la campagne et aux laboureurs qui travaillaient la terre, présidait Ezri, fils de Chélub.
27 Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
À ceux qui cultivaient les vignes, c’était Séméias, le Romathite; mais aux celliers où on met le vin, Zabdias, l’Aphonite.
28 Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
Aux plants d’oliviers, aux figuiers, qui étaient dans les plaines, Balanan, le Gédérite, et aux magasins d’huile, Joas.
29 Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
Mais aux troupeaux qui paissaient en Saron, fut préposé Sétraï, le Saronite, et aux bœufs dans les vallées, Saphat, fils d’Adli;
30 Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
Sur les chameaux, Ubil, L’Ismahélite, et sur les ânes, Jadias, le Méronathite;
31 Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
Et sur les brebis, Jaziz l’Agaréen. Tous ceux-là étaient les intendants des biens du roi David.
32 Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
Mais Jonathan, oncle de David, homme sage et savant, était un de ses conseillers; lui et Jahiel, fils d’Hachamoni, étaient auprès des enfants du roi.
33 Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
Achitophel aussi était conseiller du roi; Chusaï, l’Arachite, favori du roi.
34 Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.
Après Achitophel étaient Joïada, fils de Banaïas, et Abiathar; mais le prince de l’armée du roi était Joab.