< 1 Mbiri 27 >

1 Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
Now the children of Israel according to their number, the heads of families, captains of thousands and of hundreds, and officers, that served the king according to their companies, who came in and went out every month in the year, under every chief were four and twenty thousand.
2 Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Over the first company the first month Jesboam, the son of Zabdiel was chief, and under him were four and twenty thousand.
3 Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
Of the sons of Phares, the chief of all the captains in the host in the first month.
4 Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The company of the second month was under Dudia, an Ahohite, and after him was another named Macelloth, who commanded a part of the army of four and twenty thousand.
5 Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
And the captain of the third company for the third month, was Banaias the son of Joiada the priest: and in his division were four and twenty thousand.
6 Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
This is that Banaias the most valiant among the thirty, and above the thirty. And Amizabad his son commanded his company.
7 Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The fourth, for the fourth month, was Asahel the brother of Joab, and Zabadias his son after him: and in his company were four and twenty thousand.
8 Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The fifth captain for the fifth month, was Samaoth a Jezerite: and his company were four and twenty thousand.
9 Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The sixth, for the sixth month, was Hira the son of Acces a Thecuite: and in his company were four and twenty thousand.
10 Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The seventh, for the seventh month, was Helles a Phallonite of the sons of Ephraim: and in his company were four and twenty thousand.
11 Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
The eighth, for the eighth month, was Sobochai a Husathite of the race of Zarahi: and in his company were four and twenty thousand.
12 Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The ninth, for the ninth month, was Abiezer an Anathothite of the sons of Jemini, and in His company were four and twenty thousand.
13 Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The tenth, for the tenth month, was Marai, who was a Netophathite of the race of Zarai: and in his company were four and twenty thousand.
14 Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The eleventh, for the eleventh month, was Banaias, a Pharathonite of the sons of Ephraim: and in his company were four and twenty thousand.
15 Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The twelfth, for the twelfth month, was Holdai a Netophathite, of the race of Gothoniel: and in his company were four and twenty thousand.
16 Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
Now the chiefs over the tribes of Israel were these: over the Rubenites, Eliezer the son of Zechri was ruler: over the Simeonites, Saphatias the son of Maacha:
17 mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
Over the Levites, Hasabias the son of Camuel: over the Aaronites, Sadoc:
18 mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
Over Juda, Eliu the brother of David: over Issachar, Amri the son of Michael:
19 mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
Over the Zabulonites, Jesmaias the son of Adias: over the Nephtalites, Jerimoth the son of Ozriel:
20 mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
Over the sons of Ephraim, Osee the: son of Ozaziu: over the half tribe of Manasses, Joel the son of Phadaia:
21 mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
And over the half tribe of Manasses: in Galaad, Jaddo the son of Zacharias: and over Benjamin, Jasiel the son of Abner.
22 mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
And over Dan, Ezrihel the son of Jeroham: these were the princes of the children of Israel.
23 Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
But David would not number them from twenty years old and under: because the Lord had said that he would multiply Israel like the stars of heaven.
24 Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
Joab the son of Sarvia began to number, but he finished not: because upon this there fell wrath upon Israel: and therefore the number of them that were numbered, was not registered in the chronicles of king David.
25 Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
And over the king’s treasures was Azmoth the son of Adiel: and over those stores which were in the cities, and is the villages, and in the castles, was Jonathan the son of Ozias.
26 Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
And over the tillage, and the husbandmen, who tilled the ground, was Ezri the son of Chelub:
27 Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
And over the dressers of the vineyards, was Semeias a Romathite: and over the wine cellars, Zabdias an Aphonite.
28 Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
And over the oliveyards and the fig groves, which were in the plains, was Balanam a Gederite: and over the oil cellars, Joas.
29 Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
And over the herds that fed in Saron, was Setrai a Saronite: and over the. oxen in the valleys, Saphat the son of Adli:
30 Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
And over the camels, Ubil an Ishmahelite: and over the asses, Jadias a Meronathite:
31 Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
And over the sheep Jazia an Agarene. All these were the rulers of the substance of king David.
32 Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
And Jonathan David’s uncle, a counsellor, a wise and learned man: he and Jahiel the son of Hachamoni were with the king’s sons.
33 Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
And Achitophel was the king’s counsellor, and Chusai the Arachite, the king’s friend.
34 Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.
And after Achitophel was Joiada the son of Banaias, and Abiathar. And the general of the king’s army was Joab.

< 1 Mbiri 27 >