< 1 Mbiri 27 >

1 Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
Now the sons of Israel, according to their number, the leaders of the families, the tribunes, and the centurions, and the chiefs, who were ministering to the king by their companies, entering and departing in each month of the year as they were in charge, were twenty-four thousand.
2 Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Jashobeam, the son of Zabdiel, was in charge of the first company in the first month; and under him were twenty-four thousand.
3 Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
He was from the sons of Perez, and he was the leader of all the other leaders in the army, in the first month.
4 Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The company of the second month had Dodai, an Ahohite; and after him there was another, named Mikloth, who ruled over a portion of the army of the twenty-four thousand.
5 Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
Also, the commander of the third company, in the third month, was Benaiah, the son of Jehoiada the priest; and in his division there were twenty-four thousand.
6 Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
The same is the Benaiah who was strongest among the thirty, and was above the thirty. But his son, Ammizabad, was in charge of his company.
7 Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The fourth, for the fourth month, was Asahel, the brother of Joab, and his son Zebadiah after him; and in his company there were twenty-four thousand.
8 Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The fifth leader, for the fifth month, was Shamhuth, an Izrahite; and in his company there were twenty-four thousand.
9 Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The sixth, for the sixth month, was Ira, the son of Ikkesh, a Tekoite; and in his company there were twenty-four thousand.
10 Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The seventh, for the seventh month, was Helez, a Pelonite from the sons of Ephraim; and in his company there were twenty-four thousand.
11 Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
The eighth, for the eighth month, was Sibbecai, a Hushathite from the stock of the Zerahites; and in his company there were twenty-four thousand.
12 Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The ninth, for the ninth month, was Abiezer, an Anathothite from the sons of Benjamin; and in his company there were twenty-four thousand.
13 Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The tenth, for the tenth month, was Maharai, and he was a Netophathite from the stock of the Zerahites; and in his company there were twenty-four thousand.
14 Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The eleventh, for the eleventh month, was Benaiah, a Pirathonite from the sons of Ephraim; and in his company there were twenty-four thousand.
15 Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The twelfth, for the twelfth month, was Heldai, a Netophathite from the stock of Othniel; and in his company there were twenty-four thousand.
16 Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
Now those who were first over the tribes of Israel were these: over the Reubenites, Eliezer, the son of Zichri, was the ruler; over the Simeonites, Shephatiah, the son of Maacah, was the ruler;
17 mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
over the Levites, Hashabiah, the son of Kemuel; over the Aaronites, Zadok;
18 mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
over Judah, Elihu, the brother of David; over Issachar, Omri, the son of Michael;
19 mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
over the Zebulunites, Ishmaiah, the son of Obadiah; over the Naphtalites, Jeremoth, the son of Azriel;
20 mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
over the sons of Ephraim, Hoshea, the son of Azaziah; over the one half tribe of Manasseh, Joel, the son of Pedaiah;
21 mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
and over the one half tribe of Manasseh in Gilead, Iddo, the son of Zechariah; then over Benjamin, Jaasiel, the son of Abner;
22 mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
yet truly, Azarel, the son of Jeroham, was over Dan. These were the leaders of the sons of Israel.
23 Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
But David was not willing to number them from twenty years old and under. For the Lord had said that he would multiply Israel like the stars of heaven.
24 Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
Joab, the son of Zeruiah, had begun to number, but he did not finish. For because of this, wrath had fallen upon Israel. And therefore the number of those who had been counted was not related in the official records of king David.
25 Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
Now over the storerooms of the king was Azmaveth, the son of Adiel. But Jonathan, the son of Uzziah, was over those storerooms that were in the cities, and in the villages, and in the towers.
26 Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
And over the farmlands and the farmers, those who worked the ground, was Ezri, the son of Chelub.
27 Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
And over the cultivators of vineyards was Shimei, a Ramathite; then over the wine cellars was Zabdi, an Aphonite.
28 Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
Now over the olive groves and the fig groves, which were in the plains, was Baal-hanan, a Gederite; and over the oil cellars was Joash.
29 Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
Now over the herds that were pastured in Sharon, Shitrai, a Sharonite, was in the first place; and over the oxen in the valleys, there was Shaphat, the son of Adlai.
30 Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
Truly, over the camels was Obil, an Ishmaelite; and over the donkeys was Jehdeiah, a Meronothite.
31 Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
And over the sheep was Jaziz, a Hagarene. All these were leaders over the substance of king David.
32 Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
Now Jonathan, the uncle of David, was a counselor, a prudent and scholarly man; he and Jehiel, the son of Hachmoni, were with the sons of the king.
33 Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
Now Ahithophel was the counselor of the king; and Hushai, the Archite, was the king’s friend.
34 Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.
After Ahithophel was Jehoiada, the son of Benaiah, and Abiathar. But the leader of the army of the king was Joab.

< 1 Mbiri 27 >