< 1 Mbiri 26 >
1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
Glede na oddelke vratarjev je bil od Kórahovcev Mešelemjá, sin Koréja izmed Asáfovih sinov.
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
Mešelemjájevi sinovi so bili prvorojenec Zeharjá, drugi Jediaél, tretji Zebadjá, četrti Jatniél,
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
peti Elám, šesti Johanán, sedmi Eljoenáj.
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
Poleg tega so bili Obéd Edómovi sinovi prvorojenec Šemajá, drugi Jozabád, tretji Joáh, četrti Sahár, peti Netanél,
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
šesti Amiél, sedmi Isahár in osmi Peuletáj, kajti Bog ga je blagoslovil.
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
Tudi njegovemu sinu Šemajáju so bili rojeni sinovi, ki so vladali po hiši svojih očetov, kajti bili so močni junaški možje.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
Šemajájevi sinovi: Otní, Refaél, Obéd, Elzabád, katerega bratje so bili močni možje, Elihú in Semahjá.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
Vseh teh izmed Obéd Edómovih sinov in njihovih bratov, sposobnih mož za službo je bilo dvainšestdeset.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
Mešelemjá je imel sinove in brate, močne može, osemnajst.
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
Tudi Hosá, izmed Meraríjevih otrok, je imel sinove: vodja Šimrí, (kajti čeprav ni bil prvorojenec, ga je vendar njegov oče naredil za vodjo)
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
drugi Hilkijá, tretji Tebaljá, četrti Zeharjá. Vseh sinov Hosájevih bratov je bilo trinajst.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Med temi so bili oddelki vratarjev, celó med vodilnimi možmi so imeli straže, da služijo eden nasproti drugemu v Gospodovi hiši.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
Metali so žrebe, tako majhni kakor veliki, glede na hišo njihovih očetov, za vsaka velika vrata.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
Žreb proti vzhodu je zadel Šelemjája. Potem so metali žrebe za Zeharjá, njegovega sina, modrega svetovalca in njegov žreb je izšel proti severu.
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
Za Obéd Edóma in za njegove sinove od Asupimove hiše proti jugu.
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Šupímu in Hosáju je žreb izšel proti zahodu z velikimi vrati Šaléheta, pri tlakovani pešpoti vzpona, straža proti straži.
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
Proti vzhodu je bilo šest Lévijevcev, štirje na dan proti severu, štirje na dan proti jugu in proti Asupimu dva in dva.
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
Pri Parbarju proti zahodu, štirje pri tlakovani pešpoti in dva pri Parbarju.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
To so oddelki vratarjev med Koréjevimi sinovi in med Meraríjevimi sinovi.
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
Izmed Lévijevcev je bil Ahíja nad zakladnicami Božje hiše in nad zakladnicami posvečenih stvari.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
Glede Ladánovih sinov: sinovi Geršónca Ladána, poglavarji očetov, celó od Geršónca Ladána, je bil Jehielí.
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
Jehielíjeva sinova: Zetám in njegov brat Joél, ki sta bila nad zakladnicami Gospodove hiše.
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
Izmed Amrámovcev, Jichárovcev, Hebróncev in Uziélovcev
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
je bil Šebuél, Geršómov sin, Mojzesov sin, vladar nad zakladnicami.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
Njegovi bratje po Eliézerju: njegov sin Rehabjá, njegov sin Ješajá, njegov sin Jorám, njegov sin Zihrí in njegov sin Šelomít.
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
Ta Šelomít in njegovi bratje so bili nad vsemi zakladnicami posvečenih stvari, ki so jih kralj David, vodje očetov, tisočniki, stotniki in poveljniki vojske posvetili.
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
Od plenov, dobljenih v bitkah, so jih posvetili za vzdrževanje Gospodove hiše.
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
In vse, kar so videc Samuel, Kišev sin Savel, Nerov sin Abnêr in Cerújin sin Joáb posvetili in kdorkoli je posvetil katerokoli stvar, so bile te pod roko Šelomíta in njegovih bratov.
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
Izmed Jichárovcev so bili Kenanjá in njegovi sinovi za zunanja opravila nad Izraelom, za častnike in sodnike.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
In izmed Hebróncev Hašabjá in njegovi bratje, junaški možje, tisoč sedemsto, so bili častniki med tistimi iz Izraela na tej strani Jordana proti zahodu v vseh Gospodovih opravilih in v kraljevi službi.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
Med Hebrónovci je bil vodja Jerijá, torej med Hebrónovci glede na rodove svojih očetov. V štiridesetem letu Davidovega kraljevanja so jih iskali in med njimi so našli močne junaške može pri Jazêr Gileádu.
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
Njegovih bratov, junaških mož, je bilo dva tisoč in sedemsto vodij očetov, ki jih je David postavil [za] vladarje nad Rubenovci, Gádovci in polovico Manásejevega rodu, za vsako zadevo glede Boga in kraljevih zadev.