< 1 Mbiri 26 >

1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
А редови вратарски беху: од синова Корејевих беше Меселемија син Корејев између синова Асафових;
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
А синови Меселемијини: Захарија првенац, Једаило други, Завадија трећи, Јатнило четврти,
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
Елам пети, Јоанан шести, Елиоинај седми;
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
И Овид-Едомови синови: Семаја првенац, Јозавад други, Јоах трећи и Сихар четврти и Натанаило пети,
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
Амило шести, Исахар седми, Феултај осми; јер га благослови Бог.
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
И Семаји, сину његовом, родише се синови, који старешоваху у дому оца свог, јер беху добри јунаци.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
Синови Семајини: Готније и Рафаило и Овид и Елзавад браћа његова, храбри људи, Елиуј и Семахија.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
Сви ови беху од синова Овид-Едомових, и они и синови њихови и браћа њихова, сви храбри људи, крепки за службу, беше их шездесет и два од Овид-Едома.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
А Меселемијиних синова и браће, храбрих људи, беше осамнаест.
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
А Осини синови, од синова Мераријевих: Симрије поглавар, премда не беше првенац, али га отац постави поглаварем;
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
Хелкија други, Тевалија трећи, Захарија четврти; свих синова и браће Осине беше тринаест.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Од њих беху редови вратарски по поглаварима да чувају стражу наизменце с браћом својом служећи у дому Господњем.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
Јер меташе жреб за малог као и за великог по домовима својих отаца, за свака врата.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
И паде жреб на исток Селимији; а Захарији, сину његовом, мудром саветнику, кад бацише жреб, паде му жреб на север;
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
А Овид-Едому на југ, а синовима његовим на ризницу;
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Суфиму и Оси на запад с вратима салехетским на путу који иде горе; стража беше према стражи:
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
С истока шест Левита; са севера четири на дан; с југа на дан четири; а код ризнице по два;
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
На Парвару са запада четири на путу, два код Парвара.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
То су редови вратарски међу синовима Корејевим и синовима Мераријевим.
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
И ови још беху Левити: Ахија над благом дома Божијег, над благом од посвећених ствари.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
Од синова Ладанових између синова Гирсонових од Ладана, између главара домова отачких од Ладана сина Гирсоновог беше Јехило,
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
Синови Јехилови: Зетам и Јоило брат му беху над благом дома Господњег;
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
Од синова Амрамових, Исарових, Хевронових, Озилових,
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
Беше Севуило, син Гирсона сина Мојсијевог старешина над благом.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
А браћа његова од Елијезера: Реавија син му, а његов син Јесаија, а његов син Јорам, а његов син Зихрије, а његов син Селомит;
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
Овај Селомит и браћа његова беху над свим благом од посвећених ствари, које посвети цар Давид и поглавари домова отачких и хиљадници и стотиници и војводе;
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
Од ратова и од плена посветише да се оправи дом Господњи;
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
И шта год беше посветио Самуило виделац и Саул, син Кисов и Авенир син Ниров и Јоав син Серујин; ко год посвећиваше, даваше у руке Селомиту и браћи његовој.
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
Од синова Исарових: Хенанија и синови његови беху над спољашњим пословима у Израиљу, управитељи и судије.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
Од синова Хевронових Асавија и браћа његова, хиљаду и седам стотина храбрих људи, беху над Израиљем с ове стране Јордана на истоку за сваки посао Господњи и за службу царску.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
Између синова Хевронових беше Јерија, поглавар синовима Хевроновим по породицама њиховим и домовима отачким. Четрдесете године царовања Давидовог потражише их и нађоше међу њима храбрих јунака у Јазиру галадском.
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
И браће његове, храбрих људи, беше две хиљаде и седам стотине главара у домовима отачким; и постави их цар Давид над синовима Рувимовим и Гадовим и половином племена Манасијиног за све послове Божије и царске.

< 1 Mbiri 26 >