< 1 Mbiri 26 >

1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
Co do zmiany odźwiernych: z Korachitów był Meszelemiasz, syn Koracha, z synów Asafa.
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
A z synów Meszelemiasza: pierworodny Zachariasz, drugi Jediael, trzeci Zebadiasz, czwarty Jatniel;
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
Piąty Elam, szósty Jehochanan, siódmy Elioenaj.
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
A z synów Obed-Edoma: pierworodny Szemajasz, drugi Jehozabad, trzeci Joach, czwarty Sakar, piąty Netaneel;
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
Szósty Ammiel, siódmy Issachar, ósmy Peulletaj. Bóg bowiem mu błogosławił.
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
Również jego synowi Szemajaszowi urodzili się synowie, którzy rządzili swoim rodem. [Byli] bowiem bardzo dzielnymi ludźmi.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
Synowie Szemajasza: Otni, Rafael, Obed, Elzabad i ich bracia, ludzie mocni – Elihu i Semakiasz.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
Wszyscy ci byli z synów Obed-Edoma, oni, ich synowie i bracia, mężczyźni bardzo mocni i zdolni do służby, razem sześćdziesięciu dwóch z Obed-Edoma.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
I Meszelemiasz miał synów i braci, ludzi mocnych – osiemnastu.
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
Również Chosa, [który był] z synów Merariego, miał synów: Szimri zwierzchnik, bo chociaż nie był pierworodnym, jego ojciec ustanowił go zwierzchnikiem;
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
Drugi Chilkiasz, trzeci Tebaliasz, czwarty Zachariasz. Wszystkich synów i braci Chosy [było] trzynastu.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Spośród nich wyznaczono zmiany odźwiernych, spośród naczelników, którzy [pełnili] straż na przemian ze swoimi braćmi przy służbie w domu PANA.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
I rzucali losy o każdą bramę, tak mały, jak i wielki, według swoich rodów.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
Los dla Szelemiasza padł na stronę wschodnią. Potem rzucili los dla jego syna Zachariasza, mądrego doradcy, i jego los padł na stronę północną;
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
Dla Obed-Edoma – na południową, a jego synom [przypadła] składnica.
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Dla Szuppima i Chosy – na stronę zachodnią wraz z bramą Szalleket, przy drodze wiodącej ku górze, straż naprzeciw straży.
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
Od wschodu [było] sześciu Lewitów, od północy czterech na dzień, od południa czterech na dzień i przy składnicy po dwóch.
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
Przy Parbar na zachodzie: czterech przy drodze, [a] dwóch przy Parbar.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
Takie [są] zmiany odźwiernych spośród synów Koracha i spośród synów Merariego.
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
A z [pozostałych] Lewitów Achiasz [postawiony był] nad skarbcami domu Bożego i nad skarbcami rzeczy poświęconych.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
Synowie Ladana, [którzy byli] z synów Gerszonity: z Ladana Gerszonity naczelnicy rodów, Jechiel.
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
Synowie Jechiela: Zetam i jego brat Joel; [oni byli postawieni] nad skarbcami domu PANA.
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
Spośród Amramitów, Isharytów, Chebronitów i Uzzielitów:
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
Szebuel, syn Gerszoma, syna Mojżesza, przełożony nad skarbcami.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
A jego bracia, od strony Eliezera, to: jego syn Rechabiasz, jego syn Jeszajasz, jego syn Joram, jego syn Zikri i jego syn Szelomit.
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
Szelomit i jego bracia [byli postawieni] nad wszystkimi skarbcami rzeczy poświęconych, które poświęcił król Dawid, naczelnicy rodów, tysiącznicy, setnicy i dowódcy wojska.
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
[To, co] zdobyli z wojen i łupów, poświęcali na utrzymanie domu PANA.
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
I wszystko, co poświęcił Samuel, widzący, [a także] Saul, syn Kisza, Abner, syn Nera, i Joab, syn Serui, oraz wszystko, co zostało poświęcone, [było] pod opieką Szelomita i jego braci.
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
Spośród Isharytów: Kenaniasz i jego synowie [zajmowali się] sprawami zewnętrznymi Izraela jako urzędnicy i sędziowie.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
Spośród Chebronitów: Chaszabiasz i jego bracia, ludzie dzielni, [było ich] tysiąc siedemset przełożonych nad Izraelem po zachodniej stronie Jordanu, odpowiadali za każdą sprawę PANA i służbę dla króla.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
Spośród Chebronitów [pochodził] Jeriasz, naczelnik Chebronitów, według rodowodów jego ojców. W czterdziestym roku panowania Dawida szukano i znaleziono pośród nich bardzo dzielnych ludzi w Jazer w Gileadzie.
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
A jego braci, ludzi dzielnych, [było] dwa tysiące siedmiuset naczelników rodów, których król Dawid ustanowił zwierzchnikami nad Rubenitami, nad Gadytami i nad połową pokolenia Manassesa, by byli odpowiedzialni za wszystkie sprawy Boże i sprawy króla.

< 1 Mbiri 26 >