< 1 Mbiri 26 >
1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
Izigaba zabalindi bamasango: KwabakoKhora: kunguMeshelemiya indodana kaKhora, omunye wamadodana ka-Asafi.
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
UMeshelemiya wayelamadodana ahlanganisa uZakhariya eyakuqala loJediyeli eyesibili, loZebhadiya eyesithathu, loJathiniyeli eyesine,
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
lo-Elamu eyesihlanu, loJehohanani eyesithupha kanye lo-Eliyehonayi eyesikhombisa.
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
U-Obhedi-Edomi laye wayelamadodana: kunguShemaya eyakuqala, loJehozabhadi eyesibili, loJowa eyesithathu, loSakhari eyesine, loNethaneli eyesihlanu,
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
lo-Amiyeli eyesithupha, lo-Isakhari eyesikhombisa, kanye loPhewulethayi eyesificaminwembili. (Ngoba uNkulunkulu wayembusisile u-Obhedi-Edomi.)
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
Indodana yakhe uShemaya layo yayilamadodana, ayengabakhokheli kwabendlu kayise ngoba babengamadoda enelisayo.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
Amadodana kaShemaya wona yila: ngu-Othini, loRafayeli, lo-Obhedi kanye lo-Elizabhadi; izihlobo zakhe u-Elihu loSemakhiya lazo zazingamadoda ayesenelisa.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
Bonke laba babengabosendo luka-Obhedi-Edomi; bona kanye lamadodana abo lezihlobo zabo babengamadoda enelisayo belamandla okwenza umsebenzi, bengabosendo luka-Obhedi-Edomi, babengamatshumi ayisithupha lambili sebendawonye.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
UMeshelemiya wayelamadodana lezihlobo, amadoda ayekhaliphile ayelitshumi lasificaminwembili esendawonye.
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
UHosa ongumʼMerari wayelamadodana: uShimiri engowakuqala (loba wayengasuye izibulo, uyise wayembeke kulesosikhundla sokuba ngowokuqala),
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
loHilikhiya engowesibili, loThabhaliya engowesithathu kanye loZekhariya engowesine. Amadodana lezihlobo zikaHosa sebendawonye babelitshumi lantathu.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Izigaba zabalindi bamasango, kusiya ngabakhokheli bazo, zazilomlandu wokwenza umsebenzi ethempelini likaThixo, njengokwakusenziwa yizihlobo zabo.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
Benza inkatho isango lilinye, kusiya ngemuli, abatsha labadala kufanana.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
Inkatho yeSango langaseMpumalanga yawela kuShelemiya. Basebesenzela inkatho indodana yakhe uZakhariya owayengumcebisi okhaliphileyo, inkatho yeSango langaseNyakatho yawela kuye.
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
Inkatho yeSango langaseZansi lawela ku-Obhedi-Edomi, amadodana akhe kwathiwa kawalinde isiphala.
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Inkatho yeSango langaseNtshonalanga kanye leSango leShalekhethi emgwaqweni ongaphezulu laya kuShuphimu loHosa. Kwalinda abalindi ngabalindi:
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
Kwakusiba labaLevi abayisithupha ngelanga empumalanga, abane ngelanga enyakatho, abane ezansi ngelanga kuthi esiphaleni kube lababili lakhona ngazozonke izikhathi.
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
Phambili ngentshonalanga, kwakulabane emgwaqweni, ababili besegumeni uqobo.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
Lezi yizigaba zabalindi bamasango ababengabosendo lukaKhora loMerari.
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
Abanye babaLevi babephatha inotho yethempeli likaNkulunkulu leziligugu ezingcwele.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
Abosendo lukaLadani, ababe ngamaGeshoni ngoLadani njalo ababezinhloko zabakaLadani umGeshoni, kwakunguJehiyeli,
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
amadodana kaJehiyeli, loZethami lomfowabo uJoweli. Laba yibo ababephethe inotho yethempeli likaThixo.
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
Kuma-Amramu, ama-Izihari, lamaHebhroni lama-Uziyeli babemi ngalindlela:
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
uShubhayeli, owosendo lukaGeshomu indodana kaMosi, wayeyisikhulu esasiphethe ezenotho.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
Izihlobo zakhe ngo-Eliyezari yilezi: nguRehabhiya indodana yakhe, loJeshaya indodana yakhe, loJoramu indodana yakhe, loZikhiri indodana yakhe loShelomithi indodana yakhe.
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
(UShelomithi lezihlobo zakhe babephethe zonke ezenotho ezingcwele ezazinikelwe yinkosi uDavida, labayizinhloko zezindlu ababengabalawuli bezinkulungwane labalawuli bamakhulu, langabanye abalawuli bamabutho.
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
Eyinye impango eyayithunjwe ekulweni bayinikela ekulungisweni kwethempeli likaThixo.
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
Lakho konke okwakunikelwe nguSamuyeli umboni loSawuli indodana kaKhishi, lo-Abhineri indodana kaNeri loJowabi indodana kaZeruya, lazozonke ezinye ezazinikelwe zazisesandleni sikaShelomithi kanye lezihlobo zakhe.)
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
Kwabaka-Izihari yilaba: UKhenaniya lamadodana akhe baphiwa umsebenzi ngaphandle kwethempeli, beyizikhulu labehluleli kwabako-Israyeli.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
KwabakaHebhroni yilaba: UHashabhiya lezihlobo zakhe, amadoda enelisayo ayengamakhulu alitshumi layisikhombisa ayekhangele ingxenye ka-Israyeli entshonalanga yeJodani kuwo wonke umsebenzi kaThixo lokuba yizinceku zenkosi.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
AmaHebhroni wona, umkhokheli wawo kwakunguJeriya kusiya ngokulotshwa koluhlu lokuzalana kwezimuli zawo. Kwathi ngomnyaka wamatshumi amane wokubusa kukaDavida kwahlolisiswa kuloluluhlu lwemibhalo, kwafunyanwa ukuthi amadoda akhaliphileyo phakathi kwamaHebhroni ayeseJazeri ngaseGiliyadi.
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
UJeriya wayelezihlobo ezingamakhulu angamatshumi amabili lesikhombisa, ezazikhaliphile njalo zizinhloko zezimuli zazo, ngakho inkosi uDavida wazibeka ukuthi ziphathe abakoRubheni, abakoGadi lengxenye yesizwana sikaManase kukho konke okwakungokukaNkulunkulu lokuyizindaba zenkosi.