< 1 Mbiri 26 >
1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
NO na puu ana o na kiaipuka: o na Kora, o Meselemia he keikikane a Kore, no na keiki a Asapa.
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
A o na keikikane a Meselemia; o Zekaria ka makahiapo, o Iediaela ka lua, o Zebadia ke kolu, o Iateniela ka ha,
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
O Elama ka lima, o Iehohanana ke ono, o Elioenai ka hiku.
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
Eia hoi, o na keikikane a Obededoma: o Semaia ka makahiapo, o Iehozabada ka lua, o loa ke kolu, o Sakara ka ha, o Netaneela ka lima,
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
O Amiela ke ono, o Isakara ka hiku, a o Peuletai ka walu: no ka mea, hoopomaikai mai la ke Akua ia ia.
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
Na Semaia hoi, na kana keikikane, ua hanau na keiki; he mau luna lakou mawaena o ka ohana o ko lakou makuakane: no ka mea, he mau kanaka koa ikaika lakou.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
O na keikikane a Semaia; o Oteni, o Repaela, o Obeda, o Elezabada; o na hoahanau o lakou, he mau kanaka ikaika, o Elihu, a o Semakia.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
O keia poe a pau no na keiki a Obededoma: o lakou, o na keikikane a lakou, a me na hoahanau o lakou, na kanaka ikaika e hiki ai ka oihana, he kanaonokumamalua na Obededoma mai.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
Na Meselemia hoi na keikikane a me na hoahanau, na kanaka ikaika, he umikumamawalu:
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
A o Hosa hoi, no na keikikane a Merari, nana mai na keikikane; o Simeri ke pookela, (no ka mea, aole hoi ia o ka hiapo, aka, hoonoho iho la kona makuakane ia ia i pookela; )
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
O Hilekia ka lua, o Tebalia ke kolu, o Zekaria ka ha; o na keikikane a pau a me na hoahanau o Hosa, he umikumamakolu.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Ia lakou i na kanaka pookela, na papa kiaipuka, a he mau puu o lakou e ku pono ana kekahi i kekahi, e lawelawe iloko o ka hale o Iehova.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
A puu iho lakou no ka poe uuku a me ka poe nui, e like me ka ohana o ko lakou mau kupuna, no kela puka, a no keia puka.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
A puka mai la ka puu hikina ia Selemia, Alaila puu iho la lakou no kana keiki no Zekaria, he kakaolelo naauao: a puka mai la ka puu kukulu akau nona.
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
Ia Obededoma ke kukuluhema: a i kana mau keikikane, ka hale ahu waiwai.
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Ia Supima laua o Hosa ke komohana, a me ka puka Saleketa, ma ke alanuipapa o ka pii ana, he puu kiai maanei a he puu kiai ma o.
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
Ma ka hikina he mau Levi aono; ma ke kukuluakau, eha i ka la hookahi; ma ke kukuluhema, eha i ka la hookahi; a ma ka hale ahuwaiwai, elua a elua.
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
Ma Parebara ma ke komohana, eha ma ke alanuipapa, a elua ma Parebara.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
Oia na puu kiaipuka iwaena o na mamo a Kore, a iwaena o na mamo a Merari.
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
A no ka Levi, o Ahiia, maluna ia o na waihona waiwai o ka hale o ke Akua, a maluna o ke ahu o na mea laa.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
No na keikikane a Laadana; o na keikikane a Laadana na Geresona, o na makua'lii a Laadana no Geresona; o Iehieli.
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
O na keikikane a Iehieli; o Zetama a o Ioela kona kaikaina, maluna laua o na waihona waiwai o ka hale o Iehova.
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
No ka Amerama, a no ka Izehara, a no ka Heberona, a no ka Uziela:
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
A o Sebuela ke keiki a Geresoma ke keiki a Mose, oia ka luna o na waihona waiwai.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
A o kona poe hoahanau ma Eliezera; o Rehabia kana keiki, o Iesaia kana keiki, o Iorama kana keiki, o Zikeri kana keiki, a o Selomita kana keiki:
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
O ua Selomita la a me kona poe hoahanau, o lakou maluna o na ahu a pau o na mea laa, a ke alii a Davida me ka na makua'lii, na lunatausani, na lunahaneri, a mo na lunakaua i hoolaa ai.
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
No na waiwaipio i pio i na kaua, ka lakou i hoolaa ai, e kokua i ka hale o Iehova.
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
A o na mea a pau a Samuela ke kaula, laua o Saula ke keiki a Kisa, a me ka Abenera ke keiki a Nora, a me ka Ioaba ke keiki a Zeruia, i hoolaa ai: me ka kela mea keia mea i hoolaa ai, malalo ia o ka lima o Selomita, a o na hoahanau ona.
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
No na Izehara; o Kenania me kana mau keikikane, no na oihana mawaho lakou maluna o ka Iseraela, no na ilamuku a me na lunakanawai.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
No ka Heberona; o Hasabia me kona poe hoahanau, na kanaka koa, hookahi tausani a me na haneri ehiku, he poe luna lakou iwaena o ka Iseraela, ma keia aoao o ka Ioredane ma ke komohana, i na mea a pau a Iehova, a i ka hana a ke alii.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
Iwaena o ka Heberona, o Ieriia ke pookela iwaena o ka Heberona, mamuli o na hanauna o kona poe kupuna. I ke kanaha o ka makahiki o ko Davida alii ana ua imi ia'ku ai lakou, a ua loaa na kanaka koa ikaika iwaena o lakou ma Iazera o Gileada.
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
A o kona poe hoahanau na kanaka koa, elua tausani me na haneri ehiku o na makua'lii, ka poe a Davida i hoonoho ai i poe luna o ka Reubena, ka Gada, a me ka ohana hapa a Manase, no na mea a pau a ke Akua, a me na mea a ke alii.