< 1 Mbiri 26 >

1 Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
This is a list of the groups of men who guarded the temple gates: From the descendants of Korah, there was Meshelemiah, the son of Kore, who was one of the sons of Asaph.
2 Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
The oldest son of Meshelemiah was Zechariah. His other sons were Jediael, Zebadiah, Jathniel,
3 wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
Elam, Jehohanan, and Eliehoenai.
4 Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
[Another guard] was Obed-Edom. His oldest son was Shemaiah. His other sons were Jehozabad, Joah, Sacar, Nethanel,
5 wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
Ammiel, Issachar, and Peullethai. It was because God had blessed him that he had many sons.
6 Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
Obed-Edom’s son Shemaiah also had sons. They were leaders in their father’s family because they were capable of doing many things well.
7 Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
The sons of Shemaiah were Othni, Rephael, Obed, and Elzabad. Shemaiah’s relatives Elihu and Semakiah were also capable men.
8 Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
All of those descendants of Obed-Edom and their sons and relatives were capable people and strong workers. Altogether there were 62 of them.
9 Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
Another guard was Meshelemiah. He and his sons and relatives were also capable people. There were 18 of them altogether.
10 Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
Another guard was Hosah’s son Shimri, a descendant of Merari. Hosah appointed Shimri to be the leader, even though he was not Hosah’s oldest son.
11 wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
Hosah’s other sons were Hilkiah, Tabaliah, and Zechariah. Altogether there were 13 sons and relatives of Hosah.
12 Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
Those men were leaders of the groups of men who guarded the gates of the temple. They worked at the temple like their relatives did.
13 Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
By casting lots, the leader of each family chose one gate for their group to guard. [All of them, including] young men and old men (OR, including leaders of large families and small families), cast lots.
14 Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
Shelemiah’s group was selected to guard the East Gate. The group of Shelemiah’s son Zechariah, who was a wise counselor, was selected to guard the North Gate.
15 Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
Then Obed-Edom’s group was selected to guard the South Gate, and his sons were selected to guard the [entrances to the temple] storerooms.
16 Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
Then Shuppim’s group and Hosah’s group were selected to guard the West Gate and the Shalleketh Gate on the upper road [to the temple]. The work for the guards was divided evenly.
17 Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
Each day there were six descendants of Levi who guarded the East Gate, four who guarded the North Gate, four who guarded the South Gate, and two at a time who guarded the entrances to the storerooms.
18 Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
At the West gate there were two men who guarded the courtyard and four who guarded the road outside the courtyard.
19 Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
Those were the groups of men who were descendants of Korah and Merari who guarded the gates [of the temple].
20 Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
Other descendants of Levi were in charge of the chests that contained the money that was dedicated to Yahweh, money that the people brought to the temple.
21 Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
[One of those men was] Ladan, a descendant of Gershon. He was the ancestor of several family groups. Jehiel was the leader of one of those family groups.
22 ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
Others who had that work were Zetham and his [younger] brother Joel, who were the sons of Jehiel.
23 Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
Others who did that work were descendants of Amram, Izhar, Hebron and Uzziel.
24 Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
[From the descendants of Amram], Shubael, a descendant of Moses’s son Gershom, was the leader who was in charge of the money chests.
25 Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
[Others who did that work were] the descendants of [Gershom’s younger brother] Eliezer. Those men were Eliezer’s son Rehabiah, Rehabiah’s son Jeshaiah, Jeshaiah’s son Joram, Joram’s son Zicri, and Zicri’s son Shelomith.
26 Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
Shelomith and his relatives were in charge of all the valuable things that had been dedicated [to Yahweh] by King David, by the leaders of the family groups, by the army commanders of 1,000 soldiers and commanders of 100 soldiers, and by other army commanders.
27 Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
Some of the things that those army officers had taken [from Israel’s enemies] in battles they dedicated for the repair of the temple of Yahweh.
28 Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
And Shelomith and his relatives were also in charge of everything that had been dedicated [to Yahweh] by the prophet Samuel, by King Saul, and by [David’s two army commanders] Ner and Joab.
29 Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
From the descendants of Izhar, Kenaniah and his sons were given work outside [the temple area]. They were officials and judges in [various places] in Israel.
30 Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
From the descendants of Hebron, Hashabiah and his relatives were responsible for the work done for Yahweh and for the king in all the area west of the Jordan [river]. There were 1,700 of them who were able to do their work well.
31 Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
It was written in the records of the descendants of Hebron that Jeriah was their leader. When David had been ruling for almost 40 years, they searched in those records, and they found [names of] capable men descended from Hebron who were at Jazer [city] in the Gilead [region].
32 Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.
Jeriah had 2,700 relatives who were able to do their work well, and who were leaders of their families. King David put them in charge of governing the tribes of Reuben, Gad, and [the eastern] half of the tribe of Manasseh, to be sure that all the people did what God and the king told them to do.

< 1 Mbiri 26 >