< 1 Mbiri 24 >
1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Ahora, las divisiones en que se agruparon los hijos de Aarón fueron estas: los hijos de Aarón, Nadab y Abiú, Eleazar e Itamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Pero Nadab y Abiú llegaron a su fin antes que su padre, y no tuvieron hijos; así hicieron Eleazar e Itamar el trabajo de los sacerdotes.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
Y David, con Sadoc de los hijos de Eleazar y Ahimelec de los hijos de Itamar, los repartió en sus puestos para su trabajo.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Y hubo más jefes entre los hijos de Eleazar que entre los hijos de Itamar; y así se agruparon: de los hijos de Eleazar había dieciséis, todos jefes de familia; y de los hijos de Itamar, jefes de familia, había ocho.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
Así que fueron agrupados, por decisión del Señor, uno con el otro; porque había gobernantes del lugar santo y gobernantes de la casa de Dios entre los hijos de Eleazar y los hijos de Itamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
Entonces Semaías, hijo de Nethanel, escriba, que era levita, escribió sus nombres por escrito: el rey estaba presente con los gobernantes, y el sacerdote Sadoc, y Ahimelec, hijo de Abiatar, y jefes de familia de los sacerdotes y los levitas; una familia tomada para Eleazar y luego una para Ithamar, y así sucesivamente.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Y el primer nombre que salió fue el de Joiarib; el segundo jedaias;
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
El tercer Harim; el cuarto Seorim;
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
El quinto Malquias; el sexto Mijamin;
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
El séptimo Cos; el octavo Abías;
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
El noveno Jesúa; el décimo Secanías;
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
El undécimo Eliasib; el duodécimo Jaquim;
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
La decimotercera Hupa; el decimocuarto jesebeab;
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
La quinceava Bilga; la decimosexta Imer;
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
El decimoséptimo Hezir; el decimoctavo Afses;
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
El decimonoveno de Petaias; el vigésimo Hezequiel;
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
El vigésimo primero Jaquin; el vigésimo segundo Gamul;
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
El vigésimo tercer Delaía; el vigésimo cuarto Maazías.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Así que fueron puestos en sus diferentes grupos, para tomar sus lugares en la casa del Señor, de acuerdo con las reglas establecidas por su padre Aarón, como el Señor, el Dios de Israel, le había dado órdenes.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Y del resto de los hijos de Leví: de los hijos de Amram, Subael; de los hijos de Subael, Jehdeías.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
De los hijos de Rehabiah, Isias él mayor.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
De los Izhar, Selomot; de los hijos de Selomot, Jahat.
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Y los hijos de Hebrón: Jerías el primero; Amarías, el segundo; Jahaziel el tercero; Jacaman, el cuarto.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
Los hijos de Uziel, Micaia; de los hijos de Miqueas, Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
El hermano de Miqueas, Isias; de los hijos de Isias, Zacarías.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
Los hijos de Merari: Mahli y Musi; Los hijos de Jaazías.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
Los hijos de Merari: de Jaazias, Soham y Zacur e Ibri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
De Mahli: Eleazar, que no tuvo hijos.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
De Cis: los hijos de Kish, Jerahmeel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Y los hijos de Musi: Mahli, Edar y Jerimot. Estos fueron los hijos de los levitas por sus familias.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
La selección se hizo de estos de la misma manera que de sus hermanos, los hijos de Aarón, estando presente David el rey, con Sadoc, y Ahimelec, y los jefes de familia de los sacerdotes y de los levitas.