< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
porro filiis Aaron hae partitiones erunt filii Aaron Nadab et Abiu et Eleazar et Ithamar
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
mortui sunt autem Nadab et Abiu ante patrem suum absque liberis sacerdotioque functus est Eleazar et Ithamar
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
et divisit eos David id est Sadoc de filiis Eleazar et Ahimelech de filiis Ithamar secundum vices suas et ministerium
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
inventique sunt multo plures filii Eleazar in principibus viris quam filii Ithamar divisit autem eis hoc est filiis Eleazar principes per familias sedecim et filiis Ithamar per familias et domos suas octo
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
porro divisit utrasque inter se familias sortibus erant enim principes sanctuarii et principes Dei tam de filiis Eleazar quam de filiis Ithamar
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
descripsitque eos Semeias filius Nathanahel scriba Levites coram rege et principibus et Sadoc sacerdote et Ahimelech filio Abiathar principibus quoque familiarum sacerdotalium et leviticarum unam domum quae ceteris praeerat Eleazar et alteram domum quae sub se habebat ceteros Ithamar
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
exivit autem sors prima Ioiarib secunda Iedeiae
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
tertia Arim quarta Seorim
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
quinta Melchia sexta Maiman
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
septima Accos octava Abia
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
nona Hiesu decima Sechenia
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
undecima Eliasib duodecima Iacim
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
tertiadecima Oppa quartadecima Isbaal
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
quintadecima Belga sextadecima Emmer
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
septimadecima Ezir octavadecima Hapses
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
nonadecima Phetheia vicesima Iezecel
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
vicesima prima Iachin vicesima secunda Gamul
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
vicesima tertia Dalaiau vicesima quarta Mazziau
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
hae vices eorum secundum ministeria sua ut ingrediantur domum Domini et iuxta ritum suum sub manu Aaron patris eorum sicut praecepit Dominus Deus Israhel
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
porro filiorum Levi qui reliqui fuerant de filiis Amram erat Subahel et filiis Subahel Iedeia
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
de filiis quoque Roobiae princeps Iesias
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Isaaris vero Salemoth filiusque Salemoth Iaath
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
filiusque eius Ieriahu Amarias secundus Iazihel tertius Iecmaam quartus
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
filius Ozihel Micha filius Micha Samir
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
frater Micha Iesia filiusque Iesiae Zaccharias
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
filii Merari Mooli et Musi filius Ioziau Benno
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
filius quoque Merari Oziau et Soem et Zacchur et Hebri
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
porro Mooli filius Eleazar qui non habebat liberos
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
filius vero Cis Ierahemel
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
filii Musi Mooli Eder et Ierimoth isti filii Levi secundum domos familiarum suarum
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
miseruntque et ipsi sortes contra fratres suos filios Aaron coram David rege et Sadoc et Ahimelech et principibus familiarum sacerdotalium et leviticarum tam maiores quam minores omnes sors aequaliter dividebat

< 1 Mbiri 24 >