< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Le classi dei figliuoli d’Aaronne furono queste. Figliuoli d’Aaronne: Nadab, Abihu, Eleazar e Ithamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Nadab e Abihu morirono prima del loro padre, e non ebbero figliuoli; Eleazar e Ithamar esercitarono il sacerdozio.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
Or Davide, con Tsadok de’ figliuoli di Eleazar, e con Ahimelec de’ figliuoli d’Ithamar, classificò i figliuoli d’Aaronne secondo il servizio che doveano fare.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Tra i figliuoli di Eleazar si trovarono più capi di famiglie che tra i figliuoli d’Ithamar; e furon divisi così: per i figliuoli di Eleazar, sedici capi di famiglie patriarcali; per i figliuoli d’Ithamar, otto capi delle loro famiglie patriarcali.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
La classificazione fu fatta a sorte, tanto per gli uni quanto per gli altri; perché v’erano dei principi del santuario e de’ principi di Dio tanto tra i figliuoli d’Eleazar quanto tra i figliuoli d’Ithamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
Scemaia, figliuolo di Nathaneel, il segretario, ch’era della tribù di Levi, li iscrisse in presenza del re e dei principi, in presenza del sacerdote Tsadok, di Ahimelec, figliuolo di Ebiathar, e in presenza dei capi delle famiglie patriarcali dei sacerdoti e dei Leviti. Si tirò a sorte una casa patriarcale per Eleazar, e, proporzionalmente, per Ithamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Il primo, designato dalla sorte, fu Jehoiarib; il secondo, Jedaia;
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
il terzo, Harim; il quarto, Seorim;
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
il quinto, Malkija;
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
il sesto, Mijamin; il settimo, Hakkots; l’ottavo, Abija;
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
il nono, Jeshua; il decimo, Scecania;
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
l’undecimo, Eliascib; il dodicesimo, Jakim;
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
il tredicesimo, Huppa; il quattordicesimo, Jescebeab;
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
il quindicesimo, Bilga; il sedicesimo, Immer;
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
il diciassettesimo, Hezir; il diciottesimo, Happitsets;
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
il diciannovesimo, Pethahia; il ventesimo, Ezechiele;
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
il ventunesimo, Jakin; il ventiduesimo, Gamul;
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
il ventitreesimo, Delaia; il ventiquattresimo, Maazia.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Così furono classificati per il loro servizio, affinché entrassero nella casa dell’Eterno secondo la regola stabilita per loro da Aaronne loro padre, e che l’Eterno, l’Iddio d’Israele, gli aveva prescritta.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Quanto al rimanente de’ figliuoli di Levi, questi ne furono i capi. Dei figliuoli d’Amram: Shubael; de’ figliuoli di Shubael: Jehdia.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Di Rehabia, de’ figliuoli di Rehabia: il capo Jscia.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Degli Jtsehariti: Scelomoth; de’ figliuoli di Scelomoth: Jahath.
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Figliuoli di Hebron: Jerija, Amaria il secondo, Jahaziel il terzo, Jekameam il quarto.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
Figliuoli di Uzziel: Mica; de’ figliuoli di Mica: Shamir;
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
fratello di Mica: Jscia; de’ figliuoli d’Jscia: Zaccaria.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
Figliuoli di Merari: Mahli e Musci, e i figliuoli di Jaazia, suo figliuolo,
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
vale a dire i figliuoli di Merari, per il tramite di Jaazia suo figliuolo: Shoham, Zaccur e Ibri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Di Mahli: Eleazar, che non ebbe figliuoli.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Di Kis: i figliuoli di Kis: Jerahmeel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Figliuoli di Musci: Mahli, Eder e Jerimoth. Questi sono i figliuoli dei Leviti secondo le loro case patriarcali.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
Anch’essi, come i figliuoli d’Aaronne, loro fratelli, tirarono a sorte in presenza del re Davide, di Tsadok, di Ahimelec e dei capi delle famiglie patriarcali dei sacerdoti e dei Leviti. Ogni capo di famiglia patriarcale tirò a sorte, nello stesso modo che il fratello, più giovane di lui.

< 1 Mbiri 24 >