< 1 Mbiri 24 >
1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
OR quant'è a' figliuoli d'Aaronne, i loro spartimenti [furono questi]: I figliuoli d'Aaronne [furono] Nadab, ed Abihu, Eleazaro, ed Itamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Ed essendo Nadab ed Abihu morti senza figliuoli davanti al padre loro, Eleazaro ed Itamar esercitaroro il sacerdozio.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
Or Davide li distribuì secondo gli ordini loro nel lor ministerio, [essendo] Sadoc de' figliuoli di Eleazaro, ed Ahimelec de' figliuoli d'Itamar.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Ed i figliuoli di Eleazaro si trovarono in più gran numero di capi d'uomini, che i figliuoli di Itamar, quando gli spartimenti furono fatti. De' figliuoli di Eleazaro [vi erano] sedici capi di famiglie paterne, e de' figliuoli d'Itamar otto.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
E gli spartimenti furono fatti a sorte, gli uni per mezzo gli altri; perciocchè anche i capi del santuario, e [della Casa] di Dio, erano de' figliuoli di Eleazaro, e de' figliuoli d'Itamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
E Semaia, figliuolo di Natanael, Scriba, [della tribù] di Levi, li descrisse davanti al re, e davanti a' capi [del popolo], ed al sacerdote Sadoc, e ad Ahimelec, figliuolo di Ebiatar, ed a' capi delle [famiglie] paterne de' sacerdoti, e de' Leviti; una casa paterna si prendeva [de' discendenti] di Eleazaro, ed un'[altra congiuntamente di que]'d'Itamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
La prima sorte adunque scadde a Ioiarib, la seconda a Iedaia,
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
la terza ad Harim, la quarta a Seorim,
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
la quinta a Malchia,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
la sesta a Miamin, la settima a Cos, l'ottava ad Abia,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
la nona a Iesua, la decima a Secania,
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
l'undecima ad Eliasib, la duodecima a Iachim,
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
la tredicesima ad Huppa, la quartadecima a Iesebeab,
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
la quintadecima a Bilga, la sestadecima ad Immer,
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
la diciassettesima ad Hezir, la diciottesima a Pisses,
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
la diciannovesima a Petahia, la ventesima ad Ezechiele,
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
la ventunesima a Iachin, la ventiduesima a Gamul,
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
la ventesimaterza a Delaia, la ventiquattresima a Maazia.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Questi [furono] i loro ordini nel lor ministerio, [secondo i quali aveano] da venir nella Casa del Signore, secondo che era loro ordinato, sotto la condotta di Aaronne, lor padre; come il Signore Iddio d'Israele gli avea comandato.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
E QUANT'è al rimanente de' figliuoli di Levi, de' figliuoli di Amram, [vi fu] Subael; e de' figliuoli di Subael, Iedeia.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Quant'è a' figliuoli di Rehabia, Isia [fu] il capo.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Degl'Ishariti, Selomot; de' figliuoli di Selomot, Iahat.
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
[De' figliuoli di Hebron, Ieria era il primo], Amaria il secondo, Iahaziel il terzo, Iecamam il quarto.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
De' figliuoli di Uzziel [fu capo] Mica; de' figliuoli di Mica, Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
Il fratello di Mica [fu] Isia; de' figliuoli d'Isia, Zaccaria [fu il capo].
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
I figliuoli di Merari[furono] Mehali, e Musi; e de' figliuoli di Iaazia, Beno [fu il capo].
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
I figliuoli di Merari, per Iaazia, [furono] Beno, e Soham, e Zaccur, ed Ibri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Di Mahali [il capo fu] Eleazaro, il quale non ebbe figliuoli.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Quant'è a Chis, [il capo de]'suoi figliuoli [fu] Ierameel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
E de' figliuoli di Musi [furono i capi] Mahali, ed Eder, e Ierimot. Questi [furono] i figliuoli de' Leviti, secondo le lor case paterne.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
E tirarono anch'essi le sorti, al pari de' figliuoli d'Aaronne, lor fratelli, in presenza del re Davide, e di Sadoc, e d'Ahimelec, e de' capi delle [famiglie] paterne de' sacerdoti, e de' Leviti; le principali delle [case] paterne [essendo] pareggiate ad [altre più] piccole de' lor fratelli.