< 1 Mbiri 24 >
1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Or voici quelle fut la classification des fils d’Aaron. Les fils d’Aaron étaient Nadab, Abiu, Eléazar et Ithamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Mais Nadab et Abiu moururent avant leur père, sans enfants; et Eléazar et Ithamar exercèrent les fonctions du sacerdoce.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
David les divisa donc, c’est-à-dire Sadoc, d’entre les fils d’Eléazar, et Ahimélech, d’entre les fils d’Ithamar, selon leurs classes et leur ministère.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Mais il se trouva beaucoup plus de fils d’Eléazar parmi les princes, que de fils d’Ithamar. Il leur répartit donc, savoir: aux fils d’Eléazar, seize princes, selon leurs familles, et aux fils d’Ithamar, selon leurs familles et leurs maisons, huit.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
Il partagea encore l’une et l’autre famille au sort; car il y avait des princes du sanctuaire, et des princes de Dieu, tant d’entre les fils d’Eléazar, que d’entre les fils d’Ithamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
Séméias, fils de Nathanaël, le scribe de la tribu de Lévi, les enregistra devant le roi, les princes, Sadoc, le prêtre, Ahimélech, fils d’Abiathar, et devant les princes des familles sacerdotales et lévitiques, prenant une maison qui était à la tête des autres, celle d’Eléazar, et une autre maison qui avait sous elle les autres, celle d’Ithamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Ainsi le premier sort sortit pour Joïarib; le second, pour Jédéi;
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
Le troisième, pour Harim; le quatrième, pour Séorim;
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
Le cinquième, pour Melchia; le sixième, pour Maïman;
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
Le septième, pour Accos; le huitième, pour Abia;
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
Le neuvième, pour Jésua; le dixième, pour Séchénia;
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
Le onzième, pour Eliasib; le douzième, pour Jacim;
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
Le treizième, pour Hoppha; le quatorzième, pour Isbaab;
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
Le quinzième, pour Belga; le seizième, pour Emmer;
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
Le dix-septième, pour Hézir; le dix-huitième, pour Aphsès;
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
Le dix-neuvième, pour Phétéia; le vingtième, pour Hézéchiel;
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
Le vingt-unième, pour Jachin; le vingt-deuxième, pour Gamul;
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
Le vingt-troisième, pour Dalaïau; le vingt-quatrième, pour Maaziaü.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Telles sont leurs classes, selon leurs fonctions, afin qu’ils entrent dans la maison du Seigneur suivant le rite qui leur est prescrit, sous la main d’Aaron leur père, comme avait ordonné le Seigneur Dieu d’Israël.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Quant aux autres fils de Lévi, d’entre les fils d’Amram, était Subaël, et d’entre les fils de Subaël, Jéhédéia.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
De plus, d’entre les fils de Rohobia, le prince Jésias.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Or le fils d’Isaar était Salémoth, et le fils de Salémoth, Jaath,
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Dont le fils Jériaü fut le premier; Amarias, le second; Jahaziel, le troisième; Jecmaan, le quatrième.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
Le fils d’Oziel, Micha; le fils de Micha, Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
Le frère de Micha était Jésia, et le fils de Jésia, Zacharie;
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
Les fils de Mérari, Moholi et Musi; le fils d’Osiaü, Benno.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
Le fils de Mérari fut encore Oziaü, ainsi que Soam, Zachur et Hébri;
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Mais le fils de Moholi fut Eléazar, qui n’eut point d’enfants;
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Et le fils de Cis, Jéraméel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Les fils de Musi furent Moholi, Eder et Jérimoth. Ce sont là les fils de Lévi, selon les maisons de leurs familles.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
Or ceux-ci aussi, tant les grands que les petits, jetèrent les sorts, comme leurs frères, les fils d’Aaron, devant David, le roi, et devant Sadoc, Ahimélech, et les princes des familles sacerdotales et lévitiques: le sort les partagea tous également.