< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Now these were the divisions of the sons of Aaron: The sons of Aaron: Nadab, and Abiu, and Eleazar, and Ithamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
But Nadab and Abiu died before their father, and had no children: so Eleazar, and Ithamar did the office of the priesthood.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
And David distributed them, that is, Sadoc of the sons of Eleazar, and Ahimelech of the sons of Ithamar, according to their courses and ministry.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
And there were found many more of the sons of Eleazar among the principal men, than of the sons of Ithamar. And he divided them so, that there were of the sons of Eleazar, sixteen chief men by their families: and of the sons of Ithamar eight by their families and houses.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
And he divided both the families one with the other by lot: for there were princes of the sanctuary, and princes of God, both of the sons of Eleazar, and of the sons of Ithamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
And Semeias the son of Nathanael the scribe a Levite, wrote them down before the king and the princes, and Sadoc the priest, and Ahimelech the son of Abiathar, and the princes also of the priestly and Levitical families: one house, which was over the rest, of Eleazar: and another house, which had the rest under it, of Ithamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Now the first lot came forth to Joiarib, the second to Jedei,
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
The third to Harim, the fourth to Seorim,
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
The fifth to Melchia, the sixth to Maiman,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
The seventh to Accos, the eighth to Abia,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
The ninth to Jesua, the tenth to Sechenia,
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
The eleventh to Eliasib, the twelfth to Jacim,
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
The thirteenth to Hoppha, the fourteenth to Isbaab,
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
The fifteenth to Belga, the sixteenth to Emmer,
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
The seventeenth to Hezir, the eighteenth to Aphses,
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
The nineteenth to Pheteia, the twentieth to Hezechiel,
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
The one and twentieth to Jachin, the two and twentieth to Gamul,
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
The three and twentieth to Dalaiau, the four and twentieth to Maaziau.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
These are their courses according to their ministries, to come into the house of the Lord, and according to their manner under the hand of Aaron their father: as the Lord the God of Israel had commanded.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Now of the rest of the sons of Levi, there was of the sons of Amram, Subael: and of the sons of Subael, Jehedeia.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Also of the sons of Rohobia the chief Jesias.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
And the son of Isaar Salemoth, and the son of Salemoth Jahath:
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
And his son Jeriau the first, Amarias the second, Jahaziel the third, Jecmaan the fourth.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
The son of Oziel, Micha: the son of Micha, Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
The brother of Micha, Jesia: and the son of Jesia, Zacharias.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
The sons of Merari: Moholi and Musi: the son of Oziau: Benno.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
The son also of Merari: Oziau, and Seam, and Zacchur, and Hebri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
And the son of Moholi: Eleazar, who had no sons.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
And the son of Cis, Jeramael.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
The sons of Musi: Moholi, Eder, and Jerimoth. These are the sons of Levi according to the houses of their families.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
And they also cast lots over against their brethren the sons of Aaron before David the king, and Sadoc, and Ahimelech, and the princes of the priestly and Levitical families, both the elder and the younger. The lot divided all equally.

< 1 Mbiri 24 >