< 1 Mbiri 24 >
1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Now these were the divisions of the sons of Aaron. The sons of Aaron: Nadab, and Abihu, and Eleazar, and Ithamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
But Nadab and Abihu died before their father, and without children. And so Eleazar and Ithamar exercised the priestly office.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
And David distributed them, that is, Zadok of the sons of Eleazar, and Ahimelech of the sons of Ithamar, according to their courses and ministry.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
And there were found many more of the sons of Eleazar among the leading men, than of the sons of Ithamar. Therefore, he divided them so that there were, of the sons of Eleazar, sixteen leaders by their families, and of the sons of Ithamar eight by their families and houses.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
Then he divided among them, in both families, by lot. For there were leaders of the sanctuary and leaders of God, as much from the sons of Eleazar as from the sons of Ithamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
And the scribe Shemaiah, the son of Nethanel, a Levite, wrote these down before the king and the leaders, with Zadok, the priest, and Ahimelech, the son of Abiathar, and also the leaders of the priestly and Levitical families. And there was one house, which was preeminent over the others, that of Eleazar; and there was another house, which had the others under it, that of Ithamar.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Now the first lot went forth to Jehoiarib, the second to Jedaiah,
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
the third to Harim, the fourth to Seorim,
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
the fifth to Malchijah, the sixth to Mijamin,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
the seventh to Hakkoz, the eighth to Abijah,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
the ninth to Jeshua, the tenth to Shecaniah,
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
the eleventh to Eliashib, the twelfth to Jakim,
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
the thirteenth to Huppah, the fourteenth to Jeshebeab,
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
the fifteenth to Bilgah, the sixteenth to Immer,
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
the seventeenth to Hezir, the eighteenth to Happizzez,
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
the nineteenth to Pethahiah, the twentieth to Jehezkel,
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
the twenty-first to Jachin, the twenty-second to Gamul,
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
the twenty-third to Delaiah, the twenty-fourth to Maaziah.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
These were their courses according to their ministries, so that they would enter into the house of the Lord in accord with their practice, under the hand of Aaron, their father, just as the Lord, the God of Israel, had instructed.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Now of the sons of Levi who were remaining, there were Shubael, from the sons of Amram, and Jehdeiah, from the sons of Shubael.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Also, there were Isshiah, the leader from the sons of Rehabiah,
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
and truly Shelomoth, the son of Izhar, and Jahath, the son of Shelomoth,
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
and his son, Jeriah the first, Amariah the second, Jahaziel the third, Jekameam the fourth.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
The son of Uzziel was Micah. The son of Micah was Shamir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
The brother of Micah was Isshiah. And the son of Isshiah was Zechariah.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
The sons of Merari were Mahli and Mushi. The son of Uzziah was Beno.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
Also, the son of Merari: Uzziah, and Shoham, and Zaccur, and Hebri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
In addition, the son of Mahli was Eleazar, who had no children.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Truly, the son of Kish was Jerahmeel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
The sons of Mushi were Mahli, Eder, and Jerimoth. These were the sons of Levi according to the houses of their families.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
And they also cast lots concerning their brothers, the sons of Aaron, before David the king, and Zadok, and Ahimelech, and the leaders of the priestly and Levitical families, as much concerning the elder as the younger. The lot divided all things equitably.