< 1 Mbiri 23 >
1 Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
Ya David era viejo y lleno de días, y puso a Salomón, su hijo, como rey de Israel.
2 Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
Reunió a todos los príncipes de Israel, con los sacerdotes y los levitas.
3 Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
Los levitas fueron contados de treinta años en adelante, y su número por sus encuestas, hombre por hombre, era de treinta y ocho mil.
4 Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
David dijo: “De ellos, veinticuatro mil estaban para supervisar la obra de la casa de Yahvé, seis mil eran oficiales y jueces,
5 Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
cuatro mil eran porteros, y cuatro mil alababan a Yahvé con los instrumentos que yo hacía para dar alabanza.”
6 Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
David los dividió según los hijos de Leví: Gersón, Coat y Merari.
7 Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
De los gersonitas: Ladán y Simei.
8 Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
Los hijos de Ladán: Jehiel el principal, Zetham y Joel, tres.
9 Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
Los hijos de Simei: Selomot, Haziel y Harán, tres. Estos fueron los jefes de familia de Ladán.
10 Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
Los hijos de Simei: Jahat, Zina, Jeús y Beriá. Estos cuatro fueron los hijos de Simei.
11 Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
Jahat fue el jefe, y Zina el segundo; pero Jeús y Beriá no tuvieron muchos hijos, por lo que se convirtieron en una casa paterna en un conteo.
12 Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
Los hijos de Coat: Amram, Izhar, Hebrón y Uziel, cuatro.
13 Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
Los hijos de Amram: Aarón y Moisés; y Aarón fue separado para que santificara las cosas más santas, él y sus hijos para siempre, para quemar incienso ante Yahvé, para servirle y para bendecir en su nombre para siempre.
14 Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
En cuanto a Moisés, el hombre de Dios, sus hijos fueron nombrados en la tribu de Leví.
15 Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
Los hijos de Moisés: Gersón y Eliezer.
16 Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
Los hijos de Gersón: Sebuel, el jefe.
17 Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
El hijo de Eliezer fue Rehabía, el jefe; y Eliezer no tuvo más hijos, pero los hijos de Rehabía fueron muy numerosos.
18 Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
El hijo de Izhar: Selomit, el jefe.
19 Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Los hijos de Hebrón: Jeria el principal, Amarías el segundo, Jahaziel el tercero y Jekam el cuarto.
20 Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
Los hijos de Uziel: Miqueas, el primero, e Isías, el segundo.
21 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
Los hijos de Merari: Mahli y Mushi. Los hijos de Mahli: Eleazar y Kish.
22 Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
Eleazar murió y no tuvo hijos, sino sólo hijas; y sus parientes, los hijos de Cis, las tomaron como esposas.
23 Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
Los hijos de Mushi: Mahli, Eder y Jeremot, tres.
24 Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
Estos fueron los hijos de Leví según las casas paternas, los jefes de las casas paternas de los que fueron contados individualmente, en el número de nombres por sus encuestas, que hicieron el trabajo para el servicio de la casa de Yahvé, de veinte años en adelante.
25 Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
Porque David dijo: “Yahvé, el Dios de Israel, ha dado descanso a su pueblo; y él habita en Jerusalén para siempre.
26 sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
También los levitas ya no necesitarán llevar el tabernáculo y todos sus utensilios para su servicio.”
27 Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
Porque por las últimas palabras de David fueron contados los hijos de Leví, de veinte años para arriba.
28 Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
Porque el deber de ellos era servir a los hijos de Aarón para el servicio de la casa de Yahvé: en los atrios, en las habitaciones y en la purificación de todas las cosas santas, en la obra del servicio de la casa de Dios;
29 Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
también para el pan de la proposición y para la harina fina para la ofrenda, ya sea de obleas sin levadura, o de la que se cuece en la sartén, o de la que se remoja, y para todas las medidas de cantidad y tamaño;
30 Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
y que se pusieran de pie cada mañana para dar gracias y alabar a Yahvé, y lo mismo al atardecer;
31 ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
y que ofrecieran todos los holocaustos a Yahvé en los sábados, en las lunas nuevas y en las fiestas señaladas, en número conforme a la ordenanza relativa a ellas, continuamente ante Yahvé;
32 Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.
y que cumplieran con el deber de la Tienda de Reunión, el deber del lugar santo y el deber de los hijos de Aarón sus hermanos para el servicio de la casa de Yahvé.