< 1 Mbiri 23 >

1 Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
Der David var gammel og mæt af Dage, da gjorde han Salomo, sin Søn, til Konge over Israel.
2 Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
Og han samlede alle Israels Fyrster, Præsterne og Leviterne.
3 Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
Og Leviterne bleve talte fra tredive Aar gamle og derover, og deres Tal var, Hoved for Hoved, Mand for Mand, otte og tredive Tusinde.
4 Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
Af dem skal der til at forestaa Gerningen ved Herrens Hus være fire og tyve Tusinde, og til Fogeder og Dommere seks Tusinde;
5 Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
og fire Tusinde til Portnere og fire Tusinde til at love Herren med Instrumenterne, som jeg har gjort til Lovsangen.
6 Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
Og David delte dem i Skifter efter Levis Sønner, Gerson, Kahath og Merari.
7 Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
Af Gersoniterne vare Ladan og Simei.
8 Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
Ladans Sønner vare: Jehiel den første og Setham og Joel, i alt tre.
9 Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
Simeis Sønner vare: Selomith og Hasiel og Haran, i alt tre; disse vare Øverster for Ladans Fædrenehuse.
10 Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
Og Simeis Sønner vare: Jahath, Sisa og Jeus og Beria; disse fire vare Simeis Sønner.
11 Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
Og Jahath var den første og Sisa den anden; men Jeus og Beria havde ikke mange Sønner, derfor bleve de regnede for eet Fædrenehus.
12 Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
Kahaths Sønner vare: Amram, Jizehar, Hebron og Ussiel, i alt fire.
13 Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
Amrams Sønner vare: Aron og Mose; og Aron blev udtagen til at hellige det Højhellige, han og hans Sønner til evig Tid, til at gøre Røgelse for Herrens Ansigt, til at tjene ham og at velsigne i hans Navn til evig Tid.
14 Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
Men Mose, den Guds Mand, hans Sønner regnedes til Levi Stamme.
15 Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
Moses Sønner vare: Gersom og Elieser.
16 Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
Og Gersoms Sønner vare: Sebuel den første.
17 Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
Og Eliesers Sønner vare: Rehabia den første; og Elieser havde ikke andre Sønner, men Rehabias Børn formerede sig overmaade.
18 Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
Jizehars Sønner vare: Selomith den første.
19 Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Hebrons Sønner vare: Jerija den første, Amaria den anden, Jehasiel den tredje og Jekameam den fjerde.
20 Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
Ussiels Sønner vare: Mika den første, Jesija den anden.
21 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
Meraris Sønner vare: Maheli og Mufi; Mahelis Sønner vare: Eleasar og Kis.
22 Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
Og Eleasar døde og havde ingen Sønner, men Døtre; men Kis's Sønner, deres Brødre, toge dem til Ægte.
23 Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
Musis Sønner vare: Maheli og Eder og Jeremoth, i alt tre.
24 Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
Disse ere Levis Børn efter deres Fædres Hus, Fædrenehusenes Øverster, som bleve regnede efter Navnes Tal, efter deres Hoveder, og som gjorde Gerningen til Herrens Hus's Tjeneste, fra tyve Aar gamle og derover.
25 Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
Thi David havde sagt: Herren, Israels Gud, har skaffet sit Folk Rolighed, og det skal bo i Jerusalem ind til evig Tid,
26 sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
og Leviterne behøve heller ikke at bære Tabernaklet eller noget af dets Redskaber, som høre til dets Tjeneste.
27 Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
Thi efter Davids sidste Ord vare de, som udgjorde Tallet af Levis Børn, de fra tyve Aar gamle og derover.
28 Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
Thi de bleve satte ved Siden af Arons Børn til Herrens Hus's Tjeneste, over Forgaardene og over Kamrene og over alle Haande hellige Tings Renselse og til Gerning ved Guds Hus's Tjeneste
29 Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
og ved Skuebrødene og ved Melet til Madofferet og til de usyrede, tynde Kager og ved Panden og ved det, som æltedes, og ved Hulmaal og Længdemaal
30 Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
og til at staa hver Morgen for at takke og for at love Herren og ligesaa om Aftenen
31 ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
og til at ofre Herren alle Brændofre paa Sabbaterne, paa Nymaanederne og paa de bestemte Højtider efter Tal, som deres Vis var, idelig for Herrens Ansigt.
32 Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.
Og de skulde tage Vare paa, hvad der var at varetage ved Forsamlingens Paulun, og paa hvad der var at varetage ved Helligdommen, og paa hvad der var at varetage for Arons Børn, deres Brødre, til Herrens Hus's Tjeneste.

< 1 Mbiri 23 >