< 1 Mbiri 21 >
1 Satana anafuna kuvutitsa Aisraeli choncho anawutsa mtima wa Davide kuti awerenge Aisraeli.
Or Satan s’éleva contre Israël, et excita David à dénombrer Israël.
2 Choncho Davide anati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, “Pitani mukawerenge Aisraeli kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani. Ndipo mudzandiwuze kuti ndidziwe chiwerengero chawo.”
Et David dit à Joab et aux princes du peuple: Allez, et dénombrez Israël, depuis Bersabée jusqu’à Dan, et apportez-moi le nombre, afin que je le sache.
3 Yowabu anayankha kuti, “Yehova achulukitse ankhondo ake kukhala miyandamiyanda. Mbuye wanga mfumu, kodi anthu onsewa sali pansi panu? Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukufuna kuchita zimenezi? Nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwitsa Israeli?”
Et Joab répondit: Que le Seigneur accroisse son peuple au centuple de ce qu’il est: est-ce, mon seigneur roi, que tous ne sont pas vos serviteurs? Pourquoi mon seigneur recherche-t-il ce qui sera imputé à péché à Israël?
4 Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu, kotero Yowabu anapita mu Israeli monse ndipo kenaka anabwera ku Yerusalemu.
Mais la parole du roi prévalut, et Joab sortit et parcourut tout Israël, et il revint à Jérusalem.
5 Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda.
Et il donna à David le nombre de tous ceux qu’il avait visités, et le nombre total d’Israël se trouva onze cent mille hommes d’Israël, tous tirant le glaive; mais de Juda, quatre cent soixante-dix mille guerriers.
6 Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira.
Car, pour Lévi et Benjamin, Joab ne les dénombra point, parce que c’était à regret qu’il exécutait l’ordre du roi.
7 Lamulo limeneli silinakomerenso Mulungu. Kotero Iye analanga Israeli.
En effet, ce qui avait été commandé déplut à Dieu, et il frappa Israël.
8 Choncho Davide anati kwa Mulungu, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
Et David dit à Dieu: J’ai péché grièvement en faisant cela. Je vous conjure, effacez l’iniquité de votre serviteur, parce que j’ai agi en insensé.
9 Yehova anati kwa Gadi, mlosi wa Davide,
Alors le Seigneur parla à Gad, le Voyant de David, disant:
10 “Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
Va et parle à David, et dis-lui: Voici ce que dit le Seigneur: Je te donne l’option de trois choses; choisis celle que tu voudras, et je te la ferai.
11 Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa Iye, “Yehova akuti, ‘Musankhepo chimene mungakonde kuti chichitike:
Lors donc que Gad fut venu vers David, il lui dit: Voici ce que dit le Seigneur: Choisis ce que tu voudras:
12 mʼdziko mukhale njala zaka zitatu, mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu, akukukanthani ndi lupanga la Yehova, kapena mʼdziko mukhale mliri kwa masiku atatu, mngelo wa Yehova akuwononga Israeli yense.’ Ndipo tsono ganizirani bwino chomwe ndikamuyankhe amene wandituma.”
Ou, durant trois ans, une famine; ou, durant trois mois, fuir devant les ennemis et ne pouvoir pas éviter leur glaive; ou que, pendant trois jours, le glaive du Seigneur et une peste règnent dans le pays, et qu’un ange du Seigneur tue dans tous les confins d’Israël. Maintenant donc, vois ce que je dois répondre à celui qui m’a envoyé.
13 Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ine andilange ndi Yehova, pakuti chifundo chake ndi chachikulu kwambiri; koma ndisalangidwe ndi anthu.”
Et David dit à Gad: De toutes parts les angoisses me pressent; mais il vaut mieux pour moi que je tombe dans les mains du Seigneur (parce que ses miséricordes sont sans nombre), que dans les mains des hommes,
14 Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000.
Le Seigneur envoya donc une peste en Israël, et il mourut d’Israël soixante-dix mille hommes.
15 Ndipo Mulungu anatumiza mngelo kuti awononge Yerusalemu. Koma pamene mngeloyo amachita zimenezi, Yehova anaona ndipo anavutika mu mtima chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
Il envoya aussi un ange à Jérusalem pour la frapper; et, lorsqu’elle était frappée, le Seigneur le vit, et fut touché de compassion à cause de la grandeur du mal; il commanda donc à l’ange qui frappait: Il suffit; qu’à l’instant ta main s’arrête. Or l’ange du Seigneur se tenait alors près de l’aire d’Ornan, le Jébuséen.
16 Davide anakweza maso ake ndipo anaona mngelo wa Yehova atayima pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, mʼdzanja lake muli lupanga lotambalitsa kuloza ku Yerusalemu. Ndipo Davide ndi akuluakulu, atavala ziguduli, anadzigwetsa pansi chafufumimba.
Et David, levant ses yeux, vit l’ange du Seigneur debout entre le ciel et la terre, et un glaive nu en sa main, et tourné contre Jérusalem; alors lui aussi bien que les anciens, revêtus de cilices, tombèrent inclinés vers la terre.
17 Davide anati kwa Mulungu, “Kodi si ine amene ndinalamula kuti ankhondo awerengedwe? Ine mʼbusa ndi amene ndachimwa, ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Inu Yehova Mulungu wanga, langani ineyo pamodzi ndi banja langa, koma musalole kuti mliriwu ukhale pa anthu anuwa.”
Et David dit à Dieu: N’est-ce pas moi qui ai commandé de dénombrer le peuple? C’est moi qui ai péché; c’est moi qui ai fait le mal; mais ce troupeau, qu’a-t-il mérité? Seigneur mon Dieu, je vous conjure, que votre main se tourne contre moi et contre la maison de mon père; mais que votre peuple ne soit pas frappé.
18 Pamenepo mngelo wa Yehova analamula Gadi kuti awuze Davide kuti akamange guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
Or l’ange du Seigneur ordonna à Gad de dire à David qu’il montât et dressât un autel au Seigneur Dieu dans l’aire d’Ornan, le Jébuséen.
19 Ndipo Davide anapita pomvera mawu amene Gadi ananena mʼdzina la Yehova.
David monta donc, suivant la parole que Gad lui avait dite au nom du Seigneur.
20 Pamene Arauna ankapuntha tirigu, anatembenuka ndipo anaona mngelo ndipo ana ake anayi aamuna amene anali naye anabisala.
Mais lorsqu’Ornan eut levé les yeux, et qu’il eut vu l’ange du Seigneur, ainsi que ses quatre fils, ils se cachèrent; car, en ce moment-là, il battait du blé dans son aire.
21 Davide anayandikira, ndipo Arauna atayangʼana ndi kumuona, anachoka popunthira tirigupo ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi pamaso pa Davide.
Lors donc que David venait vers Ornan, Ornan l’aperçut, et s’avança de l’aire au-devant de lui, puis se prosterna devant lui, incliné vers la terre.
22 Davide anati kwa Arauna, “Undipatse malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe, kuti mliri uli pa anthuwa usiye. Undigulitse ine pa mtengo woyenera ndithu.”
Et David lui dit: Donne-moi la place de ton aire, afin que j’y bâtisse un autel au Seigneur; en sorte que tu reçoives autant d’argent qu’elle vaut, et que la plaie soit détournée du peuple.
23 Arauna anati kwa Davide, “Tengani! Mbuye wanga mfumu achite chomukomera. Taonani ine ndidzapereka ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, zopunthira tirigu zidzakhala nkhuni ndipo tiriguyu adzakhala chopereka chachakudya. Ndidzapereka zonsezi.”
Or Ornan répondit à David: Prenez, et que mon seigneur le roi fasse ce qui lui plaît: et je lui donne aussi les bœufs pour l’holocauste, les herses pour le bois, et le blé pour le sacrifice; je lui donne tout cela avec plaisir.
24 Koma mfumu Davide inayankha Arauna kuti, “Ayi, ine ndikuti ndipereka mtengo wathunthu. Sindingatenge chinthu chako ndi kuchipereka kwa Yehova, kapena kupereka nsembe imene sindinayigule.”
Et le roi David lui dit: Pas du tout, la chose ne se fera point ainsi, mais je donnerai autant d’argent qu’elle en vaut; car je ne dois pas te l’ôter, et offrir ainsi au Seigneur des holocaustes qui ne me coûtent rien.
25 Choncho Davide analipira Arauna masekeli agolide 600 chifukwa cha malowo.
David donna donc à Ornan, pour la place de l’aire, six cents sicles d’or d’un poids très juste.
26 Davide anamangira Yehova guwa lansembe pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Iye anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anayankha potumiza moto pa guwa lansembe zopsereza kuchokera kumwamba.
Et il bâtit là un autel au Seigneur, et il offrit des holocaustes et des sacrifices pacifiques; et il invoqua le Seigneur, qui l’exauça par le moyen du feu descendu du ciel sur l’autel de l’holocauste.
27 Tsono Yehova anayankhula kwa mngelo, ndipo analowetsa lupanga lake mʼchimake.
Et le Seigneur ordonna à l’ange, et il remit son glaive dans le fourreau.
28 Pa nthawi imeneyo, Davide ataona kuti Yehova wamuyankha pa malo opunthira tirigu a Arauna Myebusi, anapereka nsembe pamenepo.
Aussitôt donc David, voyant que le Seigneur l’avait exaucé dans l’aire d’Ornan, le Jébuséen, immola dans ce lieu des victimes.
29 Tenti ya Yehova imene Mose anapanga mʼchipululu, ndi guwa lansembe zopsereza pa nthawi imeneyi zinali pa phiri ku Gibiyoni.
Mais le tabernacle du Seigneur que Moïse avait fait dans le désert, et l’autel des holocaustes, étaient à cette époque au haut lieu de Gabaon.
30 Koma Davide sanathe kupita kumeneko kuti akapemphere pamaso pa Yehova, chifukwa amaopa lupanga la mngelo wa Yehova.
Et David n’eut pas la force d’aller jusqu’à l’autel pour y prier Dieu, parce qu’il avait été frappé d’une trop grande crainte en voyant le glaive de l’ange du Seigneur.