< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Året efter, ved den tid da kongene pleier å dra ut i krig, tok Joab ut med krigshæren og herjet Ammons barns land, og da han kom til Rabba, kringsatte han det; men David blev i Jerusalem; og Joab tok Rabba og ødela byen.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Og David tok deres konges krone fra hans hode; det viste sig at den veide en talent gull, og der var på den en kostbar sten; nu kom den på Davids hode. Og det store hærfang han hadde tatt i byen, førte han med sig bort.
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Og folket som bodde der, førte han ut og skar dem over med sager og treskesleder av jern eller hugg dem sønder med økser. Så gjorde David med alle Ammons barns byer. Derefter vendte David og alt folket tilbake til Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
Siden kom det til et slag med filistrene ved Geser; da slo husatitten Sibbekai Sippai, som hørte til Rafas barn, og de blev ydmyket.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Så kom det atter til strid med filistrene; og Elhanan, Ja'urs sønn, slo Lahmi, en bror av gittitten Goliat, som hadde et spyd hvis skaft var som en veverstang.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
Ennu en gang kom det til strid ved Gat. Der var en høivoksen mann, som hadde seks fingrer på hver hånd og seks tær på hver fot - i alt fire og tyve fingrer og tær; han var og en efterkommer av Rafa.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
Han hånte Israel; men Jonatan, sønn av Davids bror Simea, hugg ham ned.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
Disse var efterkommere av Rafa i Gat, og de falt for Davids og hans menns hånd.

< 1 Mbiri 20 >