< 1 Mbiri 20 >
1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Or il arriva qu’après le cours d’une année, au temps que les rois ont coutume d’aller à la guerre, Joab assembla l’armée, l’élite de la milice, et ravagea la terre des enfants d’Ammon; puis il alla et assiégea Rabba; mais David demeura à Jérusalem pendant que Joab battit Rabba et la détruisit.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Or David enleva la couronne de la tête de Melchom, et il y trouva un talent d’or pesant et des pierreries très précieuses, et il s’en fit un diadème; il enleva aussi une grande quantité de dépouilles de la ville;
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Mais le peuple, qui y était, il l’en retira, et fit passer sur eux les traîneaux, les herses et les chars armés de fers; en sorte qu’ils fussent coupés en deux et broyés: ainsi fit David à toutes les villes des enfants d’Ammon, et il revint avec tout son peuple à Jérusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
Après cela, on entreprit une guerre à Gazer contre les Philistins, en laquelle Sobochaï de Husathi tua Saphaï de la race des Raphaim, et il les humilia.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
On fit encore contre les Philistins une autre guerre, en laquelle Adéodat, fils de Saltus, Bethléhémite, tua le frère de Goliath, le Géthéen, dont le bois de la lance était comme une ensouple de tisserands.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
Mais, de plus, il arriva une autre guerre à Geth, en laquelle était un homme très grand, qui avait six doigts, c’est-à-dire, en tout vingt-quatre; qui lui-même aussi était sorti de la race de Rapha.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
Celui-ci blasphéma Israël; et Jonathan, fils de Samaa, frère de David, le tua. Ce sont là les enfants de Rapha, à Geth, lesquels tombèrent sous la main de David et de ses serviteurs.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.