< 1 Mbiri 20 >
1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
And it cometh to pass, at the time of the turn of the year — at the time of the going out of the messengers — that Joab leadeth out the force of the host, and destroyeth the land of the sons of Ammon, and cometh in and beseigeth Rabbah — David is abiding in Jerusalem — and Joab smiteth Rabbah, and breaketh it down.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
And David taketh the crown of their king from off his head, and findeth it [in] weight a talent of gold, and in it a precious stone, and it is on the head of David: and spoil of the city he hath brought out very much,
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
and the people who [are] in it he hath brought out, and setteth to the saw, and to cutting instruments of iron, and to axes; and thus doth David to all cities of the sons of Ammon, and David turneth back, and all the people, to Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
And it cometh to pass, after this, that there remaineth war in Gezer with the Philistines, then hath Sibbechai the Hushathite smitten Sippai, of the children of the giant, and they are humbled.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
And there is again war with the Philistines, and Elhanan son of Jair smiteth Lahmi, brother of Goliath the Gittite, the wood of whose spear [is] like a beam of weavers.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
And there is again war in Gath, and there is a man of measure, and his fingers and his toes [are] six and six, twenty and four, and also, he hath been born to the giant.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
And he reproacheth Israel, and smite him doth Jonathan son of Shimea, brother of David.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
These were born to the giant in Gath, and they fall by the hand of David, and by the hand of his servants.