< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Forsothe it was doon after the ende of a yeer, in that tyme wherinne kyngis ben wont to go forth to batels, Joab gederide the oost, and the strengthe of chyualrie, and he wastide the lond of the sones of Amon, and yede, and bisegide Rabath; forsothe Dauid dwellide in Jerusalem, whanne Joab smoot Rabath, and distriede it.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Forsothe Dauid took the coroun of Melchon fro his heed, and foond therynne the weiyt of gold a talent, and moost precious iemmes, and he made therof a diademe to hym silf; also he took ful many spuylis of the citee.
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Sotheli he ledde out the puple that was therynne, and made breris, `ethir instrumentis bi whiche cornes ben brokun, and sleddis, and irone charis, to passe on hem, so that alle men weren kit in to dyuerse partis, and weren al to-brokun; Dauid dide thus to alle the `cytees of the sones of Amon, and turnede ayen with al his puple in to Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
Aftir these thingis a batel was maad in Gazer ayens Filisteis, wherynne Sobochai Vsachites slow Saphai of the kyn of Raphym, and mekide hem.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Also another batel was don ayens Filisteis, in which a man youun of God, the sone of forest, a man of Bethleem, killide Goliath of Geth, the brother of giauntis, of whos schaft the tre was as the beem of webbis.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
But also another batel bifelde in Geth, in which a ful long man was, hauynge sixe fyngris, that is, togidere foure and twenti, and he was gendrid of the generacioun of Raphaym;
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
he blasfemyde Israel, and Jonathan, the sone of Samaa, brother of Dauid, killide hym.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
These ben the sones of Raphaym in Geth, that felden doun in the hond of Dauid and of hise seruauntis.

< 1 Mbiri 20 >