< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
and to be to/for time turn [the] year to/for time to come out: come [the] king and to lead Joab [obj] strength: soldiers [the] army: war and to ruin [obj] land: country/planet son: descendant/people Ammon and to come (in): come and to confine [obj] Rabbah and David to dwell in/on/with Jerusalem and to smite Joab [obj] Rabbah and to overthrow her
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
and to take: take David [obj] crown king their from upon head his and to find her weight talent gold and in/on/with her stone precious and to be upon head David and spoil [the] city to come out: send to multiply much
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
and [obj] [the] people which in/on/with her to come out: send and to saw in/on/with saw and in/on/with incision [the] iron and in/on/with saw and so to make: do David to/for all city son: descendant/people Ammon and to return: return David and all [the] people Jerusalem
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
and to be after so and to stand: rise battle in/on/with Gezer with Philistine then to smite Sibbecai [the] Hushathite [obj] Sippai from born [the] Raphaite and be humble
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
and to be still battle with Philistine and to smite Elhanan son: child (Jair *Q(K)*) [obj] Lahmi brother: male-sibling Goliath [the] Gittite and tree: stake spear his like/as loom-beam to weave
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
and to be still battle in/on/with Gath and to be man `great stature` and finger his six and six twenty and four and also he/she/it to beget to/for [the] Rapha
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
and to taunt [obj] Israel and to smite him Jonathan son: child Shimea brother: male-sibling David
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
these to beget to/for [the] Rapha in/on/with Gath and to fall: kill in/on/with hand: power David and in/on/with hand: power servant/slave his

< 1 Mbiri 20 >