< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Now it happened that, after the course of a year, in the time when kings usually go forth to war, Joab gathered an army with experienced soldiers, and he laid waste to the land of the sons of Ammon. And he continued on and besieged Rabbah. But David was staying in Jerusalem when Joab struck Rabbah and destroyed it.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Then David took the crown of Milcom from his head, and he found in it the weight of one talent of gold, and very precious gems. And he made for himself a diadem from it. Also, he took the best spoils of the city, which were very many.
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Then he led away the people who were in it. And he caused plows, and sleds, and iron chariots to go over them, so much so that they were cut apart and crushed. So did David treat all the cities of the sons of Ammon. And he returned with all his people to Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
After these things, a war was begun at Gezer against the Philistines, in which Sibbecai the Hushathite struck Sippai from the race of the Rephaim, and he humbled them.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Also, another war was undertaken against the Philistines, in which Adeodatus, a son of the forest, a Bethlehemite, struck the brother of Goliath the Gittite, the wood of whose spear was like a weaver’s beam.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
Then too, another war occurred in Gath, in which there was a very tall man, having six digits, that is, all together twenty-four. This man too was born from the stock of the Rephaim.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
He blasphemed Israel. And Jonathan, the son of Shimea, the brother of David, struck him down.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
These were the sons of the Rephaim in Gath, who fell by the hand of David and his servants.

< 1 Mbiri 20 >