< 1 Mbiri 20 >

1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Næste År, ved den Tid Kongerne drager i Krig, førte Joab Krigshæren ud og hærgede Ammoniternes Land; derpå drog han hen og belejrede Rabba. David blev derimod selv i Jerusalem. Og Joab indtog Rabba og ødelagde det.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Da tog David Kronen af Milkoms Hoved, og han fandt, at den var af Guld og vejede en Talent; der var en Ædelsten på den, og den blev sat på Davids Hoved. Et vældigt Bytte fra Byen førte han med sig,
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
og Indbyggerne slæbte han bort og satte dem til Savene, Jernhakkerne og Økserne. Således gjorde han ved alle Ammonifemes Byer. Derpå vendte David og hele Hæren tilbage til Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
Siden hen kom det atter til Kamp med Filisterne i Gezer. Husjatiten Sibbekaj nedhuggede da Sippaj, som var af Rafaslægten, og de blev underkuet.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Atter kom det til Kamp med Filis, terne. Elhanan, Ja'irs Søn, nedhuggede da Lami, Gatiten Goliats Broder, hvis Spydstage var som en Væverbom.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
Atter kom det til Kamp i Gat. Da var der en kæmpe stor Mand med seks Fingre på hver Hånd og seks Tæer på hver Fod, i alt fire og tyve; han var også af Rafaslægten.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
Han hånede Israel, og derfor huggede Jonatan, en Søn af Davids Broder Sjim'a, ham ned.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
Disse var af Rafaslægten i Gat; de faldt for Davids og hans Mænds Hånd.

< 1 Mbiri 20 >