< 1 Mbiri 20 >
1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Yowabu anatsogolera gulu la ankhondo. Iye anawononga Aamoni, kenaka anapita ku mzinda wa Raba ndipo anawuzungulira, koma Davide anatsala ku Yerusalemu. Yowabu anathira nkhondo mzinda wa Raba ndipo anawuwononga.
Og det skete paa den Tid, der Aaret var omme, paa den Tid Kongerne pleje at uddrage til Krig, da førte Joab Stridshæren ud og ødelagde Ammons Børns Land, og han kom og belejrede Rabba, men David blev i Jerusalem; og Joab slog Rabba og nedbrød den.
2 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Ndipo Davide anavala chipewacho. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Og David tog deres Konges Krone fra hans Hoved og fandt, at dens Vægt var et Centner Guld, og der var kostbare Stene i den, og den kom over Davids Hoved; og han bortførte af Staden saare meget Bytte.
3 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka Davide pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Men Folket, som var derudi, førte han ud, og han skar dem over med Save og med Jerntærskeslæder og med Knive, og saaledes gjorde David ved alle Ammons Børns Stæder; siden vendte David og alt Folket tilbage til Jerusalem.
4 Patapita nthawi, nkhondo inayambika pakati pa Aisraeli ndi Afilisti ku Gezeri. Nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Sipai, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai, ndipo Afilisti anagonja.
Og det skete derefter, at der stod et Slag i Geser med Filisterne; da slog Husathiten, Sibekaj, Sifaj af Rafas Børn, og de bleve ydmygede.
5 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti, Elihanani mwana wa Yairi anapha Lahimi mʼbale wake wa Goliati Mgiti, amene mkondo wake unali ngati ndodo yowombera nsalu.
Og der var endnu en Krig med Filisterne; og Elhanan, Jairs Søn, slog Lahemi, Goliaths, Githitens, Broder, hvis Spydstage var som en Væverstang.
6 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati, panali munthu wina wamtali kwambiri, wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
Og der var endnu Krig i Gat, og der var en høj Mand, og han havde seks Fingre paa hver Haand og seks Tæer paa hver Fod, i alt fire og tyve, og han var ogsaa født for Rafa.
7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
Og der han forhaanede Israel, da slog Jonathan, en Søn af Davids Broder Simea, ham ihjel.
8 Anthu amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
Disse vare fødte for Rafa i Gat, og de faldt ved Davids Haand og ved hans Tjeneres Haand.