< 1 Mbiri 2 >

1 Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
La ngamadodana kaIsrayeli: ORubeni, uSimeyoni, uLevi, loJuda, uIsakari, loZebuluni,
2 Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
uDani, uJosefa, loBhenjamini, uNafithali, uGadi, loAsheri.
3 Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
Amadodana kaJuda: OEri loOnani loShela; amathathu wawazalelwa yindodakazi kaShuwa umKhananikazi. Kodwa uEri izibulo likaJuda wayemubi emehlweni eNkosi; yasimbulala.
4 Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
UTamari, umalokozana wakhe, wasemzalela uPerezi loZera. Wonke amadodana kaJuda ayemahlanu.
5 Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
Amadodana kaPerezi: OHezironi loHamuli.
6 Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
Njalo amadodana kaZera: OZimri loEthani loHemani loKalikoli loDara; wonke ayemahlanu.
7 Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
Njalo amadodana kaKarimi: UAkari, umhluphi kaIsrayeli, owenza isiphambeko ngokuqalekisiweyo.
8 Mwana wa Etani anali Azariya.
Njalo amadodana kaEthani: UAzariya.
9 Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
Njalo amadodana kaHezironi awazalelwayo: OJerameli loRamu loKalebi.
10 Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
URamu wasezala uAminadaba; uAminadaba wasezala uNahishoni induna yabantwana bakoJuda.
11 Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
UNahishoni wasezala uSalima; uSalima wasezala uBhowazi;
12 Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
uBhowazi wasezala uObedi; uObedi wasezala uJese.
13 Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
UJese wasezala izibulo lakhe uEliyabi, loAbinadaba owesibili, loShimeya owesithathu,
14 wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
uNethaneli owesine, uRadayi owesihlanu,
15 wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
uOzema owesithupha, uDavida owesikhombisa.
16 Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
Odadewabo babengoZeruya loAbigayili. Lamadodana kaZeruya: OAbishayi loJowabi loAsaheli; abathathu.
17 Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
UAbigayili wasezala uAmasa; loyise kaAmasa wayenguJetheri umIshmayeli.
18 Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
UKalebi indodana kaHezironi wasezala kuAzuba umkakhe lakuJeriyothi; lala ngamadodana akhe: OJesheri loShobabi loAridoni.
19 Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
UAzuba esefile uKalebi wazithathela uEfrathi owamzalela uHuri.
20 Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
UHuri wasezala uUri; uUri wasezala uBhezaleli.
21 Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
Emva kwalokho uHezironi wasengena kundodakazi kaMakiri uyise kaGileyadi; wayithatha eseleminyaka engamatshumi ayisithupha. Yasimzalela uSegubi.
22 Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
USegubi wasezala uJayiri owayelemizi engamatshumi amabili lantathu elizweni leGileyadi.
23 (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
Wasethatha kibo iGeshuri leAramu kanye lemizana yeJayiri, kanye leKenathi lemizana yayo; imizi engamatshumi ayisithupha. Bonke labo babengamadodana kaMakiri uyise kaGileyadi.
24 Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
Lemva kokufa kukaHezironi eKalebi-Efratha, uAbhiya umkaHezironi wamzalela uAshuri uyise kaThekhowa.
25 Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
Njalo amadodana kaJerameli izibulo likaHezironi ayengoRamu izibulo, loBuna, loOreni, loOzema, uAhiya.
26 Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
UJerameli laye wayelomunye umfazi obizo lakhe lalinguAthara; wayengunina kaOnama.
27 Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
Njalo amadodana kaRamu izibulo likaJerameli ayengoMahazi loJamini loEkeri.
28 Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
Lamadodana kaOnama ayengoShamayi loJada. Lamadodana kaShamayi: ONadabi loAbhishuri.
29 Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
Lebizo lomkaAbhishuri lalinguAbihayili, owamzalela oAhibani loMolidi.
30 Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
Njalo amadodana kaNadabi: OSeledi loAphayimi; kodwa uSeledi wafa engelabantwana.
31 Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
Njalo amadodana kaAphayimi: UIshi. Lamadodana kaIshi: USheshani. Lamadodana kaSheshani: UAhilayi.
32 Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
Njalo amadodana kaJada umfowabo kaShamayi: OJetheri loJonathani; kodwa uJetheri wafa engelabantwana.
33 Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
Njalo amadodana kaJonathani: OPelethi loZaza. Laba babengabantwana bakaJerameli.
34 Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
Njalo uSheshani wayengelamadodana, kodwa amadodakazi; njalo uSheshani wayelenceku, umGibhithe, obizo layo lalinguJariha.
35 Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
USheshani wasenika uJariha inceku yakhe indodakazi yakhe yaba ngumkakhe; yasimzalela uAthayi.
36 Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
UAthayi wasezala uNathani, uNathani wasezala uZabadi,
37 Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
uZabadi wasezala uEfilali, uEfilali wasezala uObedi,
38 Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
uObedi wasezala uJehu, uJehu wasezala uAzariya,
39 Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
uAzariya wasezala uHelezi, uHelezi wasezala uEleyasa,
40 Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
uEleyasa wasezala uSisimayi, uSisimayi wasezala uShaluma,
41 Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
uShaluma wasezala uJekamiya, uJekamiya wasezala uElishama.
42 Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
Njalo amadodana kaKalebi umfowabo kaJerameli: OMesha, izibulo lakhe, onguyise kaZifi, lamadodana kaMaresha uyise kaHebroni.
43 Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
Njalo amadodana kaHebroni: OKora loTapuwa loRekemi loShema.
44 Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
UShema wasezala uRahama uyise kaJorikeyamu; uRekemi wasezala uShamayi.
45 Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
Lendodana kaShamayi: UMawoni; loMawoni wayenguyise kaBeti-Zuri.
46 Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
UEfa umfazi omncinyane kaKalebi wasezala oHarani loMoza loGazezi; uHarani wasezala uGazezi.
47 Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
Njalo amadodana kaJahidayi: ORegema loJothamu loGeshani loPeleti loEfa loShahafi.
48 Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
UMahaka umfazi omncinyane kaKalebi wazala oSheberi loTirihana.
49 Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
Wasezala uShahafi uyise kaMadimana, uSheva uyise kaMakibena, loyise kaGibeya. Lendodakazi kaKalebi yayinguAkisa.
50 Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
Laba babengabantwana bakaKalebi, indodana kaHuri, izibulo likaEfratha: OShobhali, uyise kaKiriyathi-Jeyarimi,
51 Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
uSalima uyise kaBhethelehema, uHarefi uyise kaBeti-Gaderi.
52 Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
UShobhali uyise kaKiriyathi-Jeyarimi wayelamadodana: UHarowe, ingxenye yamaMenuhothi.
53 ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
Njalo insendo zikaKiriyathi-Jeyarimi: AmaIthiri lamaPuti lamaShumathi lamaMishrayi; kwaphuma kuwo amaZorathi lamaEshitawoli.
54 Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
Amadodana kaSalima: OBhethelehema, lamaNetofa, uAtarothi, uBeti-Jowabi, lengxenye yamaManahethi, amaZori.
55 ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.
Lensendo zababhali ababehlala eJabezi, amaTirathi, amaShimeyathi, amaSukathi. Labo babengamaKeni avela kuHamathi uyise wendlu kaRekabi.

< 1 Mbiri 2 >