< 1 Mbiri 2 >
1 Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
The sons of Jacob were Reuben, Simeon, Levi, Judah, Issachar, Zebulun,
2 Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
Dan, Joseph, Benjamin, Naphtali, Gad, and Asher.
3 Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
Judah’s sons were Er, Onan, and Shelah. Their mother was the daughter of Shua from the Canaan people-group. [When] Judah’s oldest son Er [grew up, he] did something that Yahweh considered to be very wicked, so Yahweh caused him to die.
4 Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
Judah and his daughter-in-law Tamar had [twin boys named] Perez and Zerah. So altogether Judah had five sons.
5 Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
The sons of Perez were Hezron and Hamul.
6 Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
Zerah had five sons: Zimri, Ethan, Heman, Calcol, and Darda (OR, Dara).
7 Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
[One of the sons of Zimri was Carmi]. Carmi’s son Achan (OR, Achar) caused the people of Israel to experience much trouble, because he stole some of the things that had been devoted [to Yahweh to be destroyed].
8 Mwana wa Etani anali Azariya.
Ethan’s son was Azariah.
9 Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
Hezron’s sons were Jerahmeel, Ram, and Caleb (OR, Chelubai).
10 Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
Ram was the father of Amminadab, and Amminadab was the father of Nahshon. Nahshon was a leader of the tribe of Judah.
11 Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
Nahshon was the father of Salmon, who was the father of Boaz.
12 Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
Boaz was the father of Obed, and Obed was the father of Jesse.
13 Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
Jesse’s oldest son was Eliab. His other sons were Abinadab, Shimea,
14 wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
Nethanel, Raddai,
15 wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
Ozem, and the youngest was David.
16 Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
Their sisters were Zeruiah and Abigail. Zeruiah’s three sons were Abishai, Joab, and Asahel.
17 Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
Abigail’s husband was Jether, a descendant of Ishmael, and their son was Amasa.
18 Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
Hezron’s younger son Caleb had two wives. One of them, Azubah, gave birth to [three] sons: Jesher, Shobab, and Ardon.
19 Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
When Azubah died, Caleb married Ephrath. Their son was Hur.
20 Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
Hur was the father of Uri, and Uri was the father of Bezalel.
21 Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
When Hezron was 60 years old, he married [EUP] Makir’s daughter, who was the sister of Gilead. The son of Hezron and Makir was Segub.
22 Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
Segub was the father of Jair. Jair’s [army] controlled twenty-three cities in the region ruled by Gilead.
23 (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
But [the armies of] Geshur and Aram captured those towns controlled by Jair. They also captured Kenath [city] and the nearby towns; altogether they captured 60 towns. The people who lived there were all descendants of Makir, the father of Gilead.
24 Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
Shortly after Hezron died in Caleb-Ephrath [town], his widow Abijah had a son Asshur; Asshur started Tekoa [town].
25 Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
Hezron’s oldest son was Jerahmeel. His sons were Ram, Bunah, Oren, Ozem, and Ahijah. Jerahmeel’s oldest son was Ram.
26 Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
Jerahmeel had another wife named Atarah. Their son was Onam.
27 Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
The sons of Ram, Jerahmeel’s oldest son, were Maaz, Jamin, and Eker.
28 Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
Onam’s sons were Shammai and Jada. Shammai’s sons were Nadab and Abishur.
29 Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
Abishur’s wife was Abihail. The sons of Abishur and Abihail were Ahban and Molid.
30 Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
Nadab’s sons were Seled and Appaim. Seled did not have any children.
31 Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
Appaim’s son was Ishi; Ishi’s son was Sheshan. One of Sheshan’s daughters was Ahlai.
32 Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
Shammai’s [younger] brother was Jada. Jada’s sons were Jether and Jonathan. Jether did not have any children.
33 Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
Jonathan’s sons were Peleth and Zaza. Those were the descendants of Jerahmeel.
34 Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
Sheshan did not have any sons; he had only daughters. He had a servant from Egypt whose name was Jarha.
35 Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
Sheshan allowed his daughter to marry Jarha, and their son was Attai.
36 Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
Attai was the father of Nathan. Nathan was the father of Zabad.
37 Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
Zabad was the father of Ephlal. Ephlal was the father of Obed.
38 Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
Obed was the father of Jehu. Jehu was the father of Azariah.
39 Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
Azariah was the father of Helez. Helez was the father of Eleasah.
40 Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
Eleasah was the father of Sismai. Sismai was the father of Shallum.
41 Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
Shallum was the father of Jekamiah. And Jekamiah was the father of Elishama.
42 Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
Jerahmeel’s [younger] brother was Caleb. Caleb’s oldest son was Mesha. Mesha was the father of Ziph. Ziph was the father of Mareshah. Mareshah was the father of Hebron.
43 Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
Hebron’s sons were Korah, Tappuah, Rekem, and Shema.
44 Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
Shema was the father of Raham. Raham was the father of Jorkeam. Rekem was the father of Shammai.
45 Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
Shammai was the father of Maon. Maon was the father of Beth-Zur.
46 Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
Caleb had a slave wife who was named Ephah. Caleb and Ephah’s sons were Haran, Moza, and Gazez. Haran had a son whom he also named Gazez.
47 Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
Ephah’s father was Jahdai. Jahdai was the father of [six sons: ] Regem, Jotham, Geshan, Pelet, Ephah, and Shaaph.
48 Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
Caleb had another slave wife whose name was Maacah. Caleb and Maacah’s sons were Sheber, Tirhanah,
49 Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
Shaaph, and Sheva. Shaaph was the father of Madmannah. Sheva was the father of Macbenah and Gibea. Caleb’s daughter was Acsah.
50 Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
These people were also descendants of Caleb: [Caleb had another wife whose name was] Ephrathah. Their oldest son was Hur. Hur’s sons were Shobal, Salma, and Hareph. Shobal started Kiriath-Jearim [city]. Salma started Bethlehem [town]. Hareph started Beth-Gader [town].
51 Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
Shobal’s descendants were Haroeh, and half of the Manahath people-group.
53 ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
His descendants also included these clans that lived in Kiriath-Jearim: Ithri, Put, Shumath, and Mishra. The Zorath and Eshtaol clans were descendants of the Mishra clan.
54 Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
Salma’s descendants in Bethlehem were the Netophath clan, the Atroth-Beth-Joab clan, the other half of the Manahath clan, and the Zor clan.
55 ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.
Salma’s descendants also included the families at Jabez [town] who wrote and copied important documents. These were the Tirath clan, the Shimeath clan, and the Sucath clan. They were all from the Ken people-group who came from Hammath [city], and who had married members of the family [MTY] of Rechab.