< 1 Mbiri 2 >

1 Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
Tito jsou synové Izraelovi: Ruben, Simeon, Léví, Juda, Izachar a Zabulon,
2 Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
Dan, Jozef, Beniamin, Neftalím, Gád a Asser.
3 Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
Synové Judovi: Her, Onan a Séla. Ti tři narodili se jemu z dcery Suovy Kananejské. Ale Her, prvorozený Judův, byl zlý před očima Hospodinovýma, protož zabil ho.
4 Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
Támar pak nevěsta jeho porodila mu Fáresa a Záru. Všech synů Judových pět.
5 Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
Synové Fáresovi: Ezron a Hamul.
6 Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
Synové pak Záre: Zamri, Etan, Héman, Kalkol a Dára, všech těch pět.
7 Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
A synové Zamri: Charmi, vnuk Achar, kterýž zkormoutil Izraele, zhřešiv při věci proklaté.
8 Mwana wa Etani anali Azariya.
Synové pak Etanovi: Azariáš.
9 Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
Synové pak Ezronovi, kteříž se mu zrodili: Jerachmeel, Ram a Chelubai.
10 Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
Ram pak zplodil Aminadaba, a Aminadab zplodil Názona, kníže synů Juda.
11 Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
Názon pak zplodil Salmona, a Salmon zplodil Bóza.
12 Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
A Bóz zplodil Obéda, a Obéd zplodil Izai.
13 Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
Izai pak zplodil prvorozeného svého Eliaba, a Abinadaba druhého, a Sammu třetího,
14 wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
Natanaele čtvrtého, Raddaia pátého,
15 wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
Ozema šestého, Davida sedmého,
16 Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
A sestry jejich: Sarvii a Abigail. Synové pak Sarvie byli: Abizai, Joáb, Azael, tři.
17 Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
Abigail pak porodila Amazu, otec pak Amazův byl Jeter Izmaelitský.
18 Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
Kálef pak syn Ezronův zplodil s Azubou manželkou a s Jeriotou syny. Jehož tito synové byli: Jeser, Sobab a Ardon.
19 Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
Když pak umřela Azuba, pojal sobě Kálef Efratu, kteráž mu porodila Hura.
20 Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
A Hur zplodil Uri, a Uri zplodil Bezeleele.
21 Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
Potom všel Ezron k dceři Machira otce Galádova, kterouž on pojal, když byl v šedesáti letech. I porodila jemu Seguba.
22 Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
Segub pak zplodil Jaira, kterýž měl třimecítma měst v zemi Galád.
23 (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
Nebo vzal Gessurejským a Assyrským vsi Jairovy, i Kanat s městečky jeho, šedesáte měst. To všecko pobrali synové Machirovi, otce Galádova.
24 Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
Též i po smrti Ezronově, když již pojal byl Kálef Efratu, manželka Ezronova Abia porodila jemu také Ashura, otce Tekoa.
25 Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
Byli pak synové Jerachmeele prvorozeného Ezronova: Prvorozený Ram, po něm Buna a Oren, a Ozem s Achia.
26 Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
Měl také manželku druhou Jerachmeel, jménem Atara. Ta jest matka Onamova.
27 Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
Byli pak synové Ramovi prvorozeného Jerachmeele: Maaz a Jamin a Eker.
28 Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
Též synové Onamovi byli: Sammai a Jáda. A synové Sammai: Nádab a Abisur.
29 Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
Jméno pak manželky Abisurovy Abichail; ktéráž porodila jemu Achbana a Molida.
30 Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
A synové Nádabovi: Seled a Appaim. Ale umřel Seled bez dětí.
31 Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
Synové pak Appaimovi: Jesi; a synové Jesi: Sesan; a dcera Sesanova: Achlai.
32 Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
Synové pak Jády, bratra Sammaiova: Jeter a Jonatan. Ale umřel Jeter bez dětí.
33 Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
Synové pak Jonatanovi: Felet a Záza. Ti byli synové Jerachmeelovi.
34 Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
Neměl pak Sesan synů, ale dceru. A měl Sesan služebníka Egyptského jménem Jarchu.
35 Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
Protož dal Sesan dceru svou Jarchovi služebníku svému za manželku, kteráž porodila mu Attaie.
36 Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
Attai pak zplodil Nátana, a Nátan zplodil Zabada.
37 Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
Zabad pak zplodil Eflale, a Eflal zplodil Obéda.
38 Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
Obéd pak zplodil Jéhu, a Jéhu zplodil Azariáše.
39 Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
Azariáš pak zplodil Cheleza, a Chelez zplodil Elasu.
40 Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
Elasa pak zplodil Sismaie, a Sismai zplodil Salluma.
41 Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
Sallum pak zplodil Jekamiáše, a Jekamiáš zplodil Elisama.
42 Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
Synové pak Kálefa, bratra Jerachmeelova: Mésa prvorozený jeho. On byl otec Zifejských i synů Marese, otce Hebronova.
43 Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
Synové pak Hebronovi: Chóre a Tapuach, a Rekem a Sema.
44 Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
Sema pak zplodil Rachama otce Jorkeamova, a Rekem zplodil Sammaie.
45 Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
Syn pak Sammai byl Maon; kterýžto Maon byl otec Betsurských.
46 Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
Efa také, ženina Kálefova, porodila Chárana a Mozu a Gazeza. A Cháran zplodil Gazeza.
47 Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
Synové pak Johedai: Regem, Jotam, Gesan, Felet, Efa a Saaf.
48 Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
S ženinou Maachou Kálef zplodil Sebera a Tirchana.
49 Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
Porodila pak Saafa otce Madmanejských, Sévu otce Makbenejských a otce Gibejských. Též dcera Kálefova Axa.
50 Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
Ti byli synové Kálefovi, syna Hur prvorozeného Efraty: Sobal otec Kariatjeharimských,
51 Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
Salma otec Betlémských, Charef otec čeledi Betgaderských.
52 Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
Měl pak syny Sobal otec Kariatjeharimských: Haroe otce obyvatelů dílu Menuchotských.
53 ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
A čeledi Kariatjeharimských, Jeterských, Putských, Sumatských a Misraiských. Z těch pošli Zaratští a Estaolští.
54 Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
Synové Salmy: Betlémští, Netofatští, Atarotští z čeledi Joábovy, a Zarští, kteříž užívali dílu Menuchotských,
55 ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.
A čeledi písařů obývajících v Jábezu, Tiratských, Simatských, Suchatských. Ti jsou Cinejští příchozí z Amata, otce čeledi Rechabovy.

< 1 Mbiri 2 >