< 1 Mbiri 19 >
1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
MAHOPE mai o ia mea, make iho la o Nahasa ke alii o na mamo a Amona, a nohoalii iho la o Hanuna ma kona wahi.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
Olelo iho la o Davida, E lokomaikai no wau ia Hanuna ke keiki a Nahasa; no ka mea, i lokomaikai mai kona makuakane ia'u. Hoouna aku la o Davida i na elele e hooluolu aku ia ia no kona makuakane. A hiki aku la na elele o Davida i ka aina o na mamo a Amona, io Hanuna la, e hooluolu ia ia.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Aka, o na alii o na mamo a Amona, i aku la lakou ia Hanuna, Ke manao nei anei oe, e hoomaikai mai o Davida i kou makuakane i kona hoouna ana mai iou la i na mea hooluolu? Aole anei i hele mai kana mau kauwa iou nei e makaikai, a e hookahuli, a e hoomakakiu mai i ka aina?
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
Nolaila, lalau mai la o Hanuna i na kauwa a Davida, a kahi ae la i ko lakou umiumi, a okioki iho la i ko lakou mau aahu mawaena, ma ko lakou kikala, a kipaku mai la ia lakou.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Hele mai la kekahi, a hai aku la ia Davida i ka mea i hanaia mai i ua mau kanaka la. Hoouna aku ia ia e halawai me lakou: no ka mea, ua hilahila loa lakou. I aku la ke alii, E noho oukou ma Ieriko, a ulu ae ko oukou umiumi, alaila e hoi mai
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
A ike iho la na mamo a Amona, ua pilau lakou imua o Davida, hoouka aku la o Hanuna me na mamo a Amona i na talena kala he tausani e hoolimalima no lakou i na halekaa a me na hoohololio mai Mesopotamia, a mai Suria-maaka, a mai Zoba mai.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
Hoolimalima ae la lakou i na kaa he kanakolukumamalua tausani, a me ke alii o Maaka, a me kona poe kanaka; a hele mai lakou a hoomoana imua o Medeba. Akoakoa mai la na mamo a Amona mailoko mai o ko lakou mau kulanakauhale, a hele mai i ke kaua.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
A lohe ae la o Davida, hoouna aku la oia ia Ioaba, me ka puali a pau o ka poe ikaika.
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
Hele mai la ka poe mamo a Amona iwaho, a hoonohonoho i ke kaua ma ke alo o ka puka e komo ai iloko o ke kulanakauhale: a ku okoa ae la na alii i hiki mai ma ke kola.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
A ike aku la o Ioaba i ke alo o na kaua, mamua kekahi, a mahope kekahi, wae aku la oia i ka poe ui a pau o ka Iseraela, a hoonohonoho aku la ia lakou e ku e i ko Suria
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
A haawi aku la ia i ka poe i koe ma ka lima o Abisai kona kaikaina, a hoonohonoho aku oia ia lakou e ku e i na mamo a Amona.
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
I aku la oia, Ina e oi aku ka ikaika o ko Suria i ko'u, alaila e kokua mai oe ia'u: aka, ina e oi aku ka ikaika o na mamo a Amona i kou, alaila au e kokua aku ia oe.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
I nui ka ikaika, a e koa hoi kakou no ko kakou lahuikanaka, a me na kulanakauhale no ko kakou Akua: a e hana mai o Iehova i ka mea pono imua o kona maka.
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Neenee aku la o Ioaba me na kanaka me ia imua o ko Suria, i ke kaua ana; a hee aku la lakou imua ona.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
A ike aku la na mamo a Amona, ua hee aku la ko Suria, alaila hee aku la hoi lakou imua o Abisai kona kaikaina, a komo aku la iloko o ke kulanakauhale. Alaila hele mai la o Ioaba i Ierusalema.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
A ike ae la ko Suria, ua pepehiia lakou imua o ka Iseraela, hoouna aku la lakou i na elele, a kai mai la lakou i ko Suria e noho ana ma kela aoao o ka muliwai: a imua o lakou o Sopaka ka lunakoa no Hadarezera.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
A hai aku la kekahi ia Davida: a hoakoakoa ae la oia i ka Iseraela a pau, a hele aku la ma kela aoao o Ioredane, a hiki aku la io lakou la, a hoonohonoho aku la i ke kaua ku e ia lakou. Aia hoonohonoho aku ai o Davida i ke kaua ku e ia lakou, alaila lakou i kaua mai me ia.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
A hee aku la ko Suria imua o ka Iseraela; a pepehi aku la o Davida i na kanaka o na halekaa ehiku tausani, a me na kanaka kaniwawae he kanaha tausani, a make iho la o Sopaka ka lunakaua.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
A ike iho la na kauwa a Hadarezera, ua pepehiia lakou imua o ka Iseraela, hookuikahi mai la lakou me Davida, a lilo iho la i poe kauwa nana Aole hoi i manao ko Suria e kokua hou aku i na mamo a Amona.