< 1 Mbiri 19 >

1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Or il arriva que Naas, roi des enfants d’Ammon, mourut, et que son fils régna à sa place.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
Et David dit: Je ferai miséricorde à Hanon, fils de Naas, parce que son père m’a rendu service. David envoya donc des messagers pour le consoler de la mort de son père. Lorsque ceux-ci furent arrivés dans le pays des enfants d’Ammon, pour consoler Hanon,
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Les princes des enfants d’Ammon dirent à Hanon: Vous, peut-être, vous pensez que David, pour l’honneur de votre père, a envoyé ces messagers, afin de vous consoler; et vous ne remarquez pas que c’est pour explorer, sonder et scruter votre territoire que sont venus vers vous ses serviteurs.
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
Ainsi Hanon rasa la tête et la barbe aux serviteurs de David, coupa leurs tuniques depuis le haut des cuisses jusqu’aux pieds, et les renvoya.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Lorsque ceux-ci s’en furent allés, et qu’ils eurent mandé cela à David, il envoya à leur rencontre (car ils avaient enduré un grand outrage), et il ordonna qu’ils demeurassent à Jéricho, jusqu’à ce que leur barbe eût crû, et qu’alors ils revinssent.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
Or les enfants d’Ammon, voyant que tant Hanon que le reste du peuple avaient fait injure à David, envoyèrent mille talents d’argent, pour se procurer, de la Mésopotamie, de la Syrie de Maacha, et de Soba, des chariots et des cavaliers.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
Ils réunirent donc à eux trente-deux mille chariots, et le roi de Maacha avec son peuple. Lorsqu’ils furent venus vis-à-vis de Médaba, ils campèrent. Les enfants d’Ammon, s’étant aussi assemblés de leurs villes, vinrent au combat.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
Ce qu’ayant appris David, il envoya Joab et toute l’armée des hommes vaillants;
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
Et, étant sortis, les enfants d’Ammon rangèrent leur armée en bataille près de la porte de la ville; mais les rois qui étaient venus à leur secours se tinrent séparément dans la campagne.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
Ainsi Joab, s’apercevant que la guerre se faisait contre lui, et par devant et par derrière, choisit des hommes très braves de tout Israël, et marcha contre les Syriens.
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
Mais le reste du peuple, il le mit sous la main d’Abisaï, son frère; et ils marchèrent contre les enfants d’Ammon;
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
Et il dit: Si les Syriens me vainquent, tu me seras en aide; mais si les enfants d’Ammon l’emportent sur toi, j’irai à ton secours.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Fortifie-toi et agissons courageusement pour notre peuple et pour les villes de notre Dieu, et le Seigneur fera ce qui est bon en sa présence.
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Joab marcha donc, et le peuple qui était avec lui, au combat contre les Syriens, et il les mit en fuite.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
Or les enfants d’Ammon, voyant que les Syriens avaient fui, s’enfuirent, eux aussi, devant Abisaï, son frère, et ils entrèrent dans la ville; et Joab lui-même retourna à Jérusalem.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
Mais les Syriens, voyant qu’ils avaient succombé devant Israël, envoyèrent des messagers, et firent venir les autres Syriens qui étaient au-delà du fleuve: or Sophach, prince de la milice d’Adarézer, était leur chef.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
Lorsque cela eut été annoncé à David, il assembla tout Israël, passa le Jourdain, fondit sur eux et rangea en face son armée en bataille, eux combattant de leur côté.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
Cependant les Syriens s’enfuirent devant Israël, et David tua des Syriens sept mille hommes qui étaient sur les chariots, quarante mille de pied, et Sophach, général de cette armée.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Or les serviteurs d’Adarézer, voyant qu’ils étaient vaincus par Israël, passèrent à David et lui furent assujettis; et la Syrie ne voulut plus donner secours aux enfants d’Ammon

< 1 Mbiri 19 >