< 1 Mbiri 19 >

1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Sur ces entrefaites, Nahach, le roi des Ammonites, mourut, et son fils lui succéda.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
David se dit: "Je veux agir amicalement avec Hanoun, fils de Nahach, comme son père a agi à mon égard." Et David envoya des émissaires pour lui présenter des condoléances au sujet de son père, et les serviteurs de David se rendirent au pays des Ammonites pour porter des condoléances à Hanoun.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Mais les princes ammonites dirent à Hanoun: "Est-ce, à ton avis, pour honorer ton père que David t’a envoyé des consolateurs? N’Est-ce pas plutôt pour explorer, troubler et espionner le pays que ses serviteurs sont venus te trouver?"
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
Alors Hanoun fit saisir les serviteurs de David, ordonna de les raser et de couper la moitié de leurs vêtements jusqu’aux hanches, puis il les congédia.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Ceux-ci partis, on mit David au courant de ce qui était arrivé à ces hommes, et il envoya au-devant d’eux car ces hommes étaient accablés de honte et leur fit dire: "Restez à Jéricho jusqu’à ce que votre barbe ait repoussé, puis vous reviendrez."
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
Les Ammonites, voyant qu’ils s’étaient mis en mauvaise odeur auprès de David, envoyèrent, de concert avec Hanoun, mille kikkar d’argent pour soudoyer dans la Syrie du Double-Fleuve, dans la Syrie de Maakha et de Çoba des chars et des cavaliers.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
Ils soudoyèrent ainsi trente-deux mille chars ainsi que le roi de Maakha et son peuple, qui vinrent camper devant Mèdeba; de leur côté, les Ammonites sortirent ensemble de leurs villes et entrèrent en campagne.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
A cette nouvelle, David envoya Joab avec toute son armée de vaillants.
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
Les Ammonites s’avancèrent et se mirent en bataille à l’entrée de la ville, tandis que les rois qui étaient accourus restaient séparés dans la campagne.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
Joab, voyant que la bataille le menaçait par-devant et par-derrière, fit choix des meilleurs guerriers d’Israël et les disposa devant les Syriens.
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
Pour le reste de l’armée, il le mit sous les ordres de son frère Abchaï et le rangea devant les Ammonites.
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
Et il dit: "Si les Syriens l’emportent sur moi, tu viendras à mon secours; si les Ammonites l’emportent sur toi, c’est moi qui viendrai te secourir.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Sois fort, soyons forts pour notre peuple et pour les villes de notre Dieu, et que le Seigneur agisse selon sa volonté!"
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Joab, avec la troupe qui l’accompagnait, engagea la bataille contre les Syriens, qui s’enfuirent devant lui.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
Les Ammonites, voyant fuir les Syriens, lâchèrent pied devant son frère Abchaï et rentrèrent dans la ville; et Joab revint à Jérusalem.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
Mais les Syriens, se voyant battus par les Israélites, envoyèrent des messagers et firent avancer les Syriens de delà le Fleuve, sous le commandement de Chopakh, chef de l’armée de Hadadézer.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
Quand David en fut informé, il rassembla tout Israël, traversa le Jourdain, arriva à Hélam et aligna ses troupes en face d’eux. Il commença à combattre les Syriens, qui acceptèrent la bataille.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
Aram prit la fuite devant Israël, et David lui tua sept mille attelages et quarante mille hommes de pied. Il fit périr aussi Chopakh, chef de l’armée.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Les serviteurs de Hadadézer, voyant qu’Israël les avait défaits, firent la paix avec David et devinrent ses tributaires; et les Syriens ne furent plus disposés à venir en aide aux Ammonites.

< 1 Mbiri 19 >