< 1 Mbiri 19 >
1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Now it happened that Nahash, the king of the sons of Ammon, died, and his son reigned in his place.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
And David said: “I will act with mercy toward Hanun, the son of Nahash. For his father was gracious to me.” And so David sent messengers to console him over the death of his father. But when they had reached the land of the sons of Ammon, so that they might console Hanun,
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
the leaders of the sons of Ammon said to Hanun: “Do you think that perhaps David has sent them to console you in order to honor your father? Have you not noticed that his servants came to you so that they might explore, and investigate, and examine your land?”
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
And so Hanun shaved the heads and beards of the servants of David, and he cut away their tunics from the buttocks to the feet, and he sent them away.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
And when they had gone, and had sent word to David, (for they had suffered a great disgrace, ) he sent to meet them, and he instructed them that they should remain at Jericho until their beards grew, and then they should return.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
Then, when the sons of Ammon realized that they had committed an injury against David, both Hanun and the rest of the people sent one thousand talents of silver, so that they might hire for themselves chariots and horsemen from Mesopotamia, and from Syrian Maacah, and from Zobah.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
And they hired thirty-two thousand chariots, and the king of Maacah with his people. When these had arrived, they made camp in the region opposite Medeba. Also, the sons of Ammon, gathering from their cities, went to war.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
And when David had heard this, he sent Joab and the entire army of strong men.
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
And the sons of Ammon, going out, set up a battle line before the gate of the city. But the kings who had come to their aid stood separately in the field.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
And so Joab, understanding the war to be set facing him and behind his back, chose the strongest men from all of Israel, and he went out against the Syrians.
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
But the remaining portion of the people he placed under the hand of his brother Abishai. And they went out against the sons of Ammon.
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
And he said: “If the Syrians prevail over me, then you shall be a help to me. But if the sons of Ammon prevail over you, I will be a safeguard for you.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Be strengthened, and let us act manfully on behalf of our people, and on behalf of the cities of our God. And the Lord will do what is good in his own sight.”
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Therefore, Joab, and the people who were with him, went out to battle against the Syrians. And he put them to flight.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
Then the sons of Ammon, seeing that the Syrians had fled, also themselves fled from Abishai, his brother, and they entered into the city. And now Joab returned to Jerusalem.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
But the Syrians, seeing that they had fallen before Israel, sent messengers, and they brought the Syrians who were across the river. And Shophach, the leader of the military of Hadadezer, was their commander.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
When this had been reported to David, he gathered together all of Israel, and he crossed the Jordan. And he rushed toward them. And he set up a battle line facing them. And they fought against him.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
But the Syrians fled from Israel. And David killed of the Syrians seven thousand chariots, and forty thousand men on foot, and Shophach, the leader of the army.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Then the servants of Hadadezer, seeing themselves to be overwhelmed by Israel, crossed over to David, and they served him. And Syria was no longer willing to offer aid to the sons of Ammon.