< 1 Mbiri 19 >

1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Stalo se zatím, že umřel Náhas král Ammonitský, a kraloval syn jeho místo něho.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
I řekl David: Učiním milosrdenství s Chanunem synem Náhasovým, nebo učinil otec jeho milosrdenství nade mnou. Tedy poslal David posly, aby ho potěšili pro otce jeho. I přišli služebníci Davidovi do země synů Ammon k Chanunovi, aby ho těšili.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Tedy řekla knížata Ammonitská Chanunovi: Cožť se zdá, že David činí poctivost otci tvému, že poslal k tobě, kteříž by tě potěšili? Zdali ne proto, aby shlédli a vyšpehovali, i podvrátili zemi tuto, přišli služebníci jeho k tobě?
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
Pročež Chanun vzav služebníky Davidovy, oholil je a zustřihoval roucha jejich polovici až do rozkroků, a propustil je.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Tedy odešli někteří, a oznámili Davidovi o těch mužích. I poslal proti nim, (nebo byli muži ti zlehčeni velice), a rozkázal jim král: Pobuďte v Jerichu, dokudž neobrostou brady vaše; potom se navrátíte.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
Vidouce pak Ammonitští, že se zošklivili Davidovi, poslal Chanun a synové Ammon tisíc hřiven stříbra, aby sobě najali ze mzdy z Mezopotamie a z Syrie Maacha a z Soba vozů a jezdců.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
A najali sobě ze mzdy třidceti a dva tisíce vozů, a krále Maachu i lid jeho. Kteřížto přitáhše, položili se s vojskem naproti Medaba. Ammonitští také shromáždivše se z měst svých, přitáhli k té bitvě.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
Což uslyšav David, poslal Joába se vším vojskem udatných.
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
A tak vytáhše Ammonitští, sšikovali se k boji u brány města toho. Králové pak, kteříž byli přitáhli, byli zvláště na poli.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
A protož vida Joáb proti sobě sšikovaný lid z předu i z zadu, vybrav některé ze všech výborných Izraelských, sšikoval je také proti Syrským.
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
Ostatek pak lidu dal pod správu Abizaie bratra svého, a sšikovali se proti Ammonitským.
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
I řekl Joáb: Jestliže Syrští budou mne silnější, přispěješ mi na pomoc; pakli Ammonitští silnější budou tebe, já pomohu tobě.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Posiliž se, a zmužile se mějme, bojujíce za lid náš a za města Boha našeho, Hospodin však, což mu se dobře líbí, nechť učiní.
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Takž přistoupil Joáb i lid, kterýž při něm byl, k bitvě proti Syrským. Ale oni utekli před ním.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
V tom Ammonitští vidouce, že utíkají Syrští, utekli také i oni před Abizaiem bratrem jeho, a ušli do města. Joáb též navrátil se do Jeruzaléma.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
A tak vidouce Syrští, že jsou poraženi od Izraelských, poslali posly, a vyvedli Syrské, kteříž bydlejí za řekou, a Sofach kníže vojska Hadarezerova vedl je.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
I oznámeno to Davidovi. Kterýžto shromáždiv všecken lid Izraelský, přepravil se přes Jordán, a přitáhl k nim, a sšikoval vojsko proti nim. A když sšikoval David vojsko proti Syrským k bitvě, bojovali s ním.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
Tedy utekli Syrští před Izraelem. I porazil David z Syrských sedm tisíc vozů, a čtyřidceti tisíc lidu pěšího, až i Sofacha hejtmana vojska toho zabil.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Pročež když viděli služebníci Hadarezerovi, že jsou poraženi od Izraele, vešli v pokoj s Davidem, a sloužili jemu. A nechtěli více Syrští táhnouti na pomoc Ammonitským.

< 1 Mbiri 19 >